< Yoswa 7 >

1 Koma Aisraeli anachita zachinyengo ndi lamulo lija loti asatenge kalikonse koyenera kuwonongedwa. Akani mwana wa Karimi, mwana wa Zabidi, mwana wa Zera, wa fuko la Yuda anatengako zinthu zina. Choncho Yehova anakwiyira Israeli kwambiri.
But the sons of Israel committed a trespass in what was set apart. For Achan, the son of Carmi, the son of Zabdi, the son of Zerah, of the tribe of Judah, took from what was set apart, and the anger of Jehovah was kindled against the sons of Israel.
2 Tsono Yoswa anatuma anthu kuchokera ku Yeriko kukazonda ku mzinda wa Ai umene uli pafupi ndi mzinda wa Beti-Aveni kummawa kwa Beteli, ndipo anawawuza kuti, “Pitani mukazonde chigawochi.” Anthuwo anapitadi kukazonda Ai.
And Joshua sent men from Jericho to Ai, which is beside Beth-aven, on the east side of Bethel, and spoke to them, saying, Go up and spy out the land. And the men went up and spied out Ai.
3 Atabwera kwa Yoswa, anamuwuza kuti, “Sikofunika kuti apite anthu onse kukathira nkhondo mzinda wa Ai. Mutumizeko anthu 2,000 kapena 3,000 kuti akatenge mzindawo. Musawatume anthu onse kumeneko popeza kuli anthu ochepa.”
And they returned to Joshua, and said to him, Let not all the people go up, but let about two or three thousand men go up and smite Ai. Do not make all the people to toil there, for they are but few.
4 Choncho kunapita anthu 3,000. Koma iwo anathamangitsidwa ndi anthu a ku Ai.
So there went up there of the people about three thousand men. And they fled before the men of Ai.
5 Anthu a ku Ai anathamangitsa Aisraeli kuchokera pa chipata cha mzindawo mpaka ku ngwenya ndipo anapha anthu 36. Iwowa anawapha pamene ankatsika phiri. Choncho mitima ya anthu inasweka ndipo analibenso mphamvu.
And the men of Ai smote of them about thirty-six men. And they chased them from before the gate even to Shebarim, and smote them at the descent. And the hearts of the people melted, and became as water.
6 Tsono Yoswa anangʼamba zovala zake nagwada nʼkuweramitsa mutu wake pansi patsogolo pa Bokosi la Yehova. Akuluakulu a Israeli nawonso anadzigwetsa pansi ndipo anakhala pomwepo mpaka madzulo atadziwaza fumbi kumutu kwawo.
And Joshua tore his clothes, and fell to the earth upon his face before the ark of Jehovah until the evening, he and the elders of Israel, and they put dust upon their heads.
7 Ndipo Yoswa anati, “Kalanga ine, Ambuye Wamphamvuzonse chifukwa chiyani munatiwolotsa Yorodani? Kodi mumalinga zotipereka mʼmanja mwa Aamori kuti atiwononge chotere? Kukanakhala kwabwino ife tikanakhala tsidya linalo la Yorodani!
And Joshua said, Alas, O lord Jehovah, why have thou at all brought this people over the Jordan, to deliver us into the hand of the Amorites, to cause us to perish? Would that we had been content and dwelt beyond the Jordan!
8 Tsono Ambuye, ine ndinene chiyani, pakuti tsopano Israeli anathamangitsidwa ndi adani ake?
Oh, Lord, what shall I say after Israel has turned their backs before their enemies!
9 Akanaani ndi anthu ena a dziko lino adzamva zimenezi ndipo adzatizinga ndi kutiwonongeratu. Nanga inu mudzatani ndi dzina lanu lamphamvulo?”
For the Canaanites and all the inhabitants of the land will hear of it, and will encompass us around, and cut off our name from the earth, and what will thou do for thy great name?
10 Koma Yehova anati kwa Yoswa, “Imirira! Chifukwa chiyani wagwada pansi chotere?
And Jehovah said to Joshua, Get thee up. Why are thou thus fallen upon thy face?
11 Aisraeli achimwa. Iwo aphwanya pangano limene ndinawalamula kuti asunge. Anatengako zinthu zina zofunika kuwonongedwa. Choncho anabako, ananena bodza ndi kuyika zinthu zakubazo pamodzi ndi katundu wawo.
Israel has sinned. Yes, they have even transgressed my covenant which I commanded them. Yes, they have even taken from what was set apart, and have also stolen, and also dissembled. And they have even put it among their own stuff.
12 Nʼchifukwa chake Aisraeli sangathe kulimbana ndi adani awo. Iwo anathawa pamaso pa adani awo chifukwa ndiwo oyenera kuwonongedwa. Ine sindikhalanso ndi inu pokhapokha mutawononga chilichonse choyenera kuwonongedwa pakati panu.
Therefore the sons of Israel cannot stand before their enemies. They turn their backs before their enemies because they have become accursed. I will not be with you any more unless ye destroy what was set apart from among you.
13 “Nyamuka, ukawawuze anthu kuti, ‘Mudzipatule nokha kukonzekera kuonana nane mawa; pakuti Yehova Mulungu wa Israeli akuti choyenera kuwonongedwa chija chili pakati panu, inu Aisraeli. Simungathe kulimbana ndi adani anu mpaka mutachichotsa.’
Up, sanctify the people, and say, Sanctify yourselves against tomorrow. For thus says Jehovah, the God of Israel, There is what has been set apart in the midst of thee, O Israel. Thou cannot stand before thine enemies until ye take away the devoted thing from among you.
14 “Mawa mmamawa adzabwere pamaso pa Yehova fuko limodzilimodzi. Fuko limene Yehova adzaliloze lidzabwere patsogolo mbumba imodziimodzi. Tsono mbumba imene Yehova adzayiloze idzabwere patsogolo banja limodzilimodzi. Banja limene Yehova adzaliloze lidzabwere patsogolo munthu mmodzimmodzi.
In the morning therefore ye shall be brought near by your tribes, and it shall be, that the tribe which Jehovah takes shall come near by families, and the family which Jehovah shall take shall come near by households, and the household which Jehovah shall take shall come near man by man.
15 Iye amene adzagwidwe ndi zinthu zoyenera kuwonongedwazo adzawotchedwa ndi moto, pamodzi ndi banja lake lonse ndi zinthu zake zonse. Iyeyutu wachita chinthu chonyansa pakati pa Aisraeli ndi kuphwanya pangano limene anthu anga anachita ndi Ine!”
And it shall be, that he who is taken with the devoted thing shall be burnt with fire, he and all that he has, because he has transgressed the covenant of Jehovah, and because he has wrought folly in Israel.
16 Mmawa mwake Yoswa anabweretsa Israeli fuko limodzilimodzi ndipo fuko la Yuda linalozedwa.
So Joshua rose up early in the morning, and brought Israel near by their tribes, and the tribe of Judah was taken.
17 Anabweretsa poyera mbumba zonse za fuko la Yuda, ndipo mbumba ya Zera inagwidwa. Kenaka anatulutsa poyera mabanja onse a mbumba ya Zera ndipo banja la Zabidi linagwidwa.
And he brought near the family of Judah, and he took the family of the Zerahites. And he brought near the family of the Zerahites man by man, and Zabdi was taken.
18 Potsiriza anatulutsa anthu onse a banja la Zabidi ndipo Akani anagwidwa. Iyeyu anali mwana wa Karimi, mwana wa Zabidi, mwana wa Zera wa fuko la Yuda.
And he brought near his household man by man, and Achan, the son of Carmi, the son of Zabdi, the son of Zerah, of the tribe of Judah, was taken.
19 Ndipo Yoswa anati kwa Akani, “Mwana wanga pereka ulemerero kwa Yehova Mulungu wa Israeli ndipo umuyamike Iye. Ndiwuze zimene wachita, ndipo usandibisire.”
And Joshua said to Achan, My son, give, I pray thee, glory to Jehovah, the God of Israel, and make confession to him, and tell me now what thou have done. Hide it not from me.
20 Akani anayankha kuti, “Zoona! Ine ndachimwira Yehova Mulungu wa Israeli. Chimene ndachita ine ndi ichi:
And Achan answered Joshua, and said, Of a truth I have sinned against Jehovah, the God of Israel, and thus and thus have I done:
21 Ndinaona mwa zinthu zolanda ku nkhondo zija, mkanjo wokongola wa ku Babuloni, makilogalamu awiri a siliva ndiponso golide wolemera theka la kilogalamu. Zimenezi ndinazikhumba ndipo ndinazitenga. Ndazibisa mʼkati mwa tenti yanga, ndipo siliva ali pansi pake.”
When I saw among the spoil a goodly Babylonian mantle, and two hundred shekels of silver, and a wedge of gold of fifty shekels weight, then I coveted them, and took them. And, behold, they are hid in the ground in the midst of my tent, and the silver under it.
22 Motero Yoswa anatuma anthu, ndipo anathamanga kupita ku tenti. Anthuwo anakapeza kuti zinthuzo zinabisidwadi mʼtenti yake, ndipo siliva analidi pansi pake.
So Joshua sent messengers, and they ran to the tent. And, behold, it was hid in his tent, and the silver under it.
23 Iwo anazichotsa zinthuzo mu tenti yake nabwera nazo kwa Yoswa ndi kwa Aisraeli onse ndipo anaziyika pamaso pa Yehova.
And they took them from the midst of the tent, and brought them to Joshua, and to all the sons of Israel, and they laid them down before Jehovah.
24 Kenaka Yoswa pamodzi ndi Aisraeli onse anatenga Akani mwana wa Zera pamodzi ndi siliva, mkanjo, golide zimene anapezeka nazo zija. Anatenganso ana ake aamuna ndi aakazi, ngʼombe zake, abulu ndi nkhosa, tenti yake ndi zonse anali nazo, kupita nazo ku chigwa cha Akori.
And Joshua, and all Israel with him, took Achan the son of Zerah, and the silver, and the mantle, and the wedge of gold, and his sons, and his daughters, and his oxen, and his donkeys, and his sheep, and his tent, and all that he had, and they brought them up to the valley of Achor.
25 Yoswa anati “Chifukwa chiyani wabweretsa mavuto awa pa ife? Yehova ndiye abweretse mavuto pa iwe lero.” Kenaka Aisraeli onse anaponya miyala Akani, namupha. Anaponyanso miyala banja lake lonse, nʼkulipha. Pambuyo pake anatentha Akani uja, banja lake ndi zonse zimene anali nazo.
And Joshua said, Why have thou troubled us? Jehovah shall trouble thee this day. And all Israel stoned him with stones, and they burned them with fire, and stoned them with stones.
26 Anawunjika mulu waukulu wa miyala pa Akani, imene ilipobe mpaka lero. Nʼchifukwa chake malowa amatchedwa chigwa cha Akori mpaka lero. Ndipo Yehova anachotsa mkwiyo wake.
And they raised over him a great heap of stones, to this day, and Jehovah turned from the fierceness of his anger. Therefore the name of that place was called the valley of Achor to this day.

< Yoswa 7 >