< Yoswa 6 >

1 Tsono mzinda wa Yeriko unali utatsekedwa kuti Aisraeli asalowe. Palibe amene amatuluka kapena kulowa.
Jericho pak velmi pilně zavříno bylo pro strach synů Izraelských, a žádný nevycházel ven, ani tam nevcházel.
2 Kenaka Yehova anati kwa Yoswa, “Taona ndapereka Yeriko, pamodzi ndi mfumu yake ndi ankhondo ake mʼmanja mwako.
I řekl Hospodin k Jozue: Aj, dal jsem v ruku tvou Jericho, a krále jeho s silnými muži jeho.
3 Tsono iwe pamodzi ndi ankhondo ako onse muzizungulira mzindawu masiku asanu ndi limodzi, kamodzi pa tsiku.
Protož obcházeti budete město všickni muži bojovní, okolo města chodíce, jednou za den; tak učiníš po šest dní.
4 Ansembe asanu ndi awiri, atanyamula malipenga a nyanga za nkhosa zazimuna, akhale patsogolo pa Bokosi la Chipangano. Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri mudzazungulire mzindawu kasanu ndi kawiri ansembe akuliza malipenga.
Kněží pak sedm ať nesou sedm trub z rohů beraních před truhlou; dne pak sedmého obejdete město sedmkrát, a kněží troubiti budou v trouby.
5 Ansembe adzalize malipenga kosalekeza. Tsono anthu onse akadzamva kuliza kumeneku adzafuwule kwambiri, ndipo makoma a mzindawo adzagwa. Zikadzatero ankhondo adzalowe mu mzindawo.”
A když zdlouha troubiti budou na roh beraní, jakž nejprvé uslyšíte hlas trouby, zkřikne všecken lid křikem velikým, i oboří se zed městská na místě svém, a vejde lid do města, jeden každý proti místu, kdež stál.
6 Ndipo Yoswa mwana wa Nuni anayitana ansembe ndipo anawawuza kuti, “Nyamulani Bokosi la Chipangano cha Yehova ndipo ansembe asanu ndi awiri anyamule malipenga. Iwowa akhale patsogolo pake.”
Tedy povolav Jozue, syn Nun, kněží, řekl jim: Vezměte truhlu smlouvy, a sedm kněží ať vezmou sedm trub beraních před truhlou Hospodinovou.
7 Ndipo analamulira anthu kuti, “Yambani kuyenda! Yendani mozungulira mzinda ndipo ankhondo akhale patsogolo pa Bokosi la Yehova.”
Řekl také lidu: Jděte a obejděte město, a zbrojní ať jdou před truhlou Hospodinovou.
8 Mofanana ndi mmene Yoswa anayankhulira kwa anthu aja, ansembe asanu ndi awiri anapita patsogolo pa Bokosi la Chipangano la Yehova akuliza malipenga a nyanga za nkhosa zija, ndipo Bokosi la Chipangano cha Yehova limabwera pambuyo pawo.
A když to oznámil Jozue lidu, sedm kněží, nesouce sedm trub beraních, šli před truhlou Hospodinovou, a troubili v trouby; truhla také smlouvy Hospodinovy brala se za nimi.
9 Ankhondo amayenda patsogolo pa ansembe amene amayimba malipenga, ndiponso gulu lina pambuyo pa Bokosilo. Nthawi yonseyi nʼkuti malipenga akulira.
Zbrojní pak šli před kněžími, kteříž troubili na trouby, a ostatní šli za truhlou, jdouce a v trouby troubíce.
10 Koma Yoswa nʼkuti atalamulira anthu kuti, “Musafuwule, musakweze mawu anu kapena kuyankhula mpaka tsiku limene ndidzakuwuzani kuti mufuwule. Pamenepo mudzafuwule!”
(Lidu pak byl přikázal Jozue, řka: Nebudete křičeti, ani slyšán bude hlas váš, ani vyjde slovo z úst vašich až do dne toho, v němž řeknu vám: Křičte, i budete křičeti.)
11 Ansembe onyamula Bokosi la Chipangano la Yehova anazungulira mzindawo kamodzi. Kenaka anthu anabwerera ku msasa wawo kukagona.
Tedy obešla truhla Hospodinova město vůkol jednou, a navrátili se do stanů a zůstali v nich.
12 Yoswa anadzuka mmawa tsiku linalo ndipo ansembe ananyamula Bokosi la Yehova.
Opět povstal Jozue ráno a kněží nesli truhlu Hospodinovu.
13 Ansembe asanu ndi awiri onyamula malipenga asanu ndi awiri anakhala patsogolo pa Bokosi la Yehova akuyimba malipenga. Ankhondo anali patsogolo pawo ndipo gulu lina linatsatira Bokosi la Yehova. Apa nʼkuti malipenga akulira.
Sedm pak kněží, nesouce sedm trub beraních, předcházeli truhlu Hospodinovu, jdouce, a troubili v trouby; a zbrojní šli před nimi, a ostatní šli za truhlou Hospodinovou, když kněží šli, v trouby troubíce.
14 Tsiku lachiwiri anazunguliranso mzinda kamodzi ndi kubwerera ku misasa. Iwo anachita izi kwa masiku asanu ndi limodzi.
I obešli město druhého dne opět, a navrátili se do stanů. Tak činili po šest dní.
15 Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri, anadzuka mʼbandakucha ndipo anazungulira mzindawo kasanu ndi kawiri. Ndi pa tsiku lokhali limene anazungulira mzindawu kasanu ndi kawiri.
V den pak sedmý vstali, jakž zasvitávalo, a obešli město týmž způsobem sedmkrát; toliko toho dne obešli město sedmkrát.
16 Pomwe amazungulira kachisanu ndi chiwiri, ansembe akuliza malipenga mokweza, Yoswa analamulira anthu kuti “Fuwulani pakuti Yehova wakupatsani mzindawu!
Stalo se pak, když po sedmé obcházeli, a kněží v trouby troubili, řekl Jozue lidu: Křičtež již, dalť jest Hospodin vám město.
17 Mzindawu ndi zonse zimene zili mʼmenemo muziwononge. Rahabe yekha, mayi wadama, ndi aliyense amene ali pamodzi naye mʼnyumba mwake asaphedwe, chifukwa anabisa anthu odzazonda, amene ife tinawatuma
A budiž to město proklaté, ono i všecky věci, kteréž v něm jsou, Hospodinu; toliko Raab nevěstka ať jest živa, ona i všickni, kteříž by s ní byli v domě, nebo skryla posly, kteréž jsme byli poslali.
18 Koma musatenge kanthu kalikonse koyenera kuwonongedwa. Mukadzangotenga kanthu kalikonse koyenera kuwonongedwa, mudzaputa mavuto, misasa ya Israeli idzawonongedwa.
Avšak vystříhejte se od proklatého, abyste i vy nebyli učiněni proklatí, berouce z proklatých věcí, a uvedli byste stany Izraelské v prokletí, a zkormoutili byste je.
19 Zonse za siliva ndi golide, ziwiya zamkuwa ndi zachitsulo, ndi zake za Yehova ndipo ziyenera kukasungidwa mosungiramo chuma chake.”
Všecko pak stříbro a zlato, a nádoby měděné a železné, svaté bude Hospodinu; na poklad Hospodinu složeno bude.
20 Ansembe analiza malipenga. Anthu atamva kulira kwa malipenga, anafuwula kwambiri ndipo makoma a Yeriko anagwa. Choncho ankhondo anabwera ku mzinda uja nawulanda.
Tedy křičel lid, když zatroubili v trouby. Nebo když slyšel lid hlas trub, křičeli i oni křikem velikým, i obořila se zed na místě svém. Tedy všel lid do města, jeden každý proti místu, kdež stál. I vzali je.
21 Iwo analowa mu mzindawo nawononga ndi lupanga chilichonse chamoyo kuyambira amuna, akazi, ana ndi akulu, ngʼombe, nkhosa ndi abulu.
A pohubili ostrostí meče jako proklaté všecko, což bylo v městě, od muže až do ženy, od dítěte až do starce, a až do vola, dobytčete i osla.
22 Yoswa anawuza anthu awiri amene anakazonda dziko aja kuti, “Pitani ku nyumba ya mkazi wadama uja ndipo mukamutulutse iye pamodzi ndi onse amene ali naye ndipo mukabwere nawo kuno, munamulumbirira.”
Dvěma pak mužům, kteříž shlédli zemi, řekl Jozue: Vejděte do domu ženy nevěstky, a vyveďte ji odtud, i všecky věci, kteréž má, jakož jste jí přisáhli.
23 Choncho iwo anapita nakatenga Rahabe, abambo ake ndi amayi ake, abale ake ndi onse amene anali naye. Iwo anatulutsa banja lake lonse ndipo analiyika kuseri kwa msasa wa Aisraeli.
I všedše mládenci špehéři, vyvedli Raab a otce jejího, i matku její a bratří její i všecko, což měla, a všecku rodinu její vyvedli, a nechali jich vně za stany Izraelskými.
24 Kenaka iwo anawotcha mzinda wonse ndi chilichonse chimene chinali mʼmenemo, kupatulapo zasiliva ndi zagolide pamodzi ndi ziwiya zamkuwa ndi zachitsulo zimene anakaziyika mʼnyumba yosungiramo chuma cha Yehova.
Město pak spálili ohněm, i všecko, což v něm bylo, stříbro však a zlato a nádoby měděné a železné složili na poklad v domě Hospodinově.
25 Koma Yoswa sanaphe Rahabe, mkazi wadamayo pamodzi ndi banja lake ndi onse amene anali naye, chifukwa anabisa anthu amene iye anawatuma kukazonda Yeriko. Zidzukulu zake za Rahabeyo zikukhala pakati pa Aisraeli mpaka lero.
Raab také nevěstku, a dům otce jejího i všecko, což měla, živé zůstavil Jozue; a bydlila v lidu Izraelském až do tohoto dne, nebo skryla posly, kteréž poslal Jozue k shlédnutí Jericha.
26 Pa nthawi imeneyo Yoswa anapereka chenjezo motemberera kuti, “Akhale wotembereredwa pamaso pa Yehova munthu amene adzamangenso mzinda uwu wa Yeriko: “Aliyense amene adzayike maziko ake, mwana wake wamwamuna wachisamba adzafa, aliyense womanga zipata zake mwana wake wamngʼono adzafa.”
Toho času vydal klatbu Jozue, řka: Zlořečený buď před Hospodinem muž ten, kterýž by povstal, aby stavěl město Jericho. V prvorozeném svém založí je, a v nejmenším postaví brány jeho.
27 Motero Yehova anali ndi Yoswa, ndipo mbiri yake inafalikira dziko lonse.
Byl pak Hospodin s Jozue, a rozhlásila se pověst o něm po vší zemi.

< Yoswa 6 >