< Yoswa 21 >

1 Tsono atsogoleri a mabanja a fuko la Levi anabwera kwa wansembe Eliezara, Yoswa mwana wa Nuni, ndi kwa atsogoleri a mabanja a mafuko onse a Aisraeli,
Overhodene for levittenes familier trådte frem for Eleasar, presten, og Josva, Nuns sønn, og for familie-overhodene i Israels barns stammer
2 ku Silo mʼdziko la Kanaani ndipo anati, “Yehova analamula kudzera mwa Mose kuti atipatse mizinda kuti tikhalemo, pamodzi ndi malo odyetseramo ziweto zathu.”
og talte til dem i Silo i Kana'ans land og sa: Herren bød ved Moses at der skulde gis oss byer å bo i med jordet omkring for vårt fe.
3 Choncho, Aisraeli anapereka kwa fuko la Levi mizinda iyi pamodzi ndi malo owetera ziweto zawo kuchokera ku madera awo, monga Yehova analamulira:
Da gav Israels barn efter Herrens befaling av sine arvelodder levittene disse byer med tilhørende jorder:
4 Maere oyamba anagwera mabanja a Kohati, Alevi amene anali zidzukulu za wansembe Aaroni anapatsidwa mizinda 13 kuchokera ku mafuko a Yuda, Simeoni ndi Benjamini.
Først kom loddet ut for kahatittenes ætter, og blandt disse levitter fikk Arons, prestens, sønner ved loddkastingen tretten byer av Juda stamme og av simeonittenes stamme og av Benjamins stamme,
5 Ndipo mabanja otsala a Kohati anapatsidwa mizinda khumi kuchokera ku mafuko a Efereimu, Dani ndi theka la fuko la Manase.
og de andre Kahats barn fikk ved loddkastingen ti byer av Efra'ims stammes ætter og av Dans stamme og av den halve Manasse stamme.
6 Zidzukulu za Geresoni zinapatsidwa mizinda 13 kuchokera ku mabanja a mafuko a Isakara, Aseri, Nafutali ndi theka la fuko la Manase ku Basani.
Gersons barn fikk ved loddkastingen tretten byer av Issakars stammes ætter og av Asers stamme og av Naftali stamme og av den halve Manasse stamme i Basan.
7 Mabanja a Merari anapatsidwa mizinda khumi ndi iwiri kuchokera ku mafuko a Rubeni, Gadi ndi Zebuloni.
Meraris barn fikk efter sine ætter tolv byer av Rubens stamme og av Gads stamme og av Sebulons stamme.
8 Choncho Aisraeli anapereka kwa fuko la Levi mizindayi pamodzi ndi malo odyetserako ziweto pogwiritsa ntchito maere, monga Yehova analamula kudzera mwa Mose.
Disse byer med tilhørende jorder gav Israels barn levittene ved loddkasting, således som Herren hadde befalt ved Moses.
9 Awa ndi mayina a mizinda ya mafuko a Yuda ndi Simeoni imene inaperekedwa kwa zidzukulu za Aaroni,
Av Judas barns stamme og av Simeons barns stamme avgav de de byer som nu skal nevnes:
10 ku banja la Kohati amene anali Alevi. Paja maere oyamba anagwera mabanja a Kohati kuti alandira mizinda.
Arons sønner av kahatittenes ætter, de av Levis barn som loddet først kom ut for,
11 Anapatsidwa mzinda wa Kiriati Ariba. (Paja Ariba ndiye kholo la Anaaki). Dzina lina la mzindawu ndi Hebroni, ndipo unali mʼdziko la mapiri la Yuda. Pamodzi ndi mzindawu anapatsidwanso mabusa ake onse ozungulira.
fikk Arbas, anakittenes stamfars by, det er Hebron, i Juda-fjellene med tilhørende jorder rundt omkring;
12 Komabe minda ndi midzi yozungulira mizindayi inali itaperekedwa kale kwa Kalebe, mwana wa Yefune kuti ikhale cholowa chake.
men byens mark og dens landsbyer gav de Kaleb, Jefunnes sønn, til eiendom.
13 Choncho zidzukulu za Aaroni wansembe, zinapatsidwa Hebroni (mzinda wopulumukirako amene wapha munthu), Libina,
Arons, prestens, sønner fikk både Hebron, som var tilfluktsstad for manndrapere, med tilhørende jorder og Libna med jorder
14 Yatiri, Esitemowa,
og Jattir med jorder og Estemoa med jorder
15 Holoni, Debri,
og Holon med jorder og Debir med jorder
16 Aini, Yuta, ndi Beti-Semesi pamodzi ndi mabusa odyetseramo ziweto ozungulira mizindayi. Yonse pamodzi inali mizinda isanu ndi inayi yochokera ku mafuko awiriwa.
og A'in med jorder og Jutta med jorder og Bet-Semes med jorder - ni byer av disse to stammer;
17 Fuko la Benjamini linapereka Gibiyoni, Geba,
og av Benjamins stamme: Gibeon med jorder, Geba med jorder,
18 Anatoti ndi Alimoni, pamodzi ndi mabusa odyetsera ziweto ozungulira mizindayi. Yonse pamodzi inali mizinda inayi.
Anatot med jorder og Almon med jorder - fire byer.
19 Choncho mizinda 13 pamodzi ndi malo odyetsera ziweto anapatsidwa kwa ansembe, zidzukulu za Aaroni.
Således fikk Arons sønner, prestene, i alt tretten byer med tilhørende jorder.
20 Mabanja ena otsalira a Kohati a fuko la Levi anapatsidwa mizinda iyi kuchokera ku fuko la Efereimu:
Og Kahats barns ætter av levittene - de andre av Kahats barn - fikk av Efra'ims stamme disse byer, som utgjorde deres lodd:
21 Mizinda ya Sekemu ndi Gezeri ndiye inali mizinda wopulumukirako munthu aliyense wopha mnzake mwangozi. Mizindayi inali ku mapiri a Efereimu.
De fikk Sikem, som var tilfluktsstad for manndrapere, med tilhørende jorder i Efra'im-fjellene og Geser med jorder
22 Analandiranso mizinda ya Gezeri, Kibuzaimu, Beti-Horoni pamodzi ndi malo odyetsera ziweto ozungulira mizindayi. Yonse pamodzi inali mizinda inayi.
og Kibsa'im med jorder og Bet-Horon med jorder - fire byer;
23 Fuko la Dani linapereka mizinda ya Eliteke, Gibetoni,
og av Dans stamme: Elteke med jorder, Gibbeton med jorder,
24 Ayaloni, Gati-Rimoni pamodzi ndi mabusa odyetsera ziweto ozungulira mizindayi. Yonse pamodzi inali mizinda inayi.
Ajalon med jorder, Gat-Rimmon med jorder - fire byer;
25 Kuchokera ku theka la fuko la Manase analandira Taanaki ndi Gati-Rimoni pamodzi ndi malo awo owetera ziweto, mizinda iwiri.
og av den halve Manasse stamme: Ta'anak med jorder og Gat-Rimmon med jorder - to byer.
26 Mizinda khumi yonseyi pamodzi ndi malo odyetsera ziweto, zinapatsidwa ku mabanja ena onse a Akohati.
Det var i alt ti byer med tilhørende jorder som de andre kahatitters ætter fikk.
27 Mabanja a Ageresoni a fuko la Levi anapatsidwa mizinda iwiri kuchokera ku theka la Manase wa kummawa, Golani ku Basani (mzinda wopulumukirako amene wapha munthu mwangozi) ndi Beesitera, pamodzi ndi malo awo odyetserako ziweto.
Og Gersons barn av levittenes ætter fikk av den halve Manasse stamme Galon i Basan, som var tilfluktsstad for manndrapere, med tilhørende jorder, og Be'estera med jorder - to byer;
28 Fuko la Isakara linapereka mizinda ya Kisoni, Daberati,
og av Issakars stamme: Kisjon med jorder, Daberat med jorder.
29 Yarimuti ndi Eni Ganimu, pamodzi ndi malo awo odyetsera ziweto. Yonse pamodzi inali mizinda inayi.
Jarmut med jorder, En-Gannim med jorder - fire byer;
30 Fuko la Aseri linapereka mizinda ya Misali, Abidoni,
og av Asers stamme: Misal med jorder, Abdon med jorder,
31 Helikati ndi Rehobu pamodzi ndi malo awo odyetsera ziweto. Yonse pamodzi inali mizinda inayi.
Helkat med jorder og Rehob med jorder - fire byer;
32 Fuko la Nafutali linapereka mizinda ya Kedesi wa ku Galileya, mzinda umene unali wopulumukiramo munthu wopha mnzake mwangozi. Analandiranso mizinda ya Hamoti-Dori ndi Karitani. Kuphatikizira apa, analandira malo odyetsera ziweto a mizindayi. Yonse pamodzi inali mizinda inayi.
og av Naftali stamme: Kedes i Galilea, som var tilfluktsstad for manndrapere, med tilhørende jorder, og Hammot-Dor med jorder og Kartan med jorder - tre byer.
33 Mabanja onse a Ageresoni analandira mizinda 13 pamodzi ndi malo awo odyetsera a ziweto.
Gersonittenes byer efter deres ætter utgjorde således i alt tretten byer med tilhørende jorder.
34 Mabanja a Merari amene anali otsala a fuko la Levi, anapatsidwa mizinda iyi kuchokera ku fuko la Zebuloni: Yokineamu, Karita,
Og Meraris barns ætter, resten av levittene, fikk av Sebulons stamme: Jokneam med jorder, Karta med jorder,
35 Dimuna ndi Nahalali, pamodzi ndi malo awo odyetsera ziweto. Yonse pamodzi inali mizinda inayi.
Dimna med jorder, Nahalal med jorder - fire byer;
36 Kuchokera ku fuko la Rubeni analandira Bezeri, Yahaza,
og av Rubens stamme: Beser med jorder og Jahsa med jorder,
37 Kedemoti ndi Mefaati, pamodzi ndi malo awo odyetsera ziweto. Yonse pamodzi inali mizinda inayi.
Kedemot med jorder og Mefa'at med jorder - fire byer;
38 Kuchokera ku fuko la Gadi analandira mzinda wa Ramoti ku Giliyadi. Mzinda umene unali wopulumukiramo munthu wopha mnzake mwangozi.
og av Gads stamme: Ramot i Gilead, som var tilfluktsstad for manndrapere, med tilhørende jorder, og Mahana'im med jorder,
39 Analandiranso mizinda ya Mahanaimu, Hesiboni, Yazeri pamodzi ndi malo odyetserako ziweto ozungulira mizinda yonseyi. Yonse pamodzi inali mizindayi anayi.
Hesbon med jorder, Jaser med jorder - i alt fire byer.
40 Choncho mabanja onse a Merari, amene anali otsala a fuko la Levi analandira mizinda khumi ndi iwiri pogwiritsa ntchito maere.
De byer som Meraris barn, resten av levittenes ætter, fikk som sin lodd efter sine ætter, var i alt tolv byer.
41 Motero mizinda 48 ya mʼdziko limene Aisraeli analanda inapatsidwa kwa Alevi, kuphatikizapo malo ake odyetsera ziweto.
I alt utgjorde levittenes byer i Israels barns eiendomsland åtte og firti byer med tilhørende jorder.
42 Iliyonse mwa mizindayi inali ndi malo owetera ziweto oyizungulira.
Disse byer hadde hver for sig sine jorder rundt omkring sig; så var det med alle disse byer.
43 Motero Yehova anapereka kwa Israeli dziko limene analumbira kulipereka kwa makolo awo. Atalilandira anadzakhalamo.
Således gav Herren Israel hele det land han hadde svoret å ville gi deres fedre; og de inntok det og bosatte sig der.
44 Yehova anawapatsa mtendere mʼdziko lonse monga momwe analonjezera makolo awo. Palibe ndi mmodzi yemwe mwa adani awo amene anatha kuwagonjetsa chifukwa Yehova anapereka adani awo onse mʼmanja mwawo.
Og Herren lot dem ha ro på alle kanter, aldeles som han hadde tilsvoret deres fedre; og ingen av alle deres fiender kunde holde stand imot dem; alle deres fiender gav Herren i deres hånd.
45 Yehova anakwaniritsa zonse zimene analonjeza kwa Aisraeli.
Ikke ett ord blev til intet av alle de gode ord Herren hadde talt til Israels hus; det blev opfylt alt sammen.

< Yoswa 21 >