< Yoswa 21 >

1 Tsono atsogoleri a mabanja a fuko la Levi anabwera kwa wansembe Eliezara, Yoswa mwana wa Nuni, ndi kwa atsogoleri a mabanja a mafuko onse a Aisraeli,
Then came near the heads of the fathers of the Levites to Eleazar the priest, and to Joshua the son of Nun, and to the heads of the fathers of the tribes of the children of Israel;
2 ku Silo mʼdziko la Kanaani ndipo anati, “Yehova analamula kudzera mwa Mose kuti atipatse mizinda kuti tikhalemo, pamodzi ndi malo odyetseramo ziweto zathu.”
And they spoke to them at Shiloh in the land of Canaan, saying, the LORD commanded by the hand of Moses to give us cities to dwell in, with their suburbs for our cattle.
3 Choncho, Aisraeli anapereka kwa fuko la Levi mizinda iyi pamodzi ndi malo owetera ziweto zawo kuchokera ku madera awo, monga Yehova analamulira:
And the children of Israel gave to the Levites out of their inheritance, at the commandment of the LORD, these cities and their suburbs.
4 Maere oyamba anagwera mabanja a Kohati, Alevi amene anali zidzukulu za wansembe Aaroni anapatsidwa mizinda 13 kuchokera ku mafuko a Yuda, Simeoni ndi Benjamini.
And the lot came out for the families of the Kohathites: and the children of Aaron the priest, [who were] of the Levites, had by lot out of the tribe of Judah, and out of the tribe of Simeon, and out of the tribe of Benjamin, thirteen cities.
5 Ndipo mabanja otsala a Kohati anapatsidwa mizinda khumi kuchokera ku mafuko a Efereimu, Dani ndi theka la fuko la Manase.
And the rest of the children of Kohath [had] by lot out of the families of the tribe of Ephraim, and out of the tribe of Dan, and out of the half-tribe of Manasseh, ten cities.
6 Zidzukulu za Geresoni zinapatsidwa mizinda 13 kuchokera ku mabanja a mafuko a Isakara, Aseri, Nafutali ndi theka la fuko la Manase ku Basani.
And the children of Gershon [had] by lot out of the families of the tribe of Issachar, and out of the tribe of Asher, and out of the tribe of Naphtali, and out of the half-tribe of Manasseh in Bashan, thirteen cities.
7 Mabanja a Merari anapatsidwa mizinda khumi ndi iwiri kuchokera ku mafuko a Rubeni, Gadi ndi Zebuloni.
The children of Merari by their families [had] out of the tribe of Reuben, and out of the tribe of Gad, and out of the tribe of Zebulun, twelve cities.
8 Choncho Aisraeli anapereka kwa fuko la Levi mizindayi pamodzi ndi malo odyetserako ziweto pogwiritsa ntchito maere, monga Yehova analamula kudzera mwa Mose.
And the children of Israel gave by lot to the Levites these cities with their suburbs, as the LORD commanded by the hand of Moses.
9 Awa ndi mayina a mizinda ya mafuko a Yuda ndi Simeoni imene inaperekedwa kwa zidzukulu za Aaroni,
And they gave out of the tribe of the children of Judah, and out of the tribe of the children of Simeon, these cities which are [here] mentioned by name,
10 ku banja la Kohati amene anali Alevi. Paja maere oyamba anagwera mabanja a Kohati kuti alandira mizinda.
Which the children of Aaron, [being] of the families of the Kohathites, [who were] of the children of Levi, had: for theirs was the first lot.
11 Anapatsidwa mzinda wa Kiriati Ariba. (Paja Ariba ndiye kholo la Anaaki). Dzina lina la mzindawu ndi Hebroni, ndipo unali mʼdziko la mapiri la Yuda. Pamodzi ndi mzindawu anapatsidwanso mabusa ake onse ozungulira.
And they gave them the city of Arba the father of Anak (which [city is] Hebron) in the hill -[country] of Judah, with its suburbs round it.
12 Komabe minda ndi midzi yozungulira mizindayi inali itaperekedwa kale kwa Kalebe, mwana wa Yefune kuti ikhale cholowa chake.
But the fields of the city, and its villages, they gave to Caleb the son of Jephunneh for his possession.
13 Choncho zidzukulu za Aaroni wansembe, zinapatsidwa Hebroni (mzinda wopulumukirako amene wapha munthu), Libina,
Thus they gave to the children of Aaron the priest, Hebron with its suburbs, [to be] a city of refuge for the slayer; and Libnah with its suburbs,
14 Yatiri, Esitemowa,
And Jattir with its suburbs, and Eshtemoa with its suburbs,
15 Holoni, Debri,
And Holon with its suburbs, and Debir with its suburbs,
16 Aini, Yuta, ndi Beti-Semesi pamodzi ndi mabusa odyetseramo ziweto ozungulira mizindayi. Yonse pamodzi inali mizinda isanu ndi inayi yochokera ku mafuko awiriwa.
And Ain with its suburbs, and Juttah with its suburbs, [and] Beth-shemesh with its suburbs; nine cities out of those two tribes.
17 Fuko la Benjamini linapereka Gibiyoni, Geba,
And out of the tribe of Benjamin, Gibeon with its suburbs, Geba with its suburbs,
18 Anatoti ndi Alimoni, pamodzi ndi mabusa odyetsera ziweto ozungulira mizindayi. Yonse pamodzi inali mizinda inayi.
Anathoth with its suburbs, and Almon with its suburbs; four cities.
19 Choncho mizinda 13 pamodzi ndi malo odyetsera ziweto anapatsidwa kwa ansembe, zidzukulu za Aaroni.
All the cities of the children of Aaron, the priests, [were] thirteen cities with their suburbs.
20 Mabanja ena otsalira a Kohati a fuko la Levi anapatsidwa mizinda iyi kuchokera ku fuko la Efereimu:
And the families of the children of Kohath, the Levites who remained of the children of Kohath, even they had the cities of their lot out of the tribe of Ephraim.
21 Mizinda ya Sekemu ndi Gezeri ndiye inali mizinda wopulumukirako munthu aliyense wopha mnzake mwangozi. Mizindayi inali ku mapiri a Efereimu.
For they gave them Shechem with its suburbs in mount Ephraim, [to be] a city of refuge for the slayer; and Gezer with its suburbs,
22 Analandiranso mizinda ya Gezeri, Kibuzaimu, Beti-Horoni pamodzi ndi malo odyetsera ziweto ozungulira mizindayi. Yonse pamodzi inali mizinda inayi.
And Kibzaim with its suburbs, and Beth-horon with its suburbs; four cities.
23 Fuko la Dani linapereka mizinda ya Eliteke, Gibetoni,
And out of the tribe of Dan, Eltekeh with its suburbs, Gibbethon with its suburbs,
24 Ayaloni, Gati-Rimoni pamodzi ndi mabusa odyetsera ziweto ozungulira mizindayi. Yonse pamodzi inali mizinda inayi.
Ajalon with its suburbs, Gath-rimmon with its suburbs; four cities.
25 Kuchokera ku theka la fuko la Manase analandira Taanaki ndi Gati-Rimoni pamodzi ndi malo awo owetera ziweto, mizinda iwiri.
And out of the half-tribe of Manasseh, Taanach with its suburbs, and Gath-rimmon with its suburbs; two cities.
26 Mizinda khumi yonseyi pamodzi ndi malo odyetsera ziweto, zinapatsidwa ku mabanja ena onse a Akohati.
All the cities [were] ten with their suburbs, for the families of the children of Kohath that remained.
27 Mabanja a Ageresoni a fuko la Levi anapatsidwa mizinda iwiri kuchokera ku theka la Manase wa kummawa, Golani ku Basani (mzinda wopulumukirako amene wapha munthu mwangozi) ndi Beesitera, pamodzi ndi malo awo odyetserako ziweto.
And to the children of Gershon, of the families of the Levites, out of the [other] half-tribe of Manasseh [they gave] Golan in Bashan with its suburbs, [to be] a city of refuge for the slayer, and Beesh-terah with its suburbs; two cities.
28 Fuko la Isakara linapereka mizinda ya Kisoni, Daberati,
And out of the tribe of Issachar, Kishon with its suburbs, Dabareh with its suburbs,
29 Yarimuti ndi Eni Ganimu, pamodzi ndi malo awo odyetsera ziweto. Yonse pamodzi inali mizinda inayi.
Jarmuth with its suburbs, En-gannim with its suburbs; four cities.
30 Fuko la Aseri linapereka mizinda ya Misali, Abidoni,
And out of the tribe of Asher, Mishal with its suburbs, Abdon with its suburbs,
31 Helikati ndi Rehobu pamodzi ndi malo awo odyetsera ziweto. Yonse pamodzi inali mizinda inayi.
Helkath with its suburbs, and Rehob with its suburbs; four cities.
32 Fuko la Nafutali linapereka mizinda ya Kedesi wa ku Galileya, mzinda umene unali wopulumukiramo munthu wopha mnzake mwangozi. Analandiranso mizinda ya Hamoti-Dori ndi Karitani. Kuphatikizira apa, analandira malo odyetsera ziweto a mizindayi. Yonse pamodzi inali mizinda inayi.
And out of the tribe of Naphtali, Kedesh in Galilee with its suburbs, [to be] a city of refuge for the slayer; and Hammoth-dor with its suburbs, and Kartan with its suburbs; three cities.
33 Mabanja onse a Ageresoni analandira mizinda 13 pamodzi ndi malo awo odyetsera a ziweto.
All the cities of the Gershonites, according to their families, [were] thirteen cities with their suburbs.
34 Mabanja a Merari amene anali otsala a fuko la Levi, anapatsidwa mizinda iyi kuchokera ku fuko la Zebuloni: Yokineamu, Karita,
And to the families of the children of Merari, the rest of the Levites, out of the tribe of Zebulun, Jokneam with its suburbs, and Kartah with its suburbs,
35 Dimuna ndi Nahalali, pamodzi ndi malo awo odyetsera ziweto. Yonse pamodzi inali mizinda inayi.
Dimnah with its suburbs, Nahalal with its suburbs; four cities.
36 Kuchokera ku fuko la Rubeni analandira Bezeri, Yahaza,
And out of the tribe of Reuben, Bezer with its suburbs, and Jahazah with its suburbs,
37 Kedemoti ndi Mefaati, pamodzi ndi malo awo odyetsera ziweto. Yonse pamodzi inali mizinda inayi.
Kedemoth with its suburbs, and Mephaath with its suburbs; four cities.
38 Kuchokera ku fuko la Gadi analandira mzinda wa Ramoti ku Giliyadi. Mzinda umene unali wopulumukiramo munthu wopha mnzake mwangozi.
And out of the tribe of Gad, Ramoth in Gilead with its suburbs [to be] a city of refuge for the slayer; and Mahanaim with its suburbs,
39 Analandiranso mizinda ya Mahanaimu, Hesiboni, Yazeri pamodzi ndi malo odyetserako ziweto ozungulira mizinda yonseyi. Yonse pamodzi inali mizindayi anayi.
Heshbon with its suburbs, Jazer with its suburbs; four cities in all.
40 Choncho mabanja onse a Merari, amene anali otsala a fuko la Levi analandira mizinda khumi ndi iwiri pogwiritsa ntchito maere.
So all the cities for the children of Merari by their families, which were remaining of the families of the Levites, were [by] their lot twelve cities.
41 Motero mizinda 48 ya mʼdziko limene Aisraeli analanda inapatsidwa kwa Alevi, kuphatikizapo malo ake odyetsera ziweto.
All the cities of the Levites within the possession of the children of Israel [were] forty and eight cities with their suburbs.
42 Iliyonse mwa mizindayi inali ndi malo owetera ziweto oyizungulira.
These cities were every one with their suburbs around them. Thus [were] all these cities.
43 Motero Yehova anapereka kwa Israeli dziko limene analumbira kulipereka kwa makolo awo. Atalilandira anadzakhalamo.
And the LORD gave to Israel all the land which he swore to give to their fathers: and they possessed it, and dwelt in it.
44 Yehova anawapatsa mtendere mʼdziko lonse monga momwe analonjezera makolo awo. Palibe ndi mmodzi yemwe mwa adani awo amene anatha kuwagonjetsa chifukwa Yehova anapereka adani awo onse mʼmanja mwawo.
And the LORD gave them rest on all sides, according to all that he swore to their fathers: and there stood not a man of all their enemies before them; the LORD delivered all their enemies into their hand.
45 Yehova anakwaniritsa zonse zimene analonjeza kwa Aisraeli.
There failed not aught of any good thing which the LORD had spoken to the house of Israel; all came to pass.

< Yoswa 21 >