< Yoswa 2 >

1 Tsono Yoswa mwana wa Nuni anatuma anthu awiri okazonda dziko mwachinsinsi kuchokera ku Sitimu. Iye anawawuza kuti, “Pitani mukaone dzikolo makamaka mzinda wa Yeriko.” Kotero iwo anapita ndipo anakafika ku nyumba ya mkazi wadama dzina lake Rahabe, ndipo anagona kumeneko.
Then Joshua son of Nun secretly sent two men out from Shittim as spies. He said, “Go, look over the land, especially Jericho.” They went away and came to the house of a prostitute whose name was Rahab, and they lodged there.
2 Mfumu ya Yeriko inawuzidwa kuti, “Aisraeli ena afika mu mzinda muno usiku uno kudzazonda dziko.”
It was told to the king of Jericho, “Look, men of Israel have come here to spy on the land.”
3 Choncho Mfumu ya Yeriko inatumiza uthenga kwa Rahabe kuti, “Atulutse anthu amene abwera ku nyumba kwakowo chifukwa iwo abwera kuti adzazonde dzikoli.”
The king of Jericho sent word to Rahab and said, “Bring out the men who have come to you who entered your house, for they have come to spy on the whole land.”
4 Koma pa nthawiyi nʼkuti mkaziyo atatenga amuna awiriwo ndi kuwabisa. Tsono anayankha kuti, “Inde, anthuwo anafikadi ku nyumba kuno. Koma sindinadziwe kumene anachokera.
But the woman had taken the two men and hidden them. She replied, “Yes, the men came to me, but I did not know where they were from.
5 Iwo achoka kuno ndi chisisira, chipata cha mzinda chili pafupi kutsekedwa. Ndiye sindidziwa kumene alowera. Koma mukawalondola msanga muwapeza.”
They left when it was dusk, when it was time for the city gate to shut. I do not know where they went. You will probably catch them if you hurry after them.”
6 Koma nʼkuti atawakweza pa denga azondiwo ndi kuwabisa pansi pa mapesi a thonje amene iye anawayika pa dengapo.
But she had taken them up to the roof and hidden them with the stalks of flax that she had laid out on the roof.
7 Nthumwi za mfumu zija zitatuluka ndipo chipata chinatsekedwa. Nthumwizo zinapita kukawafunafuna azondi aja mpaka ku dooko la Yorodani.
So the men pursued them on the road that leads to the fords of the Jordan. The gate was shut as soon as the pursuers went out.
8 Azondiwo asanagone, Rahabe anakwera pa denga
The men had not yet lain down for the night, when she came up to them on the roof.
9 ndipo anawawuza kuti, “Ine ndikudziwa kuti Yehova wakupatsani dziko lino ndipo tili ndi mantha. Anthu onse a mʼdziko lino ali ndi mantha chifukwa cha inu.
She said, “I know that Yahweh has given you the land and that the fear of you has come upon us. All those who live in the land will melt away before you.
10 Ife tinamva mmene Yehova anawumitsira madzi a Nyanja Yofiira inu mukufika pamene munatuluka mʼdziko la Igupto. Tamvanso zimene munachita kwa Sihoni ndi Ogi, mafumu awiri a Aamori amene ali kummawa kwa Yorodani. Inu munawawononga kotheratu.
We have heard how Yahweh dried up the water of the Sea of Reeds for you when you came out of Egypt. We also heard what you did to the two kings of the Amorites on other side of the Jordan—Sihon and Og—whom you completely destroyed.
11 Titamva zimenezi, ife tinataya mtima ndipo aliyense wa ife ali ndi mantha chifukwa cha inu. Tikudziwa kuti Yehova Mulungu wanu ndi Mulungu wa kumwamba ndi dziko lapansi.
As soon as we had heard it, our hearts melted and there was no courage left in anyone—for Yahweh your God, he is God in heaven above and on the earth below.
12 Choncho mulumbire pamaso pa Yehova ndi kundipatsa chizindikiro choti mudzachitadi zimene mwalonjeza, kuti monga inu ndakuchitirani chifundo, inunso mudzachitira chifundo a pa banja la abambo anga.
Now then, please swear to me by Yahweh that, just as I have been kind to you, you will also deal kindly with my father's house. Give me a sure sign
13 Inu mulonjeze kuti simudzapha abambo anga ndi amayi anga, abale anga ndi alongo anga ndi mabanja awo omwe.”
that you will spare the lives of my father, mother, brothers, sisters and all their families, and that you will save us from death.”
14 Anthuwo anamuyankha kuti, “Ife ndife okonzeka kufa chifukwa cha inu. Ngati iwe sudzawulula zimene tachitazi, ndiye kuti ife tidzakukomera mtima ndi kusunga pangano lathu ndi iwe, Yehova akadzatipatsa dziko lino.”
The men said to her, “Our life for yours, even to death! If you do not speak about our business, then, when Yahweh gives us this land we will be merciful and faithful to you.”
15 Popeza nyumba ya Rahabe inali pa linga la mzindawo, azondi aja anatulukira pa zenera. Rahabe anawatsitsa pansi ndi chingwe.
So she let them down out through the window using a rope. The house in which she lived was built into the wall of the city.
16 Iye anawawuza kuti, “Pitani ku mapiri kuti okuthamangiraniwo asakupezeni. Mukabisale kumeneko masiku atatu mpaka iwo atabwerera, ndipo kenaka muzikapita kwanu.”
She said to them, “Go in the hills and hide or the pursuers will find you. Hide there for three days until the pursuers have returned. Then go on your way.”
17 Anthuwo anati kwa iye, “Lonjezo limene watichititsa ifeli tidzalisungadi
The men said to her, “We will be not be bound to the promises of the oath you made us swear to, if you do not do this.
18 tikadzalowa mʼdzikoli, iwe udzamangirire kansalu kofiira pa zenera limene unatitulutsira, ndi kusonkhanitsa abambo ako, amayi ako, abale ako ndi banja lako lonse mʼnyumba muno.
When we come into the land, you must tie this scarlet rope in the window through which you let us down, and you will gather into the house your father and mother, your brothers and all your father's household.
19 Ngati wina aliyense adzatuluka mʼnyumbamo kuti azikayendayenda mu msewu, magazi ake adzakhala pamutu pake, ife sitidzapalamula kanthu. Koma wina aliyense wokhala mʼnyumba mwakomo akadzaphedwa, mlandu udzakhala wathu.
Whoever goes out of the doors of your house into the street, their blood will be upon their own heads and we will be guiltless. But if a hand is laid upon any who is with you in the house, his blood will be on our head.
20 Komanso iwe ukangowulula zimene ife tikuchitazi ndiye kuti ife sitidzasunga zimene talonjezazi.”
But if you speak about our business, we will be free from the oath you made us swear.”
21 Rahabe anayankha kuti, “Zikhale monga mwaneneramo.” Kenaka iye anawatulutsa ndipo iwowo anapita. Pambuyo pake Rahabe anamangirira kansalu kofiira pa zenera paja.
Rahab replied, “May what you say be done.” She sent them away and they left. Then she tied the scarlet rope in the window.
22 Azondi aja anachoka napita ku mapiri ndipo anakhalako masiku atatu. Apa nʼkuti otumidwa ndi mfumu aja atawafunafuna ponseponse nʼkubwerera osawapeza.
They left and went up into the hills and they stayed there three days until their pursuers returned. The pursuers searched all along the road and found nothing.
23 Pambuyo pake azondi awiri aja anayamba ulendo wobwerera kwawo. Anatsika ku mapiri kuja, nawoloka mtsinje mpaka anakafika kwa Yoswa mwana wa Nuni. Ndipo anamuwuza zonse zimene zinawachitikira.
The two men returned and crossed over and came back to Joshua son of Nun, and they told him everything that had happened to them.
24 Iwo anati kwa Yoswa, “Ndithu, Yehova wapereka dziko lonse mʼmanja mwathu. Anthu onse kumeneko akuchita nafe mantha.”
They said to Joshua, “Truly Yahweh has given this land to us. All the inhabitants of the land are melting away because of us.”

< Yoswa 2 >