< Yoswa 17 >

1 Gawo lina la dzikolo linapatsidwa kwa mabanja ena a fuko la Manase, mwana woyamba kubadwa wa Yosefe. Makiri anali mwana woyamba kubadwa wa Manase ndiponso kholo la anthu okhala ku Giliyadi. Popeza kuti iye anali munthu wankhondo, analandira Giliyadi ndi Basani.
Il y eut aussi un sort pour la Tribu de Manassé qui fut le premier-né de Joseph. Quant à Makir premier-né de Manassé, [et] père de Galaad, parce qu'il fut un homme belliqueux, il eut Galaad et Basan.
2 Mabanja ena otsala a fuko la Manase amene analandira dziko ndi awa: Abiezeri, Heleki, Asirieli, Sekemu, Heferi ndi Semida. Izi ndi zidzukulu zina zazimuna za Manase mwana wa Yosefe ndiponso eni mbumba.
Puis le reste des enfants de Manassé eut [ce sort], selon ses familles; [savoir] les enfants d'Abihézer, les enfants de Helek, les enfants d'Asriël, les enfants de Sekem, les enfants de Hépher, et les enfants de Semidah. Ce sont là les enfants mâles de Manassé fils de Joseph, selon leurs familles.
3 Panali Zelofehadi mwana wa Heferi, mwana wa Giliyadi, mwana wa Makiri mwana wa Manase. Iyeyu analibe ana aamuna koma aakazi okhaokha ndipo mayina awo ndi awa: Mahila, Nowa, Hogila, Milika ndi Tiriza.
Or Tselophcad fils de Hépher fils de Galaad, fils de Makir, fils de Manassé, n'eut point de fils, mais des filles; et ce sont ici leurs noms, Mahla, Noha, Hogla, Milca et Tirtsa;
4 Iwo anapita kwa Eliezara wansembe, Yoswa mwana wa Nuni, ndi atsogoleri ndipo anati: “Yehova analamula Mose kuti ife ndi alongo athu atipatse cholowa chathu.” Choncho iwowo pamodzi ndi abale a abambo awo anawapatsa dera lina la dzikolo kuti likhale monga mwa lamulo la Yehova.
Lesquelles vinrent se présenter devant Eléazar le Sacrificateur, et devant Josué, fils de Nun, et devant les principaux [du peuple], en disant: L'Eternel a commandé à Moïse qu'on nous donnât un héritage parmi nos frères; c'est pourquoi on leur donna un héritage parmi les frères de leur père, selon le commandement de l'Eternel.
5 Choncho kuwonjezera pa mayiko a Giliyadi ndi Basani kummawa kwa Yorodani, anthu a fuko la Manase analandiranso magawo khumi
Et dix portions échurent à Manassé, outre le pays de Galaad et de Basan, qui étaient au delà du Jourdain.
6 chifukwa ana aakazi a fuko la Manase analandira cholowa chawo pakati pa ana aamuna. Dziko la Giliyadi linali dziko la zidzukulu zonse za Manase.
Car les filles de Manassé eurent un héritage parmi ses enfants; et le pays de Galaad fut pour le reste des enfants de Manassé.
7 Malire a dziko la Manase anayambira ku Aseri, ndipo anakafika ku Mikimetati kummawa kwa Sekemu. Tsono malire anapita kummwera kuloza kwa anthu a ku Eni-Tapuwa.
Or la frontière de Manassé fut du côté d'Aser, venant à Micmethah, qui était au devant de Sichem; puis cette frontière devait aller à main droite vers les habitants de Hen-Tappuah.
8 (Manase anatenga dziko la Tapuwa, koma mzinda wa Tapuwawo, umene unali mʼmalire mwa Manase unali wa fuko la Efereimu).
Or le pays de Tappuah appartenait à Manassé; mais Tappuah qui était près des confins de Manassé, appartenait aux enfants d'Ephraïm.
9 Ndipo malire ake anapitirira kummwera mpaka ku mtsinje wa ku Kana. Mizinda ya kummwera kwa mtsinjewo inali ya fuko la Efereimu ngakhale kuti inali mʼdziko la Manase. Malire a fuko la Manase anapita kumpoto kwa mtsinje wa Kana ndi kukathera ku Nyanja.
De là cette frontière devait descendre au torrent de Kana, tirant vers le Midi du torrent. Ces villes-là sont à Ephraïm parmi les villes de Manassé. Au reste, la frontière de Manassé était au côté du Septentrion du torrent, et ses extrémités se devaient rendre à la mer.
10 Dziko la kummwera linali la Efereimu ndipo la kumpoto linali la Manase. Dziko la Manase linafika ku nyanja ndipo linachita malire ndi Aseri, kumpoto ndiponso Isakara, kummawa.
Ce qui était vers le Midi était à Ephraïm, et ce qui était vers le Septentrion, était à Manassé, et il avait la mer pour sa borne; et, du côté du Septentrion [les frontières] se rencontraient en Aser, et en Issacar, du côté d'Orient.
11 Mʼdziko la Isakara ndi Aseri, Manase analinso ndi mizinda ya Beti-Seani ndi Ibuleamu pamodzi ndi midzi yawo yozungulira. Panalinso Akanaani amene ankakhala ku Dori, Endori, Taanaki ndi Megido pamodzi ndi mizinda yozungulira (wachitatu pa mʼndandandawu ndi Nafati Dori).
Car Manassé eut aux quartiers d'Issacar et d'Aser, Beth-séan, et les villes de son ressort; et Jibléham, et les villes de son ressort; et les habitants de Dor, et les villes de son ressort; et les habitants de Hendor, et les villes de son ressort; et les habitants de Tahanac, et les villes de son ressort; et les habitants de Meguiddo, et les villes de son ressort, qui sont trois contrées.
12 Komabe anthu a fuko la Manase sanathe kuwapirikitsa anthu okhala mʼmizinda imeneyi. Choncho Akanaani anakhalabe mʼmizindayi.
Au reste, les enfants de Manassé ne purent point déposséder [les habitants] de ces villes-là, mais les Cananéens osèrent demeurer dans le même pays.
13 Ngakhale Aisraeli anali a mphamvu mʼdzikomo, sanapirikitse Akanaani onse koma anangowasandutsa kukhala akapolo.
Mais depuis que les enfants d'Israël se furent fortifiés, ils rendirent les Cananéens tributaires; toutefois ils ne les dépossédèrent point entièrement.
14 Anthu a fuko la Yosefe anati kwa Yoswa, “Chifukwa chiyani mwatipatsa gawo limodzi lokha la dziko kuti likhale cholowa chathu? Ife tilipo anthu ambiri popeza Yehova watidalitsa kwambiri.”
Or les enfants de Joseph parlèrent à Josué, en disant: Pourquoi m'as-tu donné en héritage un seul lot, et une seule portion, vu que je suis un grand peuple, tant l'Eternel m'a béni jusqu'à présent?
15 Yoswa anayankha kuti, “Ngati muli ambiri ndipo dziko la ku mapiri la Efereimu lakucheperani kwambiri, lowani ku nkhalango mudule mitengo, mudzikonzere malo akuti mukhalemo, mʼdziko la Aperezi ndi Arefai.”
Et Josué leur dit: Si tu es un si grand peuple, monte à la forêt, et coupe-la, pour te faire place au pays des Phéréziens et des Réphaïms, si la montagne d'Ephraïm est trop étroite pour toi.
16 Tsono zidzukulu za Yosefe zinati, “Dziko la ku mapiri ndi losatikwaniradi, komanso Akanaani onse amene akukhala ku chigwa pamodzi ndi amene akukhala ku Beti-Seani ndi madera awo ndiponso amene ali ku chigwa cha Yezireeli ali ndi magaleta azitsulo.”
Et les enfants de Joseph répondirent: Cette montagne ne sera pas suffisante pour nous, et tous les Cananéens qui habitent au pays de la vallée, ont des chariots de fer, pour ceux qui habitent à Beth-séan, et aux villes de son ressort, et pour ceux qui habitent dans la vallée de Jizrehel.
17 Koma Yoswa anawuza zidzukulu za Yosefe, za fuko la Efereimu ndi za fuko la Manase kuti, “Inu mulipodi ambiri ndiponso amphamvu. Simulandira gawo limodzi lokha,
Josué donc parla à la maison de Joseph, [savoir] à Ephraïm et à Manassé, en disant: Tu es un grand peuple, et tu as de grandes forces, tu n'auras pas une portion seule.
18 dziko la ku mapiri lidzakhalanso lanu. Ngakhale kuti ndi nkhalango yokhayokha koma inu mudzadula mitengo yake ndipo lidzakhala lanu mpaka kumapeto. Ngakhale kuti Akanaani ali ndi magaleta azitsulo ndiponso kuti iwo ndi amphamvu, koma inu mudzawapirikitsa.”
Car tu auras la montagne; [et] parce que c'est une forêt, tu la couperas, et ses extrémités t'appartiendront; car tu en déposséderas les Cananéens, quoiqu'ils aient des chariots de fer, et qu ils soient puissants.

< Yoswa 17 >