< Yoswa 13 >

1 Yoswa atakalamba Yehova anamuwuza kuti, Iwe tsopano wakalamba kwambiri, koma dziko losalandidwa lilipobe lalikulu.
Now Joshua was old and well stricken in years. YHWH said to him, "You are old and advanced in years, and there remains yet very much land to be possessed.
2 “Madera amene atsala ndi awa: chigawo chonse cha Afilisti ndi Agesuri
This is the land that still remains: all the regions of the Philistines, and all the Geshurites;
3 kuchokera ku mtsinje wa Sihori kummawa kwa Igupto mpaka kumpoto kwa dziko la Ekroni. Madera onse amawerengedwa kuti ndi a Akanaani ngakhale amalamulidwa ndi mafumu asanu a Afilisti a ku Gaza, Asidodi, Asikeloni, Gati, Ekroni ndi Agiti, komanso ku Avimu ku chigawo cha kumpoto.
from the Shihor, which is before Egypt, even to the border of Ekron northward, which is counted as Canaanite; the five lords of the Philistines; the Gazites, and the Ashdodites, the Ashkelonites, the Gittites, and the Ekronites; also the Avvim,
4 Dziko lina la Akanaani ndi Ameara limene lili mʼmanja mwa Asidoni mpaka ku Afeki, dziko limene linachitana malire ndi dziko la Aamori.
on the south; all the land of the Canaanites, and from Arah that belongs to the Sidonians to Aphek, to the border of the Amorites;
5 Palinso dziko lonse la Gebala ndi Lebanoni cha kummawa kuyambira ku Baala-Gadi pa tsinde pa phiri la Herimoni mpaka ku Lebo Hamati.
and the land of the Gebalites, and all Lebanon, toward the sunrise, from Baal Gad under Mount Hermon to Lebo Hamath;
6 “Palinso anthu okhala mʼchigawo cha ku mapiri kuchokera ku Lebanoni mpaka ku Misirefoti-Maimu, Ine ndidzawapirikitsa pamene Aisraeli azidzalowa. Tsono uwagawire Aisraeli dziko limeneli kuti likhale cholowa chawo monga momwe ndakulamulira.
all the inhabitants of the hill country from Lebanon to Misrephoth Maim, even all the Sidonians; them will I drive out from before the children of Israel: only you allocate it to Israel for an inheritance, as I have commanded you.
7 Tsopano ugawire dziko limeneli mafuko asanu ndi anayi ndiponso theka la fuko la Manase, kuti likhale cholowa chawo.”
Now therefore divide this land for an inheritance to the nine tribes and the half-tribe of Manasseh: from the Jordan as far as the Great Sea toward the setting of the sun, you are to give it; the Great Sea will be the boundary.
8 Anthu a fuko la Rubeni ndi fuko la Gadi pamodzi ndi theka lina la fuko la Manase analandira kale cholowa chawo chimene Mose mtumiki wa Yehova anawapatsa. Cholowa chawocho chinali kummawa kwa mtsinje wa Yorodani.
But to the two tribes and to the half-tribe of Manasseh, with him the Reubenites and the Gadites received their inheritance, which Moses gave them, beyond the Jordan eastward, even as Moses the servant of YHWH gave them:
9 Dziko lawolo linayambira ku Aroeri mzinda umene uli pafupi ndi chigwa cha Arinoni, ndiponso mzinda umene uli pakati pa chigwacho. Dzikolo linkaphatikizanso dera lonse lokwera kuyambira ku Medeba mpaka ku Diboni.
from Aroer, that is on the edge of the Valley of the Arnon, and the city that is in the middle of the valley, and all the plain of Medeba to Dibon;
10 Linkaphatikizanso mizinda yonse ya mfumu Sihoni ya Aamori, imene inkalamulira mu Hesiboni, mpaka ku malire a Aamoni.
and all the cities of Sihon king of the Amorites, who reigned in Heshbon, to the border of the people of Ammon;
11 Dzikoli linaphatikizanso Giliyadi, dziko la anthu a ku Gesuri ndi Maaka, phiri lonse la Herimoni ndi dziko lonse la Basani mpaka ku Saleka.
and Gilead, and the border of the Geshurites and Maacathites, and all Mount Hermon, and all Bashan to Salecah;
12 Linaphatikizanso dziko la mfumu Ogi ya ku Basani imene imalamulira kuchokera ku Asiteroti ndi Ederi. Iye yekha ndiye anali mfumu ya Arefaimu amene anapulumuka. Mose anali atawagonjetsa anthu amenewa ndi kuwathamangitsira kutali.
all the kingdom of Og in Bashan, who reigned in Ashtaroth and in Edrei (the same was left of the remnant of the Rephaim); for Moses attacked these, and drove them out.
13 Koma Aisraeli sanathamangitse anthu a ku Gesuri ndi Maaka, kotero iwowa amakhalabe pakati pawo mpaka lero.
Nevertheless the children of Israel did not drive out the Geshurites, nor the Maacathites: but Geshur and Maacath dwell in the midst of Israel to this day.
14 Koma Mose sanapereke dziko kwa fuko la Alevi popeza zopereka zopatulika zimene anthu ankapereka kwa Yehova, Mulungu wa Israeli, ndizo zinali cholowa chawo monga Yehova anawalonjezera.
Only he gave no inheritance to the tribe of Levi. The offerings of YHWH, the God of Israel, made by fire are his inheritance, as he spoke to him.
15 Mose anapereka gawo lina la dziko kwa mabanja a fuko la Rubeni.
Moses gave to the tribe of the descendants of Reuben according to their families.
16 Dziko lawo linayambira ku Aroeri mzinda umene uli pafupi ndi chigwa cha Arinoni, mʼmudzi wa pakati pa chigwa, ndiponso dera lonse lokwera mpaka ku Medeba.
Their border was from Aroer, that is on the edge of the Valley of the Arnon, and the city that is in the middle of the valley, and all the plain by Medeba;
17 Dzikolo linaphatikizanso Hesiboni ndi mizinda yake yonse, komanso mizinda monga Diboni, Bamoti Baala, Beti-Baala-Meoni,
Heshbon, and all its cities that are in the plain; Dibon, Bamoth Baal, Beth Baal Meon,
18 Yahaza, Kedemoti, Mefaati.
Jahaz, Kedemoth, Mephaath,
19 Kiriataimu, Sibima, Zereti-Sahari, pa phiri limene lili mʼchigwa,
Kiriathaim, Sibmah, Zereth Shahar in the mount of the valley,
20 Beti-Peori, ku matsitso a Pisiga, ndiponso Beti-Yesimoti.
Beth Peor, the slopes of Pisgah, Beth Jeshimoth,
21 Dzikolo linaphatikizanso mizinda yonse ya ku madera okwera ndiponso dziko lonse la mfumu Sihoni ya Aamori amene ankalamulira kuchokera ku Hesiboni. Mose anamugonjetsa iye pamodzi ndi mafumu a Amidiyani awa: Evi, Rekemu, Zuri, Huri ndi Reba, mafumu amene anagwirizana ndi Sihoni. Onsewa analamulira dzikolo ngati nduna za Sihoni.
all the cities of the plain, and all the kingdom of Sihon king of the Amorites, who reigned in Heshbon, whom Moses struck with the chiefs of Midian, Evi, Rekem, Zur, Hur, and Reba, the princes of Sihon, who lived in the land.
22 Kuwonjezera pa amene anaphedwa ndi nkhondo, Aisraeli anapha ndi lupanga Balaamu mwana wa Beori, amene amachita za matsenga.
The children of Israel also killed Balaam, the son of Beor, the soothsayer, with the sword, among the rest of their slain.
23 Malire a fuko la Rubeni anali mtsinje wa Yorodani. Mizinda imeneyi pamodzi ndi midzi yake zinapatsidwa kwa mabanja a fuko la Rubeni kuti akhale cholowa chawo.
The border of the descendants of Reuben was the bank of the Jordan. This was the inheritance of the descendants of Reuben according to their families, the cities and its villages.
24 Dera limene Mose anapereka kwa mabanja a fuko la Gadi ndi ili:
Moses gave to the tribe of Gad, to the descendants of Gad, according to their families.
25 Dziko la Yazeri, mizinda yonse ya mu Giliyadi ndiponso theka la dziko la Amori kukalekezera ku Aroeri, kufupi ndi Raba;
Their border was Jazer, and all the cities of Gilead, and half the land of the people of Ammon, to Aroer that is before Rabbah;
26 ndiponso kuyambira ku Hesiboni mpaka ku Ramati-Mizipa, ndi Betonimu; ndiponso kuyambira ku Mahanaimu mpaka ku dziko la Debri.
and from Heshbon to Ramath Mizpeh, and Betonim; and from Mahanaim to the border of Debir;
27 Mu chigwa cha Yorodani analandiramo Beti-Haramu, Beti-Nimira, Sukoti ndi Zafoni pamodzi ndi dziko lonse la mfumu Sihoni ya ku Hesiboni. Malire ake a ku madzulo anali mtsinje wa Yorodani kufikira ku Nyanja ya Kinereti, kumpoto.
and in the valley, Beth Haram, Beth Nimrah, Succoth, and Zaphon, the rest of the kingdom of Sihon king of Heshbon, the Jordan's bank, to the uttermost part of the sea of Kinnereth beyond the Jordan eastward.
28 Mizinda ndi midzi imeneyi inali cholowa cha mabanja a fuko la Gadi.
This is the inheritance of the descendants of Gad according to their families, the cities and its villages.
29 Mose anali atapereka kale gawo lina la dziko limeneli kwa theka la mabanja a fuko la Manase kuti likhale cholowa chawo.
Moses gave an inheritance to the half-tribe of Manasseh. It was for the half-tribe of the descendants of Manasseh according to their families.
30 Derali linayambira ku Mahanaimu kuphatikizapo dziko lonse la mfumu Ogi, Mfumu ya ku Basani, pamodzi ndi mizinda 60 ya ku Yairi, ku Basaniko.
Their border was from Mahanaim, all Bashan, all the kingdom of Og king of Bashan, and all the towns of Jair, which are in Bashan, sixty cities.
31 Derali linaphatikizanso theka la Giliyadi pamodzi ndi Asiteroti ndi Ederi, mizinda yayikulu ya mfumu Ogi wa Basani. Mizinda imeneyi inapatsidwa kwa mabanja a Makiri, mwana wa Manase kuti ikhale cholowa cha theka la ana a Makiri, malinga ndi mabanja awo.
Half Gilead, Ashtaroth, and Edrei, the cities of the kingdom of Og in Bashan, were for the descendants of Makir the son of Manasseh, even for the half of the descendants of Makir according to their families.
32 Umu ndi mmene Mose anagawira malo a mʼchigwa cha Yorodani, kummawa kwa Yeriko, ku tsidya kwa Yorodani.
These are the inheritances which Moses distributed in the plains of Moab, beyond the Jordan at Jericho, eastward.
33 Komatu Mose sanapereke malo kwa fuko la Levi. Mose anawawuza kuti zopereka zimene anthu ankapereka kwa Yehova ndizo cholowa chawo.
But to the tribe of Levi Moses gave no inheritance. YHWH, the God of Israel, is their inheritance, as he spoke to them.

< Yoswa 13 >