< Yoswa 1 >

1 Atamwalira Mose mtumiki wa Mulungu, Yehova anati kwa Yoswa mwana wa Nuni mthandizi wa Mose:
And it was doon aftir the deeth of Moyses, seruaunt of the Lord, that the Lord spak to Josue, sone of Nun, the mynystre of Moyses, and seide to hym, Moises, my seruaunt, is deed;
2 “Mose mtumiki wanga wamwalira. Ndipo iwe ndi anthu onsewa, tsopano konzekani kuwoloka mtsinje wa Yorodani kupita ku dziko limene ndiwapatse Aisraeli onse.
rise thou, and passe this Jordan, thou, and al the puple with thee, in to the lond which Y schal yyue to the sones of Israel.
3 Paliponse pamene phazi lanu liponde, ndikupatsani monga momwe ndinalonjezera Mose.
Y schal yyue to you ech place which the step of youre foot schal trede, as Y spak to Moyses,
4 Dziko lanu lidzayambira ku chipululu kummwera mpaka ku mapiri a Lebanoni kumpoto, kuchokeranso ku mtsinje waukulu wa Yufurate kummawa, mpaka dziko lonse la Ahiti, kukafika ku Nyanja Yayikulu ya kumadzulo.
fro the deseert and Liban til to the greet flood Eufrates; al the lond of Etheis, `til to the greet see ayens the goyng doun of the sunne, schal be youre terme.
5 Palibe munthu amene adzatha kukugonjetsa masiku onse a moyo wako. Monga Ine ndinakhalira ndi Mose, chomwechonso ndidzakhala nawe. Sindidzakusiya kapena kukataya.
Noon schal mow ayenstonde you in alle the daies of thi lijf; as Y was with Moises, so Y schal be with thee; Y schal not leeue, nether Y schal forsake thee.
6 “Ukhale wamphamvu ndi wolimba mtima, chifukwa iwe udzatsogolera anthu awa kukalandira dziko limene Ine ndinalonjeza makolo awo kuti ndidzawapatsa.
Be thou coumfortid, and be thou strong; for thou schalt departe bi lot to this puple the lond, for which Y swoor to thi fadris, that Y schulde yyue it to hem.
7 Ukhale wamphamvu ndi wolimba mtima kwambiri. Usamale ndithu kuti umvere malamulo onse amene mtumiki wanga Mose anakupatsa. Usachoke pa malamulo anga ndipo kulikonse kumene udzapite udzapambana.
Therfor be thou coumfortid, and be thou ful strong, that thou kepe and do al the lawe, which Moyses, my seruaunt, comaundide to thee; bowe thou not fro it to the riyt side, ether to the left side, that thou vndirstonde alle thingis whiche thou doist.
8 Uziwerenga Buku la Malamuloli, uzilingalira zolembedwa mʼmenemo usana ndi usiku, kuti uchite zonse zimene zinalembedwamo. Ukamatero udzapeza bwino ndi kupambana.
The book of this lawe departe not fro thi mouth, but thou schalt thenke therynne in daies and nyytis, that thou kepe and do alle thingis that ben writun therynne; thanne thou schalt dresse thi weie, and schalt vndirstonde it.
9 Paja ndinakulamula kuti ukhale wamphamvu ndi wolimba mtima. Choncho usamachite mantha kapena kutaya mtima popeza Ine Yehova Mulungu wako ndidzakhala nawe kulikonse kumene udzapite.”
Lo! Y comaunde to thee; be thou coumfortid, and be thou strong; nyle thou drede `withoutforth, and nyle thou drede withynne; for thi Lord God is with thee in alle thingis, to whiche thou goost.
10 Tsono Yoswa analamula atsogoleri a Aisraeli nawawuza kuti,
And Josue comaundide to the princis of the puple, and seide, Passe ye thoruy the myddis of the castels; and comaunde `ye to the puple, and seie ye, Make ye redi metis to you,
11 “Pitani ku misasa yonse ndipo muwuze anthu kuti, ‘Konzekani, mangani katundu wanu, popeza pakapita masiku atatu kuyambira lero mudzawoloka Yorodani kupita kukatenga dziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani.’”
for after the thridde dai ye schulen passe Jordan, and ye schulen entre to welde the lond, which youre Lord God schal yyue to you.
12 Koma Yoswa anawuza fuko la Rubeni, fuko la Gadi ndi theka la fuko la Manase kuti,
Also he seide to men of Ruben, and `to men of Gad, and to the half lynage of Manasses, Haue ye mynde of the word which Moises,
13 “Kumbukirani zimene Mose mtumiki wa Yehova anakulamulani kuti, ‘Yehova Mulungu wanu akukupatsani mpumulo, ndi dziko ili kuti likhale lanu.’
the `seruaunt of the Lord, comaundide to you, and seide, Youre Lord God hath youe to you reste and al the lond;
14 Tsono akazi anu, ana anu ndi ziweto zanu zitsale mʼdziko lino limene Mose anakupatsani kummawa kwa Yorodani. Koma ankhondo anu okha ndiwo awoloke atatenga zida zawo ndi kupita patsogolo pa abale anu kukawathandiza.
youre wyues and youre sones and beestis schulen dwelle in the lond which Moises yaf to you biyende Jordan; but passe ye armed, `alle strong in hond, bifor youre britheren; and fiyte ye for hem,
15 Abale anuwo akadzalandira dziko limene Yehova Mulungu wanu akuwapatsa monga inu mwachitira, inu mudzabwerera kudzakhazikika mʼdziko lanu limene Mose mtumiki wa Yehova anakupatsani tsidya la kummawa kwa Yorodani.”
til the Lord yyue reste to youre britheren, as `he yaf also to you, and `til also thei welden the lond which youre Lord God schal yyue to hem; and so turne ye ayen in to the lond of youre possessioun, and ye schulen dwelle in that lond which Moises, `seruaunt of the Lord, yaf to you ouer Jordan, ayens the `rysyng of the sunne.
16 Kenaka iwo anayankha Yoswa kuti, “Ife tidzachita chilichonse chimene mwatilamula, ndipo kulikonse kumene mudzatitume tidzapita.
And thei answeriden to Josue, and seiden, We schulen do alle thingis whiche thou comaundidist to vs, and we schulen go, whidir euer thou sendist vs;
17 Monga momwe tinamvera Mose kwathunthu, chomwechonso tidzakumvera iwe. Yehova Mulungu wanu akhale nanu monga momwe anachitira ndi Mose.
as we obeieden in alle thingis to Moises, so we schulen obeie also to thee; oneli thi Lord God be with thee, as he was with Moyses.
18 Aliyense wotsutsana ndi inu kapena wosamvera zimene mutilamula adzaphedwa. Inu mukhale wamphamvu ndi wolimba mtima!”
Die he that ayenseith thi mouth, and obeieth not to alle thi wordis, whiche thou comaundist to hym; oneli be thou coumfortid, and do thou manli.

< Yoswa 1 >