< Yona 2 >

1 Yona ali mʼmimba mwa chinsomba chija anapemphera kwa Yehova Mulungu wake.
Then Jonah prayed unto Jehovah his God out of the fish’s belly.
2 Iye anati: “Pamene ndinali mʼmavuto anga ndinayitana Yehova, ndipo Iye anandiyankha. Ndili ku dziko la anthu akufa ndinapempha thandizo, ndipo Inu munamva kulira kwanga. (Sheol h7585)
And he said, I called by reason of mine affliction unto Jehovah, And he answered me; Out of the belly of Sheol cried I, [And] thou heardest my voice. (Sheol h7585)
3 Munandiponya mʼnyanja yozama, mʼkati mwenimweni mwa nyanja, ndipo madzi oyenda anandizungulira; mafunde anu onse ndi mkokomo wake zinandimiza.
For thou didst cast me into the depth, in the heart of the seas, And the flood was round about me; All thy waves and thy billows passed over me.
4 Ndinati, ‘Ine ndachotsedwa pamaso panu; komabe ndidzayangʼananso ku Nyumba yanu yopatulika.’
And I said, I am cast out from before thine eyes; Yet I will look again toward thy holy temple.
5 Madzi wondimiza anandichititsa mantha, nyanja yozama inandizungulira; udzu wa mʼmadzi zinakuta mutu wanga.
The waters compassed me about, even to the soul; The deep was round about me; The weeds were wrapped about my head.
6 Ndinatsikira kunsi ndithu, mʼtsinde mwa mapiri; mipiringidzo ya dziko inanditsekereza kosatha. Koma Inu munatulutsa moyo wanga mʼmandamo, Inu Yehova Mulungu wanga.
I went down to the bottoms of the mountains; The earth with its bars [closed] upon me for ever: Yet hast thou brought up my life from the pit, O Jehovah my God.
7 “Pamene moyo wanga umachoka mwa ine, ine ndinakumbukira Inu Yehova, ndipo pemphero langa linafika kwa inu, ku Nyumba yanu yopatulika.
When my soul fainted within me, I remembered Jehovah; And my prayer came in unto thee, into thy holy temple.
8 “Iwo amene amagwiritsitsa mafano achabechabe amataya chisomo chawo.
They that regard lying vanities Forsake their own mercy.
9 Koma ine ndidzapereka kwa Inu nsembe ndikuyimba nyimbo yamayamiko. Chimene ndinalonjeza ndidzachikwaniritsa. Chipulumutso chimachokera kwa Yehova.”
But I will sacrifice unto thee with the voice of thanksgiving; I will pay that which I have vowed. Salvation is of Jehovah.
10 Ndipo Yehova analamula chinsomba chija, ndipo chinakamusanza Yonayo mʼmbali mwa nyanja.
And Jehovah spake unto the fish, and it vomited out Jonah upon the dry land.

< Yona 2 >