< Yoweli 2 >

1 Lizani lipenga mu Ziyoni. Chenjezani pa phiri langa loyera. Onse okhala mʼdziko anjenjemere, pakuti tsiku la Yehova likubwera, layandikira;
Blow a horn in Zion, sound an alarm in my holy mountain, let all the inhabitants of the land tremble, for the day of the Lord comes, for near is
2 tsiku la mdima ndi chisoni, tsiku la mitambo ndi la mdima wandiweyani. Ngati mʼbandakucha umene wakuta mapiri, gulu lalikulu ndi la ankhondo amphamvu likubwera, gulu limene nʼkale lomwe silinaonekepo ngakhale kutsogolo kuno silidzaonekanso.
the day of darkness and gloom, the day of cloud and thick darkness! Like the light of dawn scattered over the mountains, a people great and powerful; its like has not been from of old, neither will be any more after it, even to the years of coming ages.
3 Patsogolo pawo moto ukupsereza, kumbuyo kwawo malawi amoto akutentha zinthu. Patsogolo pawo dziko lili ngati munda wa Edeni, kumbuyo kwawo kuli ngati chipululu, kulibe kanthu kotsalapo.
Before them the fire devours, and behind them a flame burns; like the garden of Eden is the land before them, and after them it is a desolate desert, nothing escapes them.
4 Maonekedwe awo ali ngati akavalo; akuthamanga ngati akavalo ankhondo.
Their appearance is as the appearance of horses, and like horsemen they charge.
5 Akulumpha pamwamba pa mapiri ndi phokoso ngati la magaleta, ngati moto wothetheka wonyeketsa ziputu, ngati gulu lalikulu la ankhondo lokonzekera nkhondo.
Like the sound of chariots on the tops of the mountains they leap, like the crackle of flames devouring stubble, like a mighty people preparing for battle.
6 Akangowaona, anthu a mitundu ina amazunzika mu mtima; nkhope iliyonse imagwa.
Peoples are in anguish before them, all faces grow pale.
7 Amathamanga ngati ankhondo; amakwera makoma ngati asilikali. Onse amayenda pa mizere, osaphonya njira yawo.
Like mighty men they run, like warriors they mount up a wall, they march each by himself, they break not their ranks,
8 Iwo sakankhanakankhana, aliyense amayenda molunjika. Amadutsa malo otchingidwa popanda kumwazikana.
none jostles the other. They march each in his path. They fall upon the weapons without breaking.
9 Amakhamukira mu mzinda, amathamanga mʼmbali mwa khoma. Amakwera nyumba ndi kulowamo; amalowera pa zenera ngati mbala.
They scour the city, they run on the wall. They climb up into the houses. Like a thief they enter the windows.
10 Patsogolo pawo dziko limagwedezeka, thambo limanjenjemera, dzuwa ndi mwezi zimachita mdima, ndipo nyenyezi zimaleka kuwala.
Earth trembles before them, the sky quakes, the sun and moon become dark, and the stars withdraw their shining;
11 Yehova amabangula patsogolo pawo, gulu lake lankhondo ndi losawerengeka, ndipo amphamvu ndi amene amamvera kulamula kwake. Tsiku la Yehova ndi lalikulu; ndi loopsa. Ndani adzapirira pa tsikulo?
and the Lord utters his voice before his army, for his host is exceedingly great. Mighty is he who performs his word. For great is the day of the Lord, it is terrible, who can endure it?
12 “Ngakhale tsopano, bwererani kwa Ine ndi mtima wanu wonse posala zakudya ndi kukhetsa misozi,” akutero Yehova.
But now this is the message of the Lord: Turn to me with all your heart, and with fasting and weeping and mourning,
13 Ngʼambani mtima wanu osati zovala zanu. Bwererani kwa Yehova Mulungu wanu, pakuti Iye ndi wokoma mtima ndi wachifundo, wosakwiya msanga ndi wachikondi chochuluka, ndipo amaleka kubweretsa mavuto.
rend your hearts and not your garments, and turn to the Lord your God; for he indeed is gracious and merciful, slow to anger and plenteous in love, and relents of the evil.
14 Akudziwa ndani? Mwina adzasintha maganizo nʼkutimvera chisoni, nʼkutisiyira madalitso, a chopereka cha chakudya ndi cha chakumwa kwa Yehova Mulungu wanu.
Who knows but he will turn and relent, and leave a blessing behind him, a cereal and drink-offering for the Lord your God.
15 Lizani lipenga mu Ziyoni, lengezani tsiku losala zakudya, itanitsani msonkhano wopatulika.
Blow a horn in Zion, sanctify a fast, summon an assembly,
16 Sonkhanitsani anthu pamodzi, muwawuze kuti adziyeretse; sonkhanitsani akuluakulu, sonkhanitsani ana, sonkhanitsani ndi oyamwa omwe. Mkwati atuluke mʼchipinda chake, mkwatibwi atuluke mokhala mwake.
gather the people, make holy the congregation, assemble the elders, gather the children, and the infants at the breast. Let the bridegroom come forth from his chamber, and the bride from her bridal tent.
17 Ansembe amene amatumikira pamaso pa Yehova, alire pakati pa guwa lansembe ndi khonde la Nyumba ya Yehova. Azinena kuti, “Inu Yehova, achitireni chifundo anthu anu. Musalole kuti cholowa chanu chikhale chinthu chonyozeka, kuti anthu a mitundu ina awalamulire. Kodi nʼchifukwa chiyani anthu a mitundu ina amanena kuti, ‘Ali kuti Mulungu wawo?’”
Between the porch and the altar, let the priests, the ministers of the Lord weep aloud, let them say: Spare, the Lord, your people. Make not your heritage an object of reproach, for the heathen to mock them. Why should it be said among the nations, “Where is their God?”
18 Pamenepo Yehova adzachitira nsanje dziko lake ndi kuchitira chisoni anthu ake.
Then the Lord became deeply concerned for his land, and took pity upon his people,
19 Yehova adzawayankha kuti, “Ine ndikukutumizirani tirigu, vinyo watsopano ndi mafuta ndipo mudzakhuta ndithu; sindidzakuperekaninso kuti mukhale chitonzo kwa anthu a mitundu ina.
and the Lord answered and said to his people: I will send you corn, wine, and oil. You will be satisfied. I will not make you again an object of scorn among the nations,
20 “Ine ndidzachotsa ankhondo akumpoto kuti apite kutali ndi inu, kuwapirikitsira ku dziko lowuma ndi lachipululu, gulu lawo lakutsogolo ndidzalipirikitsira ku nyanja ya kummawa ndi gulu lawo lakumbuyo, ku nyanja ya kumadzulo. Ndipo mitembo yawo idzawola, fungo lake lidzamveka.” Zoonadi Yehova wachita zinthu zazikulu.
I will remove far from you the northern foe, and I will drive it into a land barren and desolate, its front into the eastern sea, and its rear to the western sea. And from it a stench will arise. He has done great things!
21 Iwe dziko usachite mantha; sangalala ndipo kondwera. Zoonadi Yehova wachita zinthu zazikulu.
Fear not, land, exult. Rejoice for the Lord has done great things!
22 Inu nyama zakuthengo, musachite mantha, pakuti msipu wa ku chipululu ukuphukira. Mitengo ikubala zipatso zake; mitengo ya mkuyu ndi mpesa ikubereka kwambiri.
Fear not, animals of the field. For the pastures of the wilderness are putting forth new grass, for the trees bear their fruit, fig tree and vine yield full harvest.
23 Inu anthu a ku Ziyoni sangalalani, kondwerani mwa Yehova Mulungu wanu, pakuti wakupatsani mvula yoyambirira mwachilungamo chake. Iye wakutumizirani mivumbi yochuluka, mvula yoyambirira ndi mvula ya nthawi ya mphukira, monga poyamba paja.
Be glad, then, children of Zion, and rejoice in the Lord your God, for he has given you the early rain in just measure, and poured down upon you the winter rain, and sent the latter rain as before.
24 Pa malo opunthira padzaza tirigu; mʼmitsuko mudzasefukira vinyo watsopano ndi mafuta.
The threshing floors will be full of grain, and the vats will overflow with new wine and oil.
25 “Ine ndidzakubwezerani zonse zimene zinawonongedwa ndi dzombe, dzombe lalikulu ndi dzombe lalingʼono, dzombe lopanda mapiko ndi dzombe lowuluka; gulu langa lalikulu la nkhondo limene ndinalitumiza pakati panu.
I will repay you for the years which the swarming locust has eaten. The hopping, the destroying, and the cutting locusts, my great army which I sent among you, and my people will never again be put to shame.
26 Mudzakhala ndi chakudya chambiri, mpaka mudzakhuta, ndipo mudzatamanda dzina la Yehova Mulungu wanu, amene wakuchitirani zodabwitsa; ndipo anthu anga sadzachitanso manyazi.
You will eat your food and be satisfied, and praise the name of the Lord your God, who has dealt so wonderfully by you,
27 Pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine ndili mu Israeli, kuti Ine ndine Yehova Mulungu wanu, ndi kuti palibenso wina; ndipo anthu anga sadzachitanso manyazi.
and you will know that I am in the midst of Israel, that I am the Lord your God and none else, and my people will never again be put to shame.
28 “Ndipo patapita nthawi, ndidzakhuthulira Mzimu wanga pa anthu onse. Ana anu aamuna ndi ana anu aakazi adzanenera, nkhalamba zanu zidzalota maloto, anyamata anu adzaona masomphenya.
Afterwards, I will pour out my spirit on everyone. Your sons and your daughters will prophesy, your old men will dream dreams. Your young men will see visions,
29 Ngakhalenso pa antchito anga aamuna ndi aakazi ndidzakhuthulira Mzimu wanga masiku amenewo.
and even on your male and female slaves in those days, I will pour out my spirit.
30 Ndidzaonetsa zodabwitsa mlengalenga ndi pa dziko lapansi, ndizo magazi, moto ndi utsi watolotolo.
And I will show signs in the sky and on earth: Blood and fire and pillars of smoke.
31 Dzuwa lidzadetsedwa ndipo mwezi udzaoneka ngati magazi lisanafike tsiku lalikulu ndi loopsa la Ambuye.
The sun will be turned into darkness, and the moon into blood before the coming of the great and terrible day of the Lord.
32 Ndipo aliyense amene adzayitana pa dzina la Ambuye adzapulumuka; pakuti chipulumutso chidzakhala pa Phiri la Ziyoni ndi mu Yerusalemu, monga Yehova wanenera, pakati pa otsala amene Yehova wawayitana.
But whoever will call upon the name of the Lord will be saved. For in Mount Zion and in Jerusalem there will be those who escape, even as the Lord has said, and among the fugitives those whom the Lord calls.

< Yoweli 2 >