< Yobu 9 >

1 Ndipo Yobu anayankha kuti,
Alors Job prit la parole et dit:
2 “Zoonadi, ndikudziwa kuti zimenezi ndi zoona. Koma munthu angathe bwanji kukhala wolungama pamaso pa Mulungu?
Je sais bien qu'il en est ainsi: comment l'homme serait-il juste vis-à-vis de Dieu?
3 Ngakhale wina atafuna kutsutsana naye, Iye sangamuyankhe munthuyo ngakhale mawu amodzi omwe.
S'il voulait contester avec lui, sur mille choses il ne pourrait répondre à une seule.
4 Mulungu ndi wa nzeru zambiri ndipo mphamvu zake ndi zochuluka. Ndani analimbana naye popanda kupwetekeka?
Dieu est sage en son cœur, et puissant en force: qui lui a résisté, et est demeuré en paix?
5 Iye amasuntha mapiri, mapiriwo osadziwa, ndipo amawagubuduza ali wokwiya.
Il transporte les montagnes, sans qu'elles le sachent, il les renverse dans sa colère;
6 Iye amagwedeza dziko lapansi kulisuntha pamalo pake ndipo amanjenjemeretsa mizati yake.
il secoue la terre sur sa base, et ses colonnes sont ébranlées.
7 Iye amayankhula ndi dzuwa ndipo siliwala; Iyeyo amaphimba kuwala kwa nyenyezi.
Il commande au soleil, et le soleil ne se lève pas; il met un sceau sur les étoiles.
8 Ndi Mulungu yekha amene anayala mayiko akumwamba ndipo amayenda pa mafunde a pa nyanja.
Seul, il étend les cieux, il marche sur les hauteurs de la mer.
9 Iye ndiye mlengi wa nyenyezi zamlalangʼamba ndi akamwiniatsatana, nsangwe ndi kumpotosimpita.
Il a créé la Grande Ourse, Orion, les Pléiades, et les régions du ciel austral.
10 Iye amachita zozizwitsa zimene sizimvetsetseka, zodabwitsa zimene sizingawerengeke.
Il fait des merveilles qu'on ne peut sonder, des prodiges qu'on ne saurait compter.
11 Akapita pafupi ndi ine sindingathe kumuona; akadutsa, sindingathe kumuzindikira.
Voici qu'il passe près de moi, et je ne le vois pas; il s'éloigne, sans que je l'aperçoive.
12 Ngati Iye alanda zinthu, ndani angathe kumuletsa? Ndani anganene kwa Iye kuti, ‘Mukuchita chiyani?’
S'il ravit une proie, qui s'y opposera, qui lui dira: « Que fais-tu? »
13 Mulungu sabweza mkwiyo wake; ngakhale gulu lankhondo la Rahabe linawerama pa mapazi ake.
Dieu! Rien ne fléchit sa colère; devant lui s'inclinent les légions d'orgueil.
14 “Nanga ine ndingathe kukangana naye bwanji? Ndingawapeze kuti mawu oti nʼkutsutsana naye?
Et moi je songerais à lui répondre, à choisir mes paroles pour discuter avec lui!
15 Ngakhale nditakhala wosalakwa, sindingamuyankhe; ndikanangopempha chifundo kwa woweruza wanga.
Aurais-je pour moi la justice, je ne répondrais pas; j'implorerais la clémence de mon juge.
16 Ngakhale ndikanamuyitana ndipo Iye ndi kuvomera, sindikhulupirira kuti akanamva mawu angawo.
Même s'il se rendait à mon appel, je ne croirais pas qu'il eût écouté ma voix:
17 Iye akanandikantha ndi mphepo yamkuntho, ndipo akanandipweteka popanda chifukwa.
lui qui me brise comme dans un tourbillon, et multiplie mes blessures sans motif;
18 Mulungu sakanandilola kuti ndipumenso koma akanandichulukitsira zowawa.
qui ne me laisse point respirer, et me rassasie d'amertume.
19 Tikanena za mphamvu, Iye ndi wamphamvudi! Ndipo tikanena za chiweruzo cholungama, ndani angamuzenge mlandu?
S'agit-il de force, voici qu'il est fort, s'agit-il de droit, il dit: « Qui m'assigne? »
20 Ngakhale ndikanakhala wosalakwa, zoyankhula zanga zikananditsutsa; ndikanakhala wopanda cholakwa, pakamwa panga pakanandipeza wolakwa.
Serais-je irréprochable, ma bouche même me condamnerait; serais-je innocent, elle me déclarerait pervers.
21 “Ngakhale ine ndili wosalakwa, sindidziyenereza ndekha; moyo wanga ndimawupeputsa.
Innocent! Je le suis; je ne tiens pas à l'existence, et la vie m'est à charge.
22 Zonse nʼzofanana; nʼchifukwa chake ndikuti, ‘Iye amawononga anthu osalakwa ndi anthu oyipa omwe.’
Il m'importe après tout; c'est pourquoi j'ai dit: « Il fait périr également le juste et l'impie. »
23 Pamene mkwapulo ubweretsa imfa yadzidzidzi, Iye amaseka tsoka la munthu wosalakwayo.
Si du moins le fléau tuait d'un seul coup! Hélas! il se rit des épreuves de l'innocent!
24 Pamene dziko lagwa mʼmanja mwa anthu oyipa Iye amawatseka maso anthu oweruza dzikolo. Ngati si Iyeyo, nanga ndani?
La terre est livrée aux mains du méchant, Dieu voile la face de ses juges: si ce n'est pas lui, qui est-ce donc?
25 “Masiku anga ndi othamanga kwambiri kupambana munthu waliwiro; masikuwo amapita ine osaonapo zabwino.
Mes jours sont plus rapides qu'un courrier, ils fuient sans avoir vu le bonheur;
26 Amayenda ngati mabwato a njedza pa nyanja, ngati mphungu zothamangira nyama zoti zidye.
ils passent comme la barque de jonc, comme l'aigle qui fond sur sa proie.
27 Nʼtanena kuti, ‘Ndidzayiwala madandawulo anga, ndidzasintha nkhope yanga ndipo ndidzasekerera,’
Si je dis: « Je veux oublier ma plainte, quitter mon air triste, prendre un air joyeux, »
28 ndikuopabe mavuto anga onse, popeza ndikudziwa kuti simudzavomereza kuti ndine wosalakwa.
je tremble pour toutes mes douleurs, je sais que tu ne me tiendras pas pour innocent.
29 Popeza ndapezeka kale wolakwa ndivutikirenji popanda phindu?
Je serai jugé coupable: pourquoi prendre une peine inutile?
30 Ngakhale nditasamba mʼmadzi oyera kwambiri ndi kusamba mʼmanja mwanga ndi sopo,
Quand je me laverais dans la neige, quand je purifierais mes mains avec le bor,
31 mutha kundiponyabe pa dzala, kotero kuti ngakhale zovala zanga zomwe zidzandinyansa.
tu me plongerais dans la fange, et mes vêtements m'auraient en horreur.
32 “Mulungu si munthu ngati ine kuti ndithe kumuyankha, sindingathe kutsutsana naye mʼbwalo la milandu.
Dieu n'est pas un homme comme moi, pour que je lui réponde, pour que nous comparaissions ensemble en justice.
33 Pakanapezeka munthu wina kuti akhale mʼkhalapakati wathu, kuti atibweretse ife tonse pamodzi,
Il n'y a pas entre nous d'arbitre qui pose sa main sur nous deux.
34 munthu wina woti achotse ndodo ya Mulungu pa ine kuti kuopsa kwake kusandichititsenso mantha!
Qu'il retire sa verge de dessus moi, que ses terreurs cessent de m'épouvanter:
35 Pamenepo ine ndikanatha kuyankhula mosamuopa Mulunguyo, koma monga zililimu, sindingathe.
alors je parlerai sans le craindre; autrement, je ne suis point à moi-même.

< Yobu 9 >