< Yobu 5 >

1 “Itana ngati ungathe, koma ndani adzakuyankhe? Kodi ndi kwa mngelo uti ungapezeko thandizo?
Взывай, если есть отвечающий тебе. И к кому из святых обратишься ты?
2 Mkwiyo umapha chitsiru, ndipo njiru imawononga wopusa.
Так, глупца убивает гневливость, и несмысленного губит раздра-жительность.
3 Ine ndinaona chitsiru chitamera mizu, koma mwadzidzidzi nyumba yake inatembereredwa.
Видел я, как глупец укореняется, и тотчас проклял дом его.
4 Ana ake alibe ndi chitetezo chomwe; amaponderezedwa mʼbwalo la milandu popanda owateteza.
Дети его далеки от счастья, их будут бить у ворот, и не будет заступника.
5 Anthu anjala amamudyera zokolola zake, amamutengera ndi za pa minga pomwe, ndipo anthu akhwinthi amafunkha chuma chake.
Жатву его съест голодный и из-за терна возьмет ее, и жаждущие поглотят имущество его.
6 Pakuti masautso satuluka mʼfumbi, ndipo kuwukira sikuchokera mʼdothi.
Так, не из праха выходит горе, и не из земли вырастает беда;
7 Komatu munthu amabadwira kuti azunzike monga momwe mbaliwali zimathethekera mlengalenga.
но человек рождается на страдание, как искры, чтобы устремляться вверх.
8 “Koma ndikanakhala ine, ndikanamudandawulira Mulungu; ndikanapereka mlandu wanga kwa Iye.
Но я к Богу обратился бы, предал бы дело мое Богу,
9 Iye amachita zozizwitsa zimene sizimvetsetseka, zodabwitsa zimene sizingatheke kuwerengedwa.
Который творит дела великие и неисследимые, чудные без числа,
10 Iye amagwetsa mvula pa dziko lapansi, ndipo amathirira minda ya anthu.
дает дождь на лице земли и посылает воды на лице полей;
11 Iye amakweza anthu wamba, ndipo iwo amene akulira amawayika pa malo otetezedwa.
униженных поставляет на высоту, и сетующие возносятся во спасение.
12 Iyeyo amalepheretsa chiwembu cha anthu ochenjera, kotero kuti cholinga chawo sichipindula kanthu.
Он разрушает замыслы коварных, и руки их не довершают предприятия.
13 Iye amakola anthu ochenjera mu msampha wa kuchenjera kwawo, ndipo zolinga za atambwali amazithetsa msangamsanga.
Он уловляет мудрецов их же лукавством, и совет хитрых становится тщетным:
14 Mdima umawagwera nthawi yamasana; nthawi yamasana amayenda moyambasayambasa monga nthawi ya usiku.
днем они встречают тьму и в полдень ходят ощупью, как ночью.
15 Mulungu amapulumutsa amphawi ku lupanga la mʼkamwa mwawo; amawapulumutsa mʼmanja mwa anthu amphamvu.
Он спасает бедного от меча, от уст их и от руки сильного.
16 Choncho osauka ali ndi chiyembekezo, ndipo anthu opanda chilungamo amawatseka pakamwa.
И есть несчастному надежда, и неправда затворяет уста свои.
17 “Wodala munthu amene Mulungu amamudzudzula; nʼchifukwa chake usanyoze chilango cha Wamphamvuzonse.
Блажен человек, которого вразумляет Бог, и потому наказания Вседержителева не отвергай,
18 Pakuti Iye amavulaza koma amamanganso mabalawo; Iye amakantha munthu, komanso manja ake amachiritsa.
ибо Он причиняет раны и Сам обвязывает их; Он поражает, и Его же руки врачуют.
19 Pakuti adzakupulumutsa ku masautso nthawi ndi nthawi, mavuto angachuluke bwanji, sadzakukhudza ndi pangʼono pomwe.
В шести бедах спасет тебя, и в седьмой не коснется тебя зло.
20 Pa nthawi ya njala adzakulanditsa ku imfa, ndipo nthawi ya nkhondo adzakupulumutsa ku lupanga.
Во время голода избавит тебя от смерти, и на войне - от руки меча.
21 Adzakuteteza kwa anthu osinjirira, ndipo palibe chifukwa chochitira mantha pamene chiwonongeko chafika.
От бича языка укроешь себя и не убоишься опустошения, когда оно придет.
22 Uzidzaseka pa nthawi ya chiwonongeko ndi ya njala, ndipo palibe chifukwa chochitira mantha ndi zirombo za mʼdziko lapansi.
Опустошению и голоду посмеешься и зверей земли не убоишься,
23 Pakuti udzachita pangano ndi miyala ya mʼmunda mwako, ndipo nyama zakuthengo zidzakhala nawe mwamtendere.
ибо с камнями полевыми у тебя союз, и звери полевые в мире с тобою.
24 Udzadziwa kuti nyumba yako ndi malo otetezedwa; udzawerengera katundu wako ndipo sudzapeza kanthu kamene kasowapo.
И узнаешь, что шатер твой в безопасности, и будешь смотреть за домом твоим, и не согрешишь.
25 Udzadziwa kuti ana ako adzakhala ambiri, ndipo zidzukulu zako zidzakhala ngati udzu wa mʼdziko lapansi.
И увидишь, что семя твое многочисленно, и отрасли твои, как трава на земле.
26 Udzafika ku manda utakalamba, monga mitolo ya zokolola pa nyengo yake.
Войдешь во гроб в зрелости, как укладываются снопы пшеницы в свое время.
27 “Ife tafufuza zimenezi ndipo ndi zoona, choncho uzimvere ndi kuzitsata.”
Вот, что мы дознали; так оно и есть: выслушай это и заметь для себя.

< Yobu 5 >