< Yobu 41 >

1 “Kodi ungathe kukoka ngʼona ndi mbedza ya nsomba kapena kukanikiza lilime lake pansi ndi chingwe?
Tires-tu le Léviathan avec l'hameçon, fais-tu passer la ligne au travers de sa langue?
2 Kodi ungathe kumanga chingwe mʼmphuno mwake, kapena kubowola nsagwada zake ndi mbedza?
Attaches-tu la corde à son naseau, et perces-tu sa mâchoire pour y mettre l'anneau?
3 Kodi ngʼonayo idzakupempha kuti uyichitire chifundo? Kodi idzakuyankhula ndi mawu ofatsa?
Va-t-il t'adresser beaucoup de prières, et te parler d'une voix adoucie?
4 Kodi idzachita nawe mgwirizano kuti uyisandutse kapolo wako mpaka muyaya?
Va-t-il faire un pacte avec toi, pour s'engager à te servir toujours?
5 Kodi udzasewera nayo ngati mbalame, kapena kuyimangirira kuti atsikana ako asewere nayo?
Vas-tu jouer avec lui comme avec un oiseau, et le mettre à l'attache pour tes jeunes filles?
6 Kodi anthu adzayitsatsa malonda? Nanga amalondawo nʼkugawanagawana nyama yake kuti akagulitse?
Entre-t-il dans le trafic de la confrérie, et le répartit-elle entre les marchands?
7 Kodi chikopa chake ungathe kuchilasa ndi zisonga, kapena kubowola mutu wake ndi nthungo zophera nsomba?
Couvres-tu sa peau de dards, et sa tête de harpons?
8 Ukayiputa udziwe kuti pali nkhondo, ndipo iweyo sudzabwereranso.
Tentes-tu de mettre la main sur lui; tu ne t'aviseras plus de l'attaquer.
9 Chiyembekezo choti nʼkuyigonjetsa ndi chabodza; kungoyiona kokha, ndithu iwe kumangodzigwera wekha.
Voici, l'espoir de l'agresseur est bientôt déçu; n'est-il pas terrassé à son seul aspect?
10 Palibe wolimba mtima kuti ndi kuyiputa. Ndani angalimbe mtima kulimbana ndi Ine?
Nul n'a l'audace de le provoquer: et qui pourrait Me prendre à partie?
11 Kodi ndani anandipatsa kanthu kuti ndimubwezere? Zonse za pansi pa thambo ndi zanga.
Qui m'a prévenu, pour que j'aie à lui rendre? Sous le ciel entier tout est ma propriété.
12 “Sindidzaleka kuyankhula za ziwalo zake za chirombocho, za mphamvu zake ndiponso za maonekedwe a thupi lake.
Je ne tairai point sa structure, ni la nature de sa force, ni la beauté de son armure.
13 Ndani angasende chikopa chake? Ndani angayiyandikire kuti abowole chikopa chake cholimbacho?
Qui a pu soulever le recouvrement de sa robe, et pénétrer entre sa double mâchoire?
14 Ndani angatsekule kukamwa kwake, pakamwa pamene pazunguliridwa ndi mano ochititsa mantha?
Qui entr'ouvrit les portes de sa face? Tout autour sont ses dents effroyables.
15 Kumsana kwake kuli mizere ya mamba onga zishango zolumikizanalumikizana;
Des sillons sont tracés entre les boucliers de sa croupe, retenus par un sceau qui les presse;
16 Mambawo ndi olukanalukana kotero kuti mpweya sungathe kulowa pakati pake.
ils sont soudés l'un à l'autre, et l'air ne s'insinue pas dans leurs intervalles;
17 Ndi olumikizanalumikizana; ndi omatirirana kwambiri kotero kuti sangathe kulekana.
entre eux ils sont adhérents, et forment un masse solide, inséparable.
18 Kuyetsemula kwake kumatulutsa mbaliwali; maso ake amawala ngati kuwala kwa mʼbandakucha.
Son éternuement produit une gerbe lumineuse, et ses yeux sont comme les paupières de l'aurore.
19 Mʼkamwa mwake mumatuluka nsakali zamoto ndipo mumathetheka mbaliwali zamoto.
De sa gueule sortent des torches, et des étincelles enflammées s'échappent.
20 Mʼmphuno mwake mumatuluka utsi ngati wa mʼnkhali yowira yomwe ili pa moto wa bango.
Une fumée jaillit de ses narines, comme d'un vaisseau qui bout, et d'une chaudière.
21 Mpweya wake umayatsa makala, ndipo malawi amoto amatuluka mʼkamwa mwake.
Son haleine allume les charbons, et des flammes partent de sa bouche.
22 Mphamvu zake zili mʼkhosi mwake; aliyense wokumana nayo amangoti njenjenje ndi mantha.
La force réside dans son encolure, et devant lui la détresse tressaille.
23 Minyewa ya thupi lake ndi yolumikizana ndipo ndi yokhwima kwambiri ndi yolimba.
Les fanons de sa chair sont adhérents, coulés sur son corps, immobiles.
24 Pachifuwa pake ndi powuma ngati mwala, ndi pa gwaa, ngati mwala wamphero.
Son cœur a la densité de la pierre, et la densité de la meule inférieure.
25 Ngʼonayo ikangovuwuka, ndi anthu amphamvu omwe amaopa; amabwerera mʼmbuyo, kuthawa.
Se lève-t-il, les héros s'épouvantent, et la peur les déroute.
26 Ngakhale ikanthidwe ndi lupanga, lupangalo silichita kanthu, ngakhale mkondo, muvi ndi nthungo, zonse zimalephera.
Le coup qu'on lui porte, demeure sans effet; il brave la lance, le dard et la cuirasse.
27 Chitsulo imachiyesa ngati phesi chabe ndi mkuwa ngati chikuni chowola.
Pour lui le fer est autant que de la paille, et l'airain, que du bois vermoulu.
28 Muvi sungathe kuyithawitsa, miyala imene ayilasa nayo imangoyinyenyanyenya.
La flèche décochée ne le met pas en fuite, et sur lui les pierres de la fronde font l'effet de la balle.
29 Zibonga zimakhala ngati ziputu; imangoseka pamene akuyibaya ndi nthungo.
Pour lui la massue est autant que du chaume, et il se rit du frémissement des traits.
30 Mamba a ku mimba kwake ali ngati chopunthira chakunthwa ndipo imasiya mkukuluzi mʼmatope ngati galeta lopunthira tirigu.
Son ventre est muni de têts acérés; on dirait que sur le limon où il couche, un traîneau à fouler a laissé son empreinte.
31 Imagadutsa madzi ozama ngati madzi a mʼnkhali, imachititsa nyanja kuti iwire ngati mbiya yoyengera mafuta.
Il fait comme une chaudière bouillonner l'onde, et donne à la mer l'aspect d'un vaisseau où l'on broie les parfums.
32 Kumbuyo kwake imasiya nthubwitubwi zambee, kotero kuti munthu angaganize kuti nyanja yachita imvi.
Il laisse après lui un sillage lumineux; on prendrait la mer pour une blanche chevelure.
33 Pa dziko lapansi palibe china chofanana nacho, nʼcholengedwa chopanda mantha.
Sur la terre il n'a pas de maître; il fut créé pour être intrépide;
34 Chimanyoza nyama zina zonse; icho chija ndi mfumu ya nyama zonse.”
il ose regarder toute taille élevée, il est Roi au-dessus de tous les fiers animaux.

< Yobu 41 >