< Yobu 40 >

1 Yehova anati kwa Yobu:
Yahweh s'adressant à Job, dit:
2 “Kodi iwe ufuna kukangana ndi Wamphamvuzonse? Iwe amene unatsutsana ndi Mulungu umuyankhe Iyeyo!”
Le censeur du Tout-Puissant veut-il encore plaider contre lui? Celui qui dispute avec Dieu peut-il répondre?
3 Pamenepo Yobu anayankha Yehova:
Job répondit à Yahweh, en disant:
4 “Ine sindili kanthu konse, kodi ndingathe kukuyankhani chiyani? Ndagwira pakamwa panga.
Chétif que je suis, que te répondrai-je? Je mets la main sur ma bouche.
5 Ndinayankhula kamodzi, koma pano ndilibe yankho, ndinayankha kawiri, koma sindiwonjezeranso mawu ena.”
J'ai parlé une fois, je ne répliquerai pas; deux fois, je n'ajouterai rien.
6 Ndipo Yehova anayankha Yobu mʼkamvuluvulu kuti,
Yahweh parla encore à Job du sein de la tempête et dit:
7 “Tsopano vala dzilimbe ngati mwamuna; ndikufunsa mafunso ndipo iwe undiyankhe.
Ceins tes reins, comme un homme; Je vais t'interroger, et tu m'instruiras.
8 “Kodi iwe unganyoze chiweruzo changa cholungama? Kodi ungandidzudzule kuti iweyo ukhale wolungama?
Veux-tu donc anéantir ma justice, me condamner afin d'avoir droit?
9 Kodi uli ndi dzanja monga la Mulungu, ndipo mawu ako angagunde ngati mphenzi monga a Mulungu?
As-tu un bras comme celui de Dieu, et tonnes-tu de la voix comme lui?
10 Ngati zili choncho udzikometsere ndi ulemerero ndi kukongola, ndipo udziveke ulemu ndi ulemerero waufumu.
Pare-toi de grandeur et de magnificence, revêts-toi de gloire et de majesté;
11 Tsanula ukali wako wosefukirawo, uyangʼane aliyense wodzikuza ndipo umuchepetse,
épanche les flots de ta colère, d'un regard abaisse tout superbe.
12 Uyangʼane aliyense wodzikweza ndipo umutsitse, uwapondereze oyipa onse pamalo pomwe alilipo.
D'un regard fais plier tout superbe, écrase sur place les méchants;
13 Onsewo uwakwirire pamodzi mfumbi; ukulunge nkhope zawo mʼmanda.
cache-les tous ensemble dans la poussière, enferme leur visage dans les ténèbres.
14 Ukatero Ine ndidzakuvomereza kuti dzanja lako lamanja lakupulumutsadi.
Alors, moi aussi, je te rendrai l'hommage, que ta droite peut te sauver.
15 “Taganiza za mvuwu, imene ndinayipanga monga momwe ndinapangira iwe, ndipo imadya udzu ngati ngʼombe.
Vois Béhémoth, que j'ai créé comme toi: il se nourrit d'herbe, comme le bœuf.
16 Mphamvu zake ndi zazikulu kwambiri, thupi lake ndi lanyonga kwambiri!
Vois donc, sa force est dans ses reins, et sa vigueur dans les muscles de ses flancs!
17 Mchira wake umayima tolotolo ngati mtengo wamkungudza; mitsempha ya ntchafu zake ndi yogwirana bwino.
Il dresse sa queue comme un cèdre; les nerfs de ses cuisses forment un solide faisceau.
18 Mafupa ake ali ngati mapayipi amkuwa, nthiti zake zili ngati mipiringidzo yachitsulo.
Ses os sont des tubes d'airain, ses côtes sont des barres de fer.
19 Mvuwuyo ndi yayikulu mwa zolengedwa za Mulungu, komatu mlengi wake amatha kuyiopseza ndi lupanga lake.
C'est le chef-d'œuvre de Dieu; son Créateur l'a pourvu d'un glaive.
20 Imapeza chakudya chake ku mtunda ndipo nyama zakuthengo zonse zimasewera pambali pake.
Les montagnes produisent pour lui du fourrage, autour de lui se jouent toutes les bêtes des champs.
21 Imagona pa tsinde pa zitsamba za mipeta, imabisala mʼbango ndiponso pa thawale.
Il se couche sous les lotus, dans le secret des roseaux et des marécages.
22 Imaphimbika ndi mthunzi wazitsamba za mipeta; imazunguliridwa ndi misondozi ya mu mtsinje.
Les lotus le couvrent de leur ombre, les saules du torrent l'environnent.
23 Madzi a mu mtsinje akakokoma, sichita mantha, iyo sitekeseka, ngakhale madzi a mu Yorodani afike mʼkhosi mwake.
Que le fleuve déborde, il ne craint pas; il serait calme, si le Jourdain montait à sa gueule.
24 Kodi alipo amene angathe kukola mvuwu ndi mbedza kapena kuyikola mu msampha?
Est-ce en face qu'on pourra le saisir, avec des filets, et lui percer les narines?

< Yobu 40 >