< Yobu 39 >

1 “Kodi iwe umadziwa nthawi imene mbalale yayikazi imaswera? Kodi umaonerera pamene nswala ikubala?
Do you know at what time the wild goats have given birth among the rocks, or do you observe the deer when they go into labor?
2 Kodi umawerenga miyezi imene zimakhala ndi bere? Kodi nthawi imene zimaswana iwe umayidziwa?
Have you numbered the months since their conception, and do you know at what time they gave birth?
3 Zimakhala tsonga ndi kuswa ana awo; pamenepo ululu wobereka nʼkutha.
They bend themselves for their offspring, and they give birth, and they emit roars.
4 Ana a nyamazi amakhala ndi mphamvu ndipo amakulira mʼthengo; kenaka amachoka ndipo sabwereranso.
Their young are weaned and go out to feed; they depart and do not return to them.
5 “Kodi bulu wakuthengo amamupatsa ndani ufulu wongodziyendera? Ndani amamasula zingwe zake?
Who has set the wild ass free, and who has released his bonds?
6 Ine ndinamupatsa chipululu kuti chikhale mudzi wake, nthaka ya mchere kuti ikhale malo ake okhalamo
I have given a house in solitude to him, and his tabernacle is in the salted land.
7 Iye amakhala kutali ndi phokoso la mu mzinda; ndipo samva kufuwula kwa oyendetsa nyama zakatundu.
He despises the crowded city; he does not pay attention to the bellow of the tax collector.
8 Amayendayenda mʼmapiri kudya msipu ndipo amafunafuna msipu uliwonse wobiriwira.
He looks around the mountains of his pasture, and he searches everywhere for green plants.
9 “Kodi njati ingavomere kukutumikira? Kodi ingagone mu gome lako usiku?
Will the rhinoceros be willing to serve you, and will he remain in your stall?
10 Kodi ungathe kuyimanga ndi zingwe kuti izilima? Kodi ingasalaze nthumbira mʼmunda mwako?
Can you detain the rhinoceros with your harness to plough for you, and will he loosen the soil of the furrows behind you?
11 Kodi ungadalire njatiyo chifukwa champhamvu zake? Kodi ungayilekere kuti igwire ntchito zako zolemetsa?
Will you put your faith in his great strength, and delegate your labors to him?
12 Kodi ungadalire kuti idzakubweretsera tirigu wako ndi kumuyika ku malo opunthira?
Will you trust him to return to you the seed, and to gather it on your drying floor?
13 “Nthiwatiwa imakupiza mapiko ake monyadira, koma mapikowo sangafanane ndi mapiko ndi nthenga za kakowa.
The wing of the ostrich is like the wings of the heron, and of the hawk.
14 Nthiwatiwa imakwirira mazira ake pansi ndipo amafundidwa ndi nthaka,
When she leaves eggs behind in the earth, will you perhaps warm them in the dust?
15 nthiwatiwayo sidera nkhawa kuti mazira ake angathe kuswanyidwa, ndi kuti nyama zakuthengo zitha kuwaponda.
She forgets that feet may trample them, or that the beasts of the field may shatter them.
16 Nthiwatiwa imachitira nkhanza ana ake ngati anawo si ake; Imayiwala zoti inavutika powabala.
She is hardened against her young, as if they were not hers; she has labored in vain, with no fear compelling her.
17 Chifukwa Mulungu anayimana nzeru, simvetsa kanthu kalikonse.
For God has deprived her of wisdom; neither has he given her understanding.
18 Komatu nthiwatiwa ikadzambatuka ndi kuyamba kuthamanga, imamusiya kutali kavalo ndi wokwerapo wake.
Yet, when the time is right, she raises her wings on high; she ridicules the horse and his rider.
19 “Kodi ndiwe amene umamupatsa mphamvu kavalo kapena kumuveka chenjerere mʼkhosi mwake?
Will you supply strength to the horse, or envelope his throat with neighing?
20 Kodi ndiwe amene umalipatsa dzombe ulemerero wolumphira, ukali wake nʼkumachititsa mantha?
Will you alarm him as the locusts do? His panic is revealed by the display of his nostrils.
21 Iye amalumphalumpha moopseza, kukondwerera mphamvu zake, ndipo amapita ku nkhondo ndi mphamvu zake zonse.
He digs at the earth with his hoof; he jumps around boldly; he advances to meet armed men.
22 Iye sachita mantha, saopa chilichonse; sabwerera mʼmbuyo akaona lupanga.
He despises fear; he does not turn away from the sword.
23 Zida zankhondo zimachita kwichikwichi mʼchimake pambali pake pamodzi ndi mkondo wonyezimira ndi nthungo.
Above him, the quiver rattles, the spear and the shield shake.
24 Kavaloyo amanjenjemera ndi ukali ndi kulumphalumpha; satha kungoyima pamene wamva kulira kwa lipenga.
Seething and raging, he drinks up the earth; neither does he pause when the blast of the trumpet sounds.
25 Lipenga likalira amati, ‘Twee!’ Amamva fungo la nkhondo ali patali, kufuwula kwa anthu olamulira nkhondo ndi mfuwu wankhondo.
When he hears the bugle, he says, “Ha!” He smells the battle from a distance, the exhortation of the officers, and the battle cry of the soldiers.
26 “Kodi kabawi amawuluka ndi nzeru zako, ndi kutambasula mapiko ake kupita kummwera?
Does the hawk grow feathers by means of your wisdom, spreading her wings towards the south?
27 Kodi umalamulira chiwombankhanga ndiwe kuti chiziwuluka ndi kumanga chisa chake pamwamba penipeni?
Will the eagle lift herself up at your command and make her nest in steep places?
28 Chimakhala pa phiri ndipo chimakhala pamenepo usiku; chimakhala pa msonga penipeni pa mwala.
She dwells among the rocks, and she lingers among broken boulders and inaccessible cliffs.
29 Chili pamenepo chimayangʼanayangʼana choti chigwire kuti chidye; maso ake amachionera patali chinthucho.
From there, she looks for food, and her eyes catch sight of it from far away.
30 Ana ake amayamwa magazi, ndipo kumene kuli mitembo ndiko chimapezeka.”
Her young will drink blood, and wherever the carcass will be, she is there immediately.

< Yobu 39 >