< Yobu 36 >

1 Ndipo Elihu anapitirira kuyankhula nati:
Élihu continua, et dit:
2 “Mundilole pangʼono pokha ndipo ndikuonetsani kuti zilipo zambiri zoti ziyankhulidwe mʼmalo mwa Mulungu.
Attends un peu et je t'instruirai, car il y a encore des raisons pour la cause de Dieu.
3 Nzeru zanga ndimazitenga kutali; ndidzaonetsa kulungama kwa Mlengi wanga.
Je prendrai de loin ma science, et je donnerai droit à mon créateur.
4 Ndithudi mawu anga si abodza; wanzeru zangwiro ali ndi inu.
Car, certainement, mes discours ne sont point mensongers, et c'est un homme qui te parle d'une science parfaite.
5 “Mulungu ndi wamphamvu, koma sanyoza anthu; Iye ndi wamphamvu, ndipo ndi wokhazikika pa cholinga chake.
Voici, Dieu est puissant, et il ne dédaigne personne; il est puissant par la force de son intelligence.
6 Salola oyipa kuti akhalebe ndi moyo koma amapereka ufulu kwa anthu osautsidwa.
Il ne laisse point vivre le méchant, et il fait droit aux affligés.
7 Iye saleka kuyangʼanira anthu olungama; amawayika kuti alamulire pamodzi ndi mafumu ndipo amawalemekeza mpaka muyaya.
Il ne détourne pas ses yeux des justes, il place ces justes avec les rois sur le trône; et il les y fait asseoir pour toujours, et ils sont élevés.
8 Koma ngati anthu amangidwa ndi unyolo, ndipo akondwa ndi zingwe zamasautso,
S'ils sont liés de chaînes, s'ils sont pris dans les liens de l'affliction,
9 Iye amawafotokozera zomwe anachita, kuti iwo anachimwa modzikuza.
Il leur fait connaître ce qu'ils ont fait, leurs péchés et leur orgueil.
10 Mulungu amawatsekula makutu kuti amve malangizo ake ndipo amawalamula kuti alape zoyipa zawo.
Alors il ouvre leur oreille à la réprimande; il leur dit de se détourner de l'iniquité.
11 Ngati iwo amumvera ndi kumutumikira, adzatsiriza masiku a moyo wawo mwamtendere, adzatsiriza zaka zawo mosangalala.
S'ils l'écoutent, et s'ils le servent, ils achèvent leurs jours dans le bonheur, et leurs années dans la joie;
12 Koma ngati samvera, adzaphedwa ndi lupanga ndipo adzafa osadziwa kanthu.
Mais s'ils ne l'écoutent pas, ils passent par l'épée, et ils expirent dans leur aveuglement.
13 “Anthu osapembedza amasunga mkwiyo mu mtima mwawo; akawalanga, safuwulira kwa Iye kupempha thandizo.
Les cœurs impies se mettent en colère; ils ne crient point à lui quand il les a liés.
14 Amafa akanali achinyamata, pakati pa amuna achiwerewere a kumalo azipembedzo.
Leur âme meurt en sa jeunesse, et leur vie s'éteint comme celle des débauchés.
15 Koma ovutika, Iye amawapulumutsa pa mavuto awo; Mulungu amawayankhula mʼmasautso awowo.
Il sauve l'affligé par son affliction, et il l'instruit par sa douleur.
16 “Iye akukukopani inu kuti muchoke mʼmasautso, kuti mupite ku malo aakulu kumene kulibe chokutchingani, kumalo a mpumulo kumene kuli chakudya chabwino kwambiri.
Et toi-même, il te mettra hors de ta détresse, au large, loin de toute angoisse, et ta table sera dressée, couverte de graisse.
17 Koma tsopano inu mwapezeka wopalamula chifukwa cha kuyipa kwanu; chiweruzo ndi chilungamo chakugwerani.
Mais si tu es plein de la cause du méchant, cette cause et la condamnation se suivront de près.
18 Muchenjere kuti wina asakukopeni ndi chuma; musalole kuti chiphuphu chachikulu chikusocheretseni.
Prends garde que la colère ne te pousse au blasphème, et ne te laisse pas égarer par la pensée d'une abondante expiation.
19 Kodi chuma chanu kapena mphamvu zanu zonse zingakusungeni kotero kuti simungakhale pa masautso?
Ferait-il cas de ta richesse? Il n'estimera ni l'or ni les moyens de l'opulence.
20 Musalakalake kuti usiku ubwere, pakuti ndiyo nthawi imene anthu adzawonongeka.
Ne souhaite point la nuit, en laquelle les peuples sont enlevés sur place.
21 Muchenjere kuti musatembenukire ku uchimo, chifukwa uchimowo ndiwo unabweretsa kuzunzika kwanu.
Garde-toi de te tourner vers l'iniquité; car tu la préfères à l'affliction.
22 “Taonani, Mulungu ndi wamkulu ndiponso ndi wamphamvu. Kodi ndi mphunzitsi uti amene angafanane naye?
Voici, Dieu est élevé en sa puissance; qui pourrait enseigner comme lui?
23 Kodi ndani amene anamuwuzapo Mulungu zoti achite, kapena kumuwuza kuti, ‘Inu mwachita chinthu cholakwa?’
Qui lui a prescrit sa voie? Et qui lui dira: Tu as fait une injustice?
24 Kumbukirani kutamanda ntchito zake zimene anthu amaziyamika mʼnyimbo.
Souviens-toi de célébrer ses ouvrages, que tous les hommes chantent.
25 Anthu onse amaziona ntchitozo; anthuwo amaziona ali kutali.
Tout homme les admire, chacun les contemple de loin.
26 Ndithudi, Mulungu ndi wamkulu, sitimudziwa nʼpangʼono pomwe! Chiwerengero cha zaka zake nʼchosadziwika.
Voici, Dieu est élevé, et nous ne le connaissons pas; le nombre de ses années, nul ne peut le sonder!
27 “Mulungu ndiye amakweza timadontho tamadzi kuthambo, timene timasungunuka nʼkukhala mvula;
Il attire les gouttes d'eau, elles se fondent en pluie, au milieu du brouillard;
28 mitambo imagwetsa mvulayo ndipo mvulayo imavumbwa pa anthu mokwanira.
Les nuées la font couler, et tomber goutte à goutte sur la foule des hommes.
29 Kodi ndani amene angadziwe momwe mitambo imayendera, momwe Iye amabangulira kuchokera kumalo ake?
Et qui pourrait comprendre le déploiement des nuées, et le fracas de sa tente?
30 Taonani momwe amawalitsira zingʼaningʼani pa malo ake onse, zimafika ngakhale pansi pa nyanja.
Voici, il étend sur lui-même la lumière, et il couvre le profond des mers.
31 Umu ndi mmene Iye amalamulira mitundu ya anthu ndi kuwapatsa chakudya chochuluka.
C'est ainsi qu'il juge les peuples, et qu'il donne la nourriture en abondance.
32 Amadzaza manja ake ndi zingʼaningʼani, ndipo amazilamulira kuti zigwe pamalo pamene Iye akufuna.
Il tient cachée dans sa main la lumière, et il lui prescrit de frapper.
33 Mabingu ake amalengeza za kubwera kwa mvula yamkuntho; ngʼombe nazo zimalengeza za kubwera kwake.
Son tonnerre l'annonce, et les troupeaux font connaître qu'il s'approche.

< Yobu 36 >