< Yobu 34 >

1 Pamenepo Elihu anapitiriza kuyankhula kuti,
ויען אליהוא ויאמר
2 “Imvani mawu anga, inu anthu anzeru; tcherani khutu inu anthu ophunzira.
שמעו חכמים מלי וידעים האזינו לי
3 Pakuti khutu limayesa mawu monga momwe mʼkamwa mumalawira chakudya.
כי-אזן מלין תבחן וחך יטעם לאכל
4 Tsono tiyeni tizindikire chomwe chili choyenera; tiphunzire pamodzi chomwe chili chabwino.
משפט נבחרה-לנו נדעה בינינו מה-טוב
5 “Yobu akunena kuti, ‘Ndine wosalakwa, koma Mulungu akukana kundiweruza molungama.
כי-אמר איוב צדקתי ואל הסיר משפטי
6 Ngakhale ndine wolungama mtima, akundiyesa wabodza; ngakhale ndine wosachimwa, mivi yake ikundichititsa mabala osachiritsidwa.’
על-משפטי אכזב אנוש חצי בלי-פשע
7 Kodi munthu wofanana ndi Yobu ndani, amene amayankhula zamwano ngati akumwa madzi?
מי-גבר כאיוב ישתה-לעג כמים
8 Iye amayenda ndi anthu ochita zoyipa; amayanjana ndi anthu oyipa mtima.
וארח לחברה עם-פעלי און וללכת עם-אנשי-רשע
9 Paja iye amanena kuti, ‘Munthu sapindula kanthu poyesetsa kukondweretsa Mulungu.’
כי-אמר לא יסכן-גבר-- ברצתו עם-אלהים
10 “Tsono mverani ine, inu anthu anzeru zomvetsa zinthu. Mulungu sangachite choyipa ndi pangʼono pomwe, Wamphamvuzonse sangathe kuchita cholakwa.
לכן אנשי לבב-- שמעו-לי חללה לאל מרשע ושדי מעול
11 Iye amamubwezera munthu molingana ndi ntchito zake; Mulungu amabweretsa pa munthu molingana ndi zomwe amachita.
כי פעל אדם ישלם-לו וכארח איש ימצאנו
12 Nʼchosayembekezeka kuti Mulungu achite cholakwa, kuti Wamphamvuzonse apotoze chilungamo.
אף-אמנם אל לא-ירשיע ושדי לא-יעות משפט
13 Kodi anapatsa Mulungu udindo wolamulira dziko lapansi ndani? Ndani anayika Mulungu kuti azilamulira dziko lonse?
מי-פקד עליו ארצה ומי שם תבל כלה
14 Mulungu akanakhala ndi maganizo oti achotse mzimu wake ndi mpweya wake,
אם-ישים אליו לבו רוחו ונשמתו אליו יאסף
15 zamoyo zonse zikanawonongekeratu ndipo munthu akanabwerera ku fumbi.
יגוע כל-בשר יחד ואדם על-עפר ישוב
16 “Ngati ndinu omvetsa zinthu, imvani izi; mvetserani zimene ndikunena.
ואם-בינה שמעה-זאת האזינה לקול מלי
17 Kodi Mulungu wodana ndi chilungamo angathe kukhala wolamulira? Kodi iwe ungathe kuweruza Wolungama ndi Wamphamvuyo?
האף שונא משפט יחבוש ואם-צדיק כביר תרשיע
18 Kodi si Iye amene amanena kwa mafumu kuti, ‘Ndinu opanda pake,’ ndipo amawuza anthu otchuka, ‘Ndinu oyipa,’
האמר למלך בליעל-- רשע אל-נדיבים
19 Iye sakondera akalonga ndipo salemekeza anthu olemera kupambana osauka, pakuti onsewa ndi ntchito ya manja ake?
אשר לא-נשא פני שרים ולא נכר-שוע לפני-דל כי-מעשה ידיו כלם
20 Iwo amafa mwadzidzidzi, pakati pa usiku; anthu amachita mantha ndipo amamwalira; munthu wamphamvu amachotsedwa popanda dzanja la munthu.
רגע ימתו-- וחצות לילה יגעשו עם ויעברו ויסירו אביר לא ביד
21 “Maso a Mulungu amapenya njira za munthu; amaona mayendedwe ake onse.
כי-עיניו על-דרכי-איש וכל-צעדיו יראה
22 Palibe malo obisika kapena a mdima wandiweyani kumene anthu ochita zoyipa angabisaleko.
אין-חשך ואין צלמות-- להסתר שם פעלי און
23 Mulungu sasowa kuti apitirizebe kufufuza munthu, kuti abwere pamaso pake kudzaweruzidwa.
כי לא על-איש ישים עוד-- להלך אל-אל במשפט
24 Popanda kufufuza, Iye amawononga anthu amphamvu ndipo mʼmalo mwawo amayikamo ena.
ירע כבירים לא-חקר ויעמד אחרים תחתם
25 Pakuti Iyeyo amadziwa bwino ntchito zawo amawagubuduza usiku ndipo amatswanyika.
לכן--יכיר מעבדיהם והפך לילה וידכאו
26 Iye amawalanga chifukwa cha kuyipa kwawo, pamalo pamene aliyense akuwaona;
תחת-רשעים ספקם-- במקום ראים
27 Chifukwa anasiya kumutsata ndipo sasamaliranso njira zake zonse.
אשר על-כן סרו מאחריו וכל-דרכיו לא השכילו
28 Anachititsa amphawi kuti kulira kwawo kufike pamaso pake, kotero Iyeyo anamva kulira kwa amphawiwo.
להביא עליו צעקת-דל וצעקת עניים ישמע
29 Koma ngati Mulungu akhala chete, ndani angamunene kuti walakwa? Akabisa nkhope yake, ndani angathe kumupenyabe? Komatu ndiye amene amayangʼana za munthu komanso mtundu wa anthu,
והוא ישקט ומי ירשע-- ויסתר פנים ומי ישורנו ועל-גוי ועל-אדם יחד
30 kuti asalamuliridwe ndi anthu osapembedza, kuti asatchere anthu misampha.
ממלך אדם חנף-- ממקשי עם
31 “Mwina munthu atanena kwa Mulungu kuti, ‘Ndine wolakwa koma sindidzachimwanso,
כי-אל-אל האמר נשאתי-- לא אחבל
32 ndiphunzitseni zimene sindikuziona ngati ndachita choyipa, sindidzachitanso.’
בלעדי אחזה אתה הרני אם-עול פעלתי לא אסיף
33 Kodi Mulungu akuweruzeni potsata mmene inuyo mukuganizira, pamene inu mukukana kulapa? Chisankho nʼchanu, osati changa; tsono ndiwuzeni zomwe mukudziwa.
המעמך ישלמנה כי-מאסת--כי-אתה תבחר ולא-אני ומה-ידעת דבר
34 “Anthu omvetsa zinthu adzakambirana, anthu anzeru amene akundimva adzandiwuza kuti,
אנשי לבב יאמרו לי וגבר חכם שמע לי
35 ‘Yobu akuyankhula mopanda nzeru; mawu ake ndi opanda fundo.’
איוב לא-בדעת ידבר ודבריו לא בהשכיל
36 Aa, kunali bwino Yobu akanayesedwa mpaka kumapeto chifukwa choyankha ngati munthu woyipa!
אבי--יבחן איוב עד-נצח על-תשבת באנשי-און
37 Pa tchimo lake amawonjezerapo kuwukira; amawomba mʼmanja mwake monyoza pakati pathu, ndipo amachulukitsa mawu otsutsana ndi Mulungu.”
כי יסיף על-חטאתו פשע בינינו יספוק וירב אמריו לאל

< Yobu 34 >