< Yobu 33 >

1 “Koma tsopano, inu abambo Yobu chonde mverani mawu anga; mutcherere khutu zonse zimene ndinene.
約伯啊,請聽我的話, 留心聽我一切的言語。
2 Tsopano ndiyamba kuyankhula; mawu anga ali pa msonga ya lilime langa.
我現在開口, 用舌發言。
3 Mawu anga akuchokera mu mtima wolungama; pakamwa panga pakuyankhula zoonadi zimene ndikuzidziwa.
我的言語要發明心中所存的正直; 我所知道的,我嘴唇要誠實地說出。
4 Mzimu wa Mulungu wandiwumba, mpweya wa Wamphamvuzonse umandipatsa moyo.
上帝的靈造我; 全能者的氣使我得生。
5 Mundiyankhe ngati mungathe; konzekani tsopano kuti munditsutse.
你若回答我, 就站起來,在我面前陳明。
6 Ine ndili monga inu pamaso pa Mulungu; nanenso ndinachokera ku dothi.
我在上帝面前與你一樣, 也是用土造成。
7 Musachite mantha ndipo musandiope ayi, Ine sindikupanikizani kwambiri ayi.
我不用威嚴驚嚇你, 也不用勢力重壓你。
8 “Koma inu mwayankhula ine ndikumva, ndamva mawu anuwo onena kuti,
你所說的,我聽見了, 也聽見你的言語,說:
9 ‘Ndine wolungama mtima ndi wopanda tchimo; ndine woyera mtima ndipo ndilibe cholakwa.
我是清潔無過的,我是無辜的; 在我裏面也沒有罪孽。
10 Komatu Mulungu wapeza zifukwa zoti anditsutsire nazo; Iye akundiyesa ngati mdani wake.
上帝找機會攻擊我, 以我為仇敵,
11 Iyeyo wamanga mapazi anga mʼzigologolo, akulonda mayendedwe anga onse.’
把我的腳上了木狗, 窺察我一切的道路。
12 “Koma ine ndi kuti kwa inu, inuyo simukukhoza pa zimenezi, pakuti Mulungu ndi wamkulu kupambana munthu.
我要回答你說:你這話無理, 因上帝比世人更大。
13 Chifukwa chiyani mukudandaula kwa Iye kuti sayankha mawu ena aliwonse a munthu?
你為何與他爭論呢? 因他的事都不對人解說?
14 Pajatu Mulungu amayankhula mwa njira zosiyanasiyana, ngakhale munthu sazindikira zimenezi.
上帝說一次、兩次, 世人卻不理會。
15 Mʼmaloto, mʼmasomphenya usiku, pamene anthu ali mʼtulo tofa nato pamene akungosinza chabe pa bedi,
人躺在床上沉睡的時候, 上帝就用夢和夜間的異象,
16 amawanongʼoneza mʼmakutu ndi kuwaopseza ndi machenjezo ake,
開通他們的耳朵, 將當受的教訓印在他們心上,
17 kumuchotsa munthu ku zoyipa, ndi kuthetseratu kunyada kwake,
好叫人不從自己的謀算, 不行驕傲的事,
18 kumulanditsa munthu ku manda, kuti moyo wake usawonongeke ndi lupanga.
攔阻人不陷於坑裏, 不死在刀下。
19 “Mwina Mulungu amalanga munthu ndi matenda ndi ululu ali pa bedi pake, nthawiyo thupi lake lonse limangophwanya,
人在床上被懲治, 骨頭中不住地疼痛,
20 kuti asakhalenso ndi chilakolako cha chakudya, ndipo amanyansidwa ndi chakudya chabwino chomwe.
以致他的口厭棄食物, 心厭惡美味。
21 Thupi lake limawonda ndipo mafupa ake, omwe anali obisika, tsopano amaonekera poyera.
他的肉消瘦,不得再見; 先前不見的骨頭都凸出來。
22 Munthuyo amayandikira ku manda, moyo wake umayandikira kwa amene amabweretsa imfa.
他的靈魂臨近深坑; 他的生命近於滅命的。
23 “Koma patakhala mngelo ngati mthandizi, mmodzi mwa ambirimbiri oterewa, adzafotokoza zimene zili zoyenera,
一千天使中, 若有一個作傳話的與上帝同在, 指示人所當行的事,
24 kudzamukomera mtima ndi kunena kuti, ‘Mupulumutseni kuti asapite ku manda; ine ndapeza cholowa mʼmalo mwa moyo wake,’
上帝就給他開恩, 說:救贖他免得下坑; 我已經得了贖價。
25 pamenepo thupi lake lidzasanduka lasee ngati la mwana; ndipo adzabwezeretsedwanso kukhala ngati mʼmasiku a unyamata wake.
他的肉要比孩童的肉更嫩; 他就返老還童。
26 Akapemphera kwa Mulungu, iyeyo adzalandiridwa. Mulungu adzamulandira mwa chimwemwe ndipo adzamubwezeretsa pamalo ake oyamba.
他禱告上帝, 上帝就喜悅他, 使他歡呼朝見上帝的面; 上帝又看他為義。
27 Ndipo adzabwera kwa anzake ndi kunena kuti, ‘Ndinachimwa ndipo sindinachite zolungama, koma sindinalangidwe koyenerana ndi kuchimwa kwanga.
他在人前歌唱說: 我犯了罪,顛倒是非, 這竟與我無益。
28 Iye anapulumutsa moyo wanga kuti usapite ku manda, ndipo ndidzakhala ndi moyo ndi kuonanso kuwala kwa dzuwa.’
上帝救贖我的靈魂免入深坑; 我的生命也必見光。
29 “Mulungu amachita zonsezi kwa munthu kawirikawiri,
上帝兩次、三次向人行這一切的事,
30 kupulumutsa moyo wa munthuyo ku manda, kuti athe kuonanso kuwala kwa moyo.
為要從深坑救回人的靈魂, 使他被光照耀,與活人一樣。
31 “Abambo Yobu, tcherani khutu ndipo mundimvere; khalani chete kuti ndiyankhule.
約伯啊,你當側耳聽我的話, 不要作聲,等我講說。
32 Ngati muli nʼchoti munene, ndiyankheni; yankhulani, pakuti ine ndikufuna mupezeke wolungama.
你若有話說,就可以回答我; 你只管說,因我願以你為是。
33 Koma ngati sichoncho, mundimvere; khalani chete ndipo ine ndidzakuphunzitsani nzeru.”
若不然,你就聽我說; 你不要作聲,我便將智慧教訓你。

< Yobu 33 >