< Yobu 31 >

1 “Ndinachita pangano ndi maso anga kuti sindidzapenya namwali momusirira.
Fiz concerto com os meus olhos: como pois attentaria n'uma virgem?
2 Kodi Mulungu kumwambako wandisungira zotani? Kodi cholowa changa chochokera kwa Wamphamvuzonse kumwambako nʼchotani?
Porque qual seria a parte de Deus de cima? ou a herança do Todo-poderoso para mim desde as alturas?
3 Kodi si chiwonongeko kwa anthu oyipa, tsoka kwa iwo amene amachita zolakwa?
Porventura não é a perdição para o perverso, o desastre para os que obram iniquidade?
4 Kodi Mulungu saona zochita zanga, ndi kudziwa mayendedwe anga?
Ou não vê elle os meus caminhos, e não conta todos os meus passos?
5 “Ngati ndachita zinthu mwachiphamaso, kapena kufulumira kukachita zachinyengo,
Se andei com vaidade, e se o meu pé se apressou para o engano
6 Mulungu andiyeze ndi muyeso wake wolungama ndipo Iye adzadziwa kuti ine ndine wosalakwa,
(Pese-me em balanças fieis, e saberá Deus a minha sinceridade),
7 ngati mayendedwe anga asempha njira, ngati mtima wanga wakhumbira zimene maso anga aona, kapena ngati ndachita choyipa chilichonse.
Se os meus passos se desviavam do caminho, e se o meu coração segue os meus olhos, e se ás minhas mãos se apegou coisa alguma,
8 Pamenepo ena adye zimene ndinadzala, ndipo zomera zanga zizulidwe.
Então semeie eu e outro coma, e seja a minha descendencia arrancada até á raiz.
9 “Ngati mtima wanga unakopekapo ndi mkazi, ndipo ngati ndinalakalaka mkazi wa mnansi wanga,
Se o meu coração se deixou seduzir por uma mulher, ou se eu armei traições á porta do meu proximo,
10 pamenepo mkazi wanga aphikire mwamuna wina chakudya, ndipo amuna ena azigona naye.
Então môa minha mulher para outro, e outros se encurvem sobre ella.
11 Pakuti zimenezo zikanakhala zochititsa manyazi, tchimo loyenera kulangidwa nalo.
Porque é uma infamia, e é delicto pertencente aos juizes.
12 Ndi moto umene umayaka mpaka chiwonongeko; ukanapsereza zokolola zanga.
Porque fogo é que consomem até á perdição, e desarreigaria toda a minha renda.
13 “Ngati ndinkapondereza mlandu wa akapolo anga aamuna kapena aakazi, pamene ankabwera kwa ine ndi milandu yawo,
Se desprezei o direito do meu servo ou da minha serva, quando elles contendiam comigo,
14 ndidzatani pamene Mulungu adzanditsutsa? Nanga ndidzayankha chiyani akadzandifunsa?
Então que faria eu quando Deus se levantasse? e, inquirindo a causa, que lhe responderia?
15 Kodi amene anapanga ine mʼmimba mwa amayi anga si yemwe anapanganso iwo? Kodi si mmodzi yemweyo amene anatipanga tonsefe mʼmimba mwa amayi athu?
Aquelle que me fez no ventre não o fez tambem a elle? ou não nos formou do mesmo modo na madre?
16 “Ngati ndinawamana aumphawi zinthu zimene ankazikhumba, kapena kuwagwiritsa fuwa lamoto akazi amasiye amene amafuna thandizo kwa ine,
Se retive o que os pobres desejavam, ou fiz desfallecer os olhos da viuva,
17 ngati chakudya changa ndinadya ndekha, wosagawirako mwana wamasiye,
Ou só comi o meu bocado, e o orphão não comeu d'elle
18 chonsechotu kuyambira unyamata wanga ndinamulera monga abambo ake, ndipo moyo wanga wonse ndakhala ndikusamalira akazi amasiye,
(Porque desde a minha mocidade cresceu comigo como com seu pae, e o guiei desde o ventre de minha mãe),
19 ngati ndinaona wina aliyense akuzunzika ndi usiwa, kapena munthu wosauka alibe chofunda,
Se a alguem vi perecer por falta de vestido, e ao necessitado por não ter coberta,
20 ndipo ngati iyeyo sananditamandepo chifukwa chomufunditsa ndi nsalu ya ubweya wankhosa,
Se os seus lombos me não abençoaram, se elle não se aquentava com as pelles dos meus cordeiros,
21 ngati ndinaopsezapo mwana wamasiye, poganiza kuti ndinali ndi mphamvu mʼbwalo la milandu,
Se eu levantei a minha mão contra o orphão, porquanto na porta via a minha ajuda,
22 pamenepo phewa langa lipokonyeke, mkono wanga ukonyoke polumikizira pake.
Então caia do hombro a minha espadoa, e quebre-se o meu braço do osso.
23 Popeza ine ndinaopa kwambiri chiwonongeko chochokera kwa Mulungu, ndinachitanso mantha ndi ulemerero wake, sindikanatha kuchita zinthu zimenezi.
Porque o castigo de Deus era para mim um assombro, e eu não podia supportar a sua alteza.
24 “Ngati ndinayika mtima wanga pa chuma kapena kunena kwa golide wabwino kwambiri kuti, ‘Iwe ndiye chitetezo changa,’
Se no oiro puz a minha esperança, ou disse ao oiro fino: Tu és a minha confiança;
25 ngati ndinakondwera chifukwa choti chuma changa chinali chambiri, zinthu zimene manja anga anazipeza,
Se me alegrei de que era muita a minha fazenda, e de que a minha mão tinha alcançado muito;
26 ngati pamene ndinaona dzuwa likuwala, kapena mwezi ukuyenda mwa ulemerero wake,
Se olhei para o sol, quando resplandecia, ou para a lua, caminhando gloriosa,
27 ndipo kuti mtima wanga unakopeka nazo nʼkuyika dzanja langa pakamwa mozilemekeza,
E o meu coração se deixou enganar em occulto, e a minha bocca beijou a minha mão,
28 pamenepo zimenezinso zikanakhala machimo oti ndilangidwe nawo, chifukwa ndikanakhala wosakhulupirika kwa Mulungu wakumwamba.
Tambem isto seria delicto pertencente ao juiz: pois assim negaria a Deus que está em cima.
29 “Ngati ndinasangalala ndi kuwonongeka kwa mdani wanga, kapena kusekera mavuto pamene mavuto anamugwera,
Se me alegrei da desgraça do que me tem odio, e se eu exultei quando mal o achou
30 ine sindinachimwe ndi pakamwa panga potulutsa matemberero a mdani wanga kuti awonongeke,
(Tambem não deixei peccar o meu paladar, desejando a sua morte com maldição),
31 ngati anthu amene ndimakhala nawo mʼnyumba mwanga sananenepo kuti, ‘Kodi ndani amene sakhuta ndi chakudya cha Yobu?’
Se a gente da minha tenda não disse: Ah, quem nos désse da sua carne! nunca nos fartariamos d'ella:
32 Komatu mlendo sindinamusiye pa msewu usiku wonse, pakuti khomo langa linali lotsekuka nthawi zonse kwa alendo,
O estrangeiro não passava a noite na rua; as minhas portas abria ao viandante.
33 ngati ndinabisa tchimo langa monga amachitira anthu ena, kubisa kulakwa mu mtima mwanga
Se, como Adão, encobri as minhas transgressões, occultando o meu delicto no meu seio;
34 chifukwa choopa gulu la anthu, ndi kuchita mantha ndi mnyozo wa mafuko kotero ndinakhala chete ndipo sindinatuluke panja.
Porque eu temia a grande multidão, e o desprezo das familias me apavoraria, e eu me calaria, e não sairia da porta.
35 “Aa, pakanakhala wina wondimva! Tsopano ndikutsiriza mawu anga odzitetezera. Wamphamvuzonse andiyankhe; mdani wanga achite kulemba pa kalata mawu ake ondineneza.
Ah quem me dera um que me ouvisse! eis que o meu intento é que o Todo-poderoso me responda, e que o meu adversario escreva um livro.
36 Ndithu ine ndikanakoleka kalatayo pa phewa langa, ndikanayivala kumutu ngati chipewa chaufumu.
Por certo que o levaria sobre o meu hombro, sobre mim o ataria por corôa.
37 Ndikanamufotokozera zonse zimene ndinachita; ndikanafika pamaso pake ngati kalonga.
O numero dos meus passos lhe mostraria: como principe me chegaria a elle.
38 “Ngati minda yanga ikulira monditsutsa ine ndipo malo ake onse osalimidwa anyowa ndi misozi,
Se a minha terra clamar contra mim, e se os seus regos juntamente chorarem,
39 ngati ndinadya za mʼminda mwake osapereka ndalama kapena kukhumudwitsa anthu olima mʼmindamo,
Se comi a sua novidade sem dinheiro, e suffoquei a alma dos seus donos,
40 pamenepo mʼmindamo mumere namsongole mʼmalo mwa tirigu ndi udzu mʼmalo mwa barele.” Mawu a Yobu athera pano.
Por trigo me produza cardos, e por cevada joio. Acabaram-se as palavras de Job.

< Yobu 31 >