< Yobu 30 >

1 “Koma tsopano akundinyoza, ana angʼonoangʼono kwa ine, anthu amene makolo awo sindikanawalola kuti azithandizana ndi agalu anga kuweta nkhosa zanga.
Nunc autem derident me iuniores tempore, quorum non dignabar patres ponere cum canibus gregis mei:
2 Kodi mphamvu zawo ndi za phindu lanji kwa ine, pakuti mphamvu zawo zinatha kale?
Quorum virtus manuum mihi erat pro nihilo, et vita ipsa putabantur indigni.
3 Anali atatheratu kuwonda ndi njala, ankayendayenda mʼdziko lopanda madzi, mʼchipululu usiku.
Egestate et fame steriles, qui rodebant in solitudine, squallentes calamitate, et miseria.
4 Ankathyola therere ndi masamba owawa, ndipo chakudya chawo chinali mizu ya mitengo ya masache.
Et mandebant herbas, et arborum cortices, et radix iuniperorum erat cibus eorum.
5 Anapirikitsidwa pakati pa anthu anzawo, akuwakuwiza ngati kuti anali akuba.
Qui de convallibus ista rapientes, cum singula reperissent, ad ea cum clamore currebant.
6 Anawumirizidwa kukhala ku zigwembe za mitsinje yowuma, pakati pa matanthwe ndi mʼmaenje a mʼnthaka.
In desertis habitabant torrentium, et in cavernis terrae, vel super glaream.
7 Ankalira ngati nyama kuthengo ndipo ankawunjikana pamodzi pa ziyangoyango.
Qui inter huiuscemodi laetabantur, et esse sub sentibus delicias computabant.
8 Anali anthu achabechabe ndi wopanda dzina, anathamangitsidwa mʼdziko.
Filii stultorum et ignobilium, et in terra penitus non parentes.
9 “Ndipo tsopano ana awo akundiyimba nyimbo zachipongwe; ineyo ndasanduka chisudzo chawo.
Nunc in eorum canticum versus sum, et factus sum eis in proverbium.
10 Iwo amanyansidwa nane ndipo amandithawa; akandiona salephera kundilavulira mʼmaso mwangamu.
Abominantur me, et longe fugiunt a me, et faciem meam conspuere non verentur.
11 Tsopano pakuti Mulungu wakhwefula uta wanga ndipo wandisautsa, iwowo analekeratu kundiopa.
Pharetram enim suam aperuit, et afflixit me, et frenum posuit in os meum.
12 Ku dzanja langa lamanja anthu akulimbana nane; andikumbira dzenje loti ndigweremo ndikamayenda, andipangira mitumbira ya nkhondo kuti alimbane nane.
Ad dexteram orientis calamitatis meae illico surrexerunt: pedes meos subverterunt, et oppresserunt quasi fluctibus semitis suis.
13 Iwo anditsekera njira; akufuna kundichititsa ngozi, popanda wina aliyense wowaletsa.
Dissipaverunt itinera mea, insidiati sunt mihi, et praevaluerunt, et non fuit qui ferret auxilium.
14 Akundithamangitsa ngati madzi olowera pa mpanda wobowoka, iwo akubwererabwerera pakati pa chipasupasu.
Quasi rupto muro, et aperta ianua, irruerunt super me, et ad meas miserias devoluti sunt.
15 Zoopsa zandithetsa mphamvu; ulemu wanga wachita ngati wauluzika ndi mphepo, chuma changa chija chazimirira ngati mtambo.
Redactus sum in nihilum: abiit quasi ventus desiderium meum: et velut nubes pertransiit salus mea.
16 “Ndipo tsopano mtima wanga wachokamo; ndili mʼmasiku amasautso.
Nunc autem in memetipso marcescit anima mea, et possident me dies afflictionis.
17 Mafupa anga akuphwanya usiku pakuti zowawa zanga sizikuleka.
Nocte os meum perforatur doloribus: et qui me comedunt, non dormiunt.
18 Mʼmphamvu zake Mulungu wakhala ngati chovala changa; Iye wandigwira ngati chovala chondithina pa khosi.
In multitudine eorum consumitur vestimentum meum, et quasi capito tunicae succinxerunt me.
19 Wandiponya mʼmatope, ndipo ndasanduka ngati fumbi ndi phulusa.
Comparatus sum luto, et assimilatus sum favillae et cineri.
20 “Inu Mulungu, ine ndikulirira kwa Inu, koma simukundiyankha; ndikayimirira, Inu simundiyangʼana nʼkomwe.
Clamo ad te, et non exaudis me: sto, et non respicis me.
21 Inuyo mumandichitira zankhanza; mumandizunza ndi dzanja lanu lamphamvu.
Mutatus es mihi in crudelem, et in duritia manus tuae adversaris mihi.
22 Mwandinyamulira ku mphepo ndipo mwandiwulutsa ndi mphepoyo; mwandiponya mʼmphepo ya mkuntho.
Elevasti me, et quasi super ventum ponens elisisti me valide.
23 Ndikudziwa kuti Inu mudzandifikitsa ku imfa, kumalo kumene amoyo onse adzapitako.
Scio quia morti trades me, ubi constituta est domus omni viventi.
24 “Ndithudi palibe munthu amene amalanga munthu wosweka mtima, amene akupempha thandizo mʼmasautso ake.
Verumtamen non ad consumptionem meam emittis manum tuam: et si corruerim, ipse salvabis.
25 Kodi ine sindinalire nawo iwo amene anali pamavuto? Kodi mtima wanga sunamvere chisoni anthu osauka?
Flebam quondam super eo, qui afflictus erat, et compatiebatur anima mea pauperi.
26 Koma pamene ndinkayembekezera zabwino, zoyipa ndiye zinandigwera; pamene ndinkafunafuna kuwala, mdima ndiye unandigwera.
Expectabam bona, et venerunt mihi mala: praestolabar lucem, et eruperunt tenebrae.
27 Kuwawa kwa mʼkati mwanga sikukuleka; ndili mʼmasiku amasautso.
Interiora mea efferbuerunt absque ulla requie, praevenerunt me dies afflictionis.
28 Ndikuyenda wothimbirira, komatu osati ndi dzuwa; ndimayimirira pa msonkhano ndi kupempha chithandizo molira.
Moerens incedebam, sine furore, consurgens, in turba clamabam.
29 Ndasanduka mʼbale wa nkhandwe, mnzawo wa akadzidzi.
Frater fui draconum, et socius struthionum.
30 Khungu langa layamba kuda ndipo likufunduka; thupi langa likutentha chifukwa cha kuphwanya kwa thupi.
Cutis mea denigrata est super me, et ossa mea aruerunt prae caumate.
31 Pangwe wanga wasanduka woyimbira maliro, ndipo chitoliro changa chikuyimbira anthu olira.
Versa est in luctum cithara mea, et organum meum in vocem flentium.

< Yobu 30 >