< Yobu 3 >

1 Pambuyo pake Yobu anatsekula pakamwa pake nayamba kutemberera tsiku limene iyeyo anabadwa.
Potem Hiob otworzył swoje usta i przeklinał swój dzień.
2 Ndipo Yobu anati:
Hiob odezwał się i zawołał:
3 “Tsiku limene ine ndinabadwa litembereredwe ndi usiku umene ananena kuti, ‘Mwana wamwamuna wabadwa!’
Niech zginie dzień, w którym się urodziłem, i noc, [w którą] powiedziano: Poczęty mężczyzna.
4 Tsiku limenelo lisanduke mdima; Mulungu wa kumwambako asalilabadirenso; kuwala kusaonekenso pa tsikulo.
Niech ten dzień stanie się ciemnością, niech o niego nie troszczy się Bóg z wysokości i nie oświetla go światłość.
5 Mdima ndi mthunzi wa imfa zikhale pa tsiku limeneli; mtambo uphimbe tsikuli; mdima wandiweyani udetse kuwala kwake.
Niech go pokryje ciemność i cień śmierci, niech go ogarnie obłok i przerazi mrok dnia.
6 Usiku umenewo ukutidwe ndi mdima wandiweyani; usawerengedwenso pamodzi ndi masiku a chaka, kapena kukhala pa mwezi wina uliwonse.
Niech tą nocą zawładnie ciemność, niech nie będzie liczona wśród dni roku [i] nie wejdzie w liczbę miesięcy.
7 Usiku umenewo usabweretse chilichonse chabwino; kusamvekenso nthungululu za chikondwerero.
Niech ta noc będzie samotna, niech nie będzie w niej radosnego śpiewu.
8 Odziwa kutemberera masiku alitemberere tsikulo, iwo amene akonzekera kuwutsa Leviyatani.
Niech przeklną ją ci, którzy przeklinają dzień, którzy są gotowi podnieść swój lament.
9 Nyenyezi zake za mʼbandakucha zikhale mdima; tsikulo liyembekezere kucha pachabe ndipo lisaonenso kuwala koyamba kwa mʼbandakucha.
Niech gwiazdy zaćmią się [o] zmierzchu, niech nie doczeka się światła ani nie zobaczy zorzy porannej;
10 Pakuti tsiku limenelo ndiye ndinatuluka mʼmimba ya amayi anga ndipo ndi limene linandionetsa zovuta.
Bo nie zamknęła drzwi łona mej [matki] i nie ukryła smutku przed moimi oczami.
11 “Bwanji ine sindinawonongeke pamene ndinkabadwa ndi kufa pamene ndimatuluka mʼmimba?
Czemu nie umarłem w łonie? [Czemu] nie zginąłem, kiedy wyszedłem z łona?
12 Chifukwa chiyani panali mawondo wondilandirirapo ndi mawere woti andiyamwitsepo?
Czemu przyjęły mnie kolana? Czemu [przyjęły mnie] piersi, abym mógł [je] ssać?
13 Pakuti tsopano bwenzi ndili gone mwamtendere; ndikanakhala nditagona tulo ndili pa mpumulo
Teraz bowiem leżałbym i trwał w spokoju, spałbym i odpoczywał;
14 pamodzi ndi mafumu ndi aphungu a dziko lapansi, amene anadzimangira nyumba zikuluzikulu zimene tsopano ndi mabwinja,
Z królami i z doradcami ziemi, którzy sobie budowali opustoszałe miejsca;
15 pamodzi ndi olamulira amene anali ndi golide, amene anadzaza nyumba zawo ndi siliva.
Albo z książętami, którzy mieli złoto i napełnili swe domy srebrem;
16 Kapena, bwanji sindinakwiriridwe pansi monga mwana wobadwa wakufa kale, ngati khanda limene silinaone kuwala kwa dzuwa?
Albo [czemu] nie stałem się jak ukryty, martwy płód, jak niemowlęta, [które] nie widziały światła?
17 Ku mandako anthu oyipa sakhalanso pa mavuto, ndipo kumeneko anthu otopa ali pa mpumulo.
Tam bezbożni przestają straszyć, tam pozbawieni siły odpoczywają.
18 A mʼndende kumeneko akusangalala ndi mtendere; sakumvanso mawu ofuwula a kapitawo wa akapolo.
Tam więźniowie razem wypoczywają i nie słyszą głosu ciemięzcy.
19 Anthu wamba ndi anthu apamwamba ali kumeneko, ndipo kapolo ndi womasuka kwa mbuye wake.
Mały i wielki [są] tam sobie równi i niewolnik jest wolny od swego pana.
20 “Chifukwa chiyani dzuwa limawalira iwo amene ali pa mavuto, ndipo moyo umapatsidwa kwa owawidwa mtima,
Czemu nędznemu dane jest światło, a życie [tym], którzy są rozgoryczeni na duszy;
21 kwa iwo amene amalakalaka imfa imene sibwera, amene amayifunafuna imfayo kupambana chuma chobisika,
Którzy z tęsknotą wypatrują śmierci, a [ta] nie przychodzi, choć jej szukają pilniej niż ukrytych skarbów;
22 amene amakondwa ndi kusangalala akamalowa mʼmanda?
Którzy wielce się radują i cieszą, kiedy grób znajdują?
23 Chifuwa chiyani moyo umaperekedwa kwa munthu amene njira yake yabisika, amene Mulungu wamuzinga ponseponse?
[Czemu dane jest światło] człowiekowi, którego droga jest ukryta i którego Bóg osaczył?
24 Mʼmalo moti ndidye, ndimalira, ndi kubuwula kwanga nʼkosalekeza.
Kiedy bowiem mam jeść, przychodzi moje wzdychanie, a moje jęki rozchodzą się jak woda;
25 Chimene ndinkachiopa chandigwera; chimene ndinkachita nacho mantha chandichitikira.
Bo to, czego się bałem, spotkało mnie, a to, czego się obawiałem, spadło na mnie.
26 Ndilibe mtendere kapena bata, ndilibe mpumulo, koma mavuto okhaokha.”
Nie byłem bezpieczny, nie miałem spokoju ani odpoczynku, a jednak nadeszła trwoga.

< Yobu 3 >