< Yobu 3 >

1 Pambuyo pake Yobu anatsekula pakamwa pake nayamba kutemberera tsiku limene iyeyo anabadwa.
After this Job opened his mouth, and cursed his day.
2 Ndipo Yobu anati:
And Job answered and said,
3 “Tsiku limene ine ndinabadwa litembereredwe ndi usiku umene ananena kuti, ‘Mwana wamwamuna wabadwa!’
Let the day perish in which I was born, and the night which said, There is a man-child conceived.
4 Tsiku limenelo lisanduke mdima; Mulungu wa kumwambako asalilabadirenso; kuwala kusaonekenso pa tsikulo.
Let that day be darkness. Let not God from above seek for it, nor let the light shine upon it.
5 Mdima ndi mthunzi wa imfa zikhale pa tsiku limeneli; mtambo uphimbe tsikuli; mdima wandiweyani udetse kuwala kwake.
Let darkness and the shadow of death claim it for their own. Let a cloud dwell upon it. Let blackness come upon it.
6 Usiku umenewo ukutidwe ndi mdima wandiweyani; usawerengedwenso pamodzi ndi masiku a chaka, kapena kukhala pa mwezi wina uliwonse.
As for that night, let thick darkness seize upon it. Let it not rejoice among the days of the year. Let it not come into the number of the months.
7 Usiku umenewo usabweretse chilichonse chabwino; kusamvekenso nthungululu za chikondwerero.
Lo, let that night be barren. Let no joyful voice come in it.
8 Odziwa kutemberera masiku alitemberere tsikulo, iwo amene akonzekera kuwutsa Leviyatani.
Let them curse it who curse the day, who are ready to rouse up leviathan.
9 Nyenyezi zake za mʼbandakucha zikhale mdima; tsikulo liyembekezere kucha pachabe ndipo lisaonenso kuwala koyamba kwa mʼbandakucha.
Let the stars of the twilight of it be dark. Let it look for light, but have none, nor let it behold the eyelids of the morning.
10 Pakuti tsiku limenelo ndiye ndinatuluka mʼmimba ya amayi anga ndipo ndi limene linandionetsa zovuta.
Because it did not shut up the doors of my mother's womb, nor hide trouble from my eyes.
11 “Bwanji ine sindinawonongeke pamene ndinkabadwa ndi kufa pamene ndimatuluka mʼmimba?
Why did I not die from the womb? Why did I not give up the spirit when my mother bore me?
12 Chifukwa chiyani panali mawondo wondilandirirapo ndi mawere woti andiyamwitsepo?
Why did the knees receive me? Or why the breast, that I should suck?
13 Pakuti tsopano bwenzi ndili gone mwamtendere; ndikanakhala nditagona tulo ndili pa mpumulo
For now I should have lain down and been quiet. I should have slept. Then I would have been at rest
14 pamodzi ndi mafumu ndi aphungu a dziko lapansi, amene anadzimangira nyumba zikuluzikulu zimene tsopano ndi mabwinja,
with kings and counselors of the earth, who built waste places for themselves,
15 pamodzi ndi olamulira amene anali ndi golide, amene anadzaza nyumba zawo ndi siliva.
or with rulers who had gold, who filled their houses with silver.
16 Kapena, bwanji sindinakwiriridwe pansi monga mwana wobadwa wakufa kale, ngati khanda limene silinaone kuwala kwa dzuwa?
Or I should have been as a hidden untimely birth, as infants that never saw light.
17 Ku mandako anthu oyipa sakhalanso pa mavuto, ndipo kumeneko anthu otopa ali pa mpumulo.
There the wicked cease from troubling, and there the weary are at rest.
18 A mʼndende kumeneko akusangalala ndi mtendere; sakumvanso mawu ofuwula a kapitawo wa akapolo.
There the prisoners are at ease together. They do not hear the voice of the taskmaster.
19 Anthu wamba ndi anthu apamwamba ali kumeneko, ndipo kapolo ndi womasuka kwa mbuye wake.
The small and the great are there. And the servant is free from his master.
20 “Chifukwa chiyani dzuwa limawalira iwo amene ali pa mavuto, ndipo moyo umapatsidwa kwa owawidwa mtima,
Why is light given to him who is in misery, and life to the bitter in soul,
21 kwa iwo amene amalakalaka imfa imene sibwera, amene amayifunafuna imfayo kupambana chuma chobisika,
who long for death, but it comes not, and dig for it more than for hid treasures,
22 amene amakondwa ndi kusangalala akamalowa mʼmanda?
who rejoice exceedingly, and are glad when they can find the grave?
23 Chifuwa chiyani moyo umaperekedwa kwa munthu amene njira yake yabisika, amene Mulungu wamuzinga ponseponse?
Why is light given to a man whose way is hid, and whom God has hedged in?
24 Mʼmalo moti ndidye, ndimalira, ndi kubuwula kwanga nʼkosalekeza.
For my sighing comes before I eat, and my groanings are poured out like water.
25 Chimene ndinkachiopa chandigwera; chimene ndinkachita nacho mantha chandichitikira.
For the thing which I fear comes upon me, and that which I am afraid of comes to me.
26 Ndilibe mtendere kapena bata, ndilibe mpumulo, koma mavuto okhaokha.”
I am not at ease, nor am I quiet, neither have I rest, but trouble comes.

< Yobu 3 >