< Yobu 22 >

1 Pamenepo Elifazi wa ku Temani anayankha kuti,
Så tog Temaniten Elifaz til Orde og sagde:
2 “Kodi munthu nʼkukhala waphindu kwa Mulungu? Kodi munthu wanzeru angamupindulire Iye?
"Gavner et Menneske Gud? Nej, den kloge gavner sig selv.
3 Kodi Wamphamvuzonse akanapeza chabwino chotani iweyo ukanakhala wolungama? Kodi iyeyo akanapeza phindu lanji makhalidwe ako akanakhala angwiro?
Har den Almægtige godt af din Retfærd, Vinding af, at din Vandel er ret?
4 “Kodi nʼchifukwa choti umamuopa, kuti azikudzudzula, kuti azifuna kukukokera ku mlandu?
Revser han dig for din Gudsfrygt? Eller går han i Rette med dig derfor?
5 Kodi osati nʼchifukwa chakuti kuyipa kwako nʼkwakukulu? Kodi machimo ako si opanda malire?
Er ikke din Ondskab stor og din Brøde uden Ende?
6 Iwe unkawumiriza abale ako kuti akupatse chikole popanda chifukwa; umalanda anthu zovala zawo ndi kuwasiya amaliseche.
Thi du pantede Brødre uden Grund, trak Klæderne af de nøgne,
7 Sunawapatse madzi anthu otopa, ndipo unawamana chakudya anthu anjala,
gav ikke den trætte Vand at drikke og nægted den sultne Brød.
8 ngakhale unali munthu wamphamvu, wokhala ndi malo akeake, munthu waulemu wake, wokhala mʼdzikomo.
Den mægtige - hans var Landet, den hædrede boede der.
9 Ndipo akazi amasiye unawachotsa wopanda kanthu, ndipo unapondereza ana amasiye.
Du lod Enker gå tomhændet bort, knuste de faderløses Arme.
10 Nʼchifukwa chake misampha yakuzungulira, nʼchifukwa chake tsoka ladzidzidzi lakuchititsa mantha,
Derfor var der Snaret omkring dig, og Rædsel ængsted dig brat.
11 nʼchifukwa chake kuli mdima kuti sungathe kuona kanthu, nʼchifukwa chakenso madzi achigumula akumiza.
Dit Lys blev Mørke, du kan ej se, og Strømme af Vand går over dig!
12 “Kodi Mulungu sali kutalitali kumwamba? Ndipo ona nyenyezi zili mmwamba kwambirizo, ona kutalika kwake pamene zililipo!
Er Gud ej i højen Himmel? Se Stjernernes Tinde, hvor højt de står!
13 Komabe iweyo ukunena kuti, ‘Kodi Mulungu amadziwa chiyani? Kodi Iye amaweruza mu mdima woterewu?
Dog siger du: "Hvad ved Gud, holder han Dom bag sorten Sky?
14 Mitambo yakuda yamuphimba, kotero kuti Iye sakutiona pamene akuyendayenda pamwamba pa thambopo.’
Skyerne skjuler ham, så han ej ser, på Himlens Runding går han!"
15 Kodi iwe udzayendabe mʼnjira yakale imene anthu oyipa ankayendamo?
Vil du følge Fortidens Sti, som Urettens Mænd betrådte,
16 Iwo anachotsedwa nthawi yawo isanakwane, maziko awo anakokoloka ndi madzi achigumula.
de, som i Utide reves bort, hvis Grundvold flød bort som en Strøm,
17 Anthuwo anati kwa Mulungu, ‘Tichokereni! Kodi Wamphamvuzonse angatichitire chiyani?’
som sagde til Gud: "Gå fra os! Hvad kan den Almægtige gøre os?"
18 Chonsecho ndi Iye amene anadzaza nyumba zawo ndi zinthu zabwino, choncho ine sindigwirizana ndi uphungu wa anthu oyipa.
Og han havde dog fyldt deres Huse med godt. Men de gudløses Råd er ham fjernt.
19 “Anthu olungama amaona kuwonongeka kwawo ndipo amakondwera; anthu osalakwa amangoseka, akamuona woyipa akulangidwa.
De retfærdige så det og glædede sig, den uskyldige spottede dem:
20 Amanena kuti, ‘Ndithudi adani athu awonongeka ndipo moto wawononga chuma chawo!’
For vist, vore Fjender forgik, og Ild fortæred de sidste af dem.
21 “Gonjera Mulungu kuti ukhale naye pamtendere; ukatero udzaona zabwino.
Bliv Ven med ham og hold Fred. derved vil der times dig Lykke;
22 Landira malangizo a pakamwa pake ndipo usunge mawu ake mu mtima mwako.
tag dog mod Lærdom af ham og læg dig hans Ord på Sinde!
23 Ukabwerera kwa Wamphamvuzonse udzabwezeretsedwa; ukachotsa zoyipa zonse zimene zimachitika mʼnyumba mwako,
Vender du ydmygt om til den Almægtige, fjerner du Uretten fra dit Telt,
24 ndipo chuma chamtengowapatali nuchiona ngati fumbi, golide wa ku Ofiri numutaya ku miyala ya ku zigwa.
kaster du Guldet på Jorden, Ofirguldet blandt Bækkenes Sten,
25 Pamenepo Wamphamvuzonseyo adzakhala golide wako, siliva wako wamtengowapatali.
så den Almægtige bliver dit Guld, hans Lov dit Sølv,
26 Pamenepo udzakondwera naye Wamphamvuzonse ndipo udzakweza nkhope yako kwa Mulungu.
ja, da skal du fryde dig over den Almægtige og løfte dit Åsyn til Gud.
27 Udzamupempha ndipo adzakumvera, ndipo udzapereka zimene unalonjeza.
Beder du til ham, hører han dig, indfri kan du, hvad du har lovet;
28 Chimene watsimikiza kuti uchite, chidzachitikadi, kuwala kudzakuwunikira pa njira yako.
hvad du sætter dig for, det lykkes, det lysner på dine Veje;
29 Pamene anthu agwetsedwa pansi, iwe nʼkunena kuti, ‘Akwezeni!’ Pamenepo Iye adzapulumutsa anthu oponderezedwa.
thi stolte, hovmodige ydmyger han, men hjælper den, der slår Øjnene ned;
30 Iye adzapulumutsa ngakhale munthu amene ndi wolakwa, ameneyo adzapulumutsidwa kudzera mʼkulungama kwako.”
han frelser uskyldig Mand; det sker ved hans Hænders Renhed!

< Yobu 22 >