< Yobu 20 >

1 Pamenepo Zofari wa ku Naama anayankha kuti
E Zofar, o naamita, respondeu, dizendo:
2 “Kuvutika kwa mʼmaganizo kwanga kwandifulumiza kuti ndiyankhe chifukwa ndasautsidwa kwambiri.
Por isso meus meus pensamentos me fazem responder; por causa da agitação dentro de mim.
3 Ndikumva kudzudzula kondinyoza, ndipo kumvetsetsa kwanga kwa zinthu kwandifulumiza kuti ndiyankhe.
Eu ouvi a repreensão que me envergonha; mas o espírito desde o meu entendimento responderá por mim.
4 “Ndithudi iwe ukudziwa momwe zinthu zakhala zikuchitikira kuyambira kale, kuchoka nthawi imene munthu analengedwa pa dziko lapansi,
Por acaso não sabes isto, [que foi] desde a antiguidade, desde que o ser humano foi posto no mundo?
5 kuti chisangalalo cha woyipa nʼchosachedwa kutha, chimwemwe cha wosapembedza Mulungu nʼchakanthawi kochepa.
Que o júbilo dos perversos é breve, e a alegria do hipócrita [dura apenas] um momento?
6 Ngakhale atamayenda mapewa ake ali mmwamba ndipo mutu wake uli nengʼaa,
Ainda que sua altura subisse até o céu, e sua cabeça chegasse até as nuvens,
7 iye adzatheratu monga momwe imatayikira ndowe yake yomwe; iwo amene ankamuona adzati, ‘Kodi uje uja ali kuti?’
[Mesmo assim] com o seu excremento perecerá para sempre; os que houverem o visto, dirão: Onde ele está?
8 Adzazimirira ngati maloto ndipo sadzapezekanso, adzachotsedwa ngati masomphenya a usiku.
Como um sonho voará, e não será achado; e será afugentado como a visão noturna.
9 Diso limene linamuona silidzamuonanso; sadzapezekanso pamalo pake.
O olho que já o viu nunca mais o verá; nem seu lugar olhará mais para ele.
10 Ana ake adzabwezera zonse zimene iyeyo analanda anthu osauka;
Seus filhos procurarão o favor dos pobres; e suas mãos devolverão a sua riqueza.
11 Mphamvu zaunyamata zimene zili mʼthupi mwake zidzagona naye limodzi mʼfumbi.
Seus ossos estão cheios de sua juventude, que juntamente com ele se deitará no pó.
12 “Ngakhale zoyipa zili zozuna mʼkamwa mwake ndipo amazibisa kunsi kwa lilime lake,
Se o mal é doce em sua boca, e o esconde debaixo de sua língua;
13 ngakhale salola kuzilavula, ndipo amazisunga mʼkamwa mwake,
Se o guarda para si, e não o abandona; ao contrário, o retém em sua boca.
14 koma chakudya chake chidzawawasa mʼmimba mwake; chidzasanduka ngati ndulu ya njoka mʼkati mwa iyeyo.
Sua comida se mudará em suas entranhas, veneno de cobras será em seu interior.
15 Adzachisanza chuma chimene anachimeza; Mulungu adzachitulutsa mʼmimba mwa munthuyo.
Engoliu riquezas, porém as vomitará; Deus as tirará de seu ventre.
16 Iye adzayamwa ndulu ya njoka ndipo ululu wa mphiri udzamupha.
Veneno de cobras subará; língua de víbora o matará.
17 Sadzasangalala ndi timitsinje, mitsinje yoyenda uchi ndi mafuta.
Não verá correntes, rios, [e] ribeiros de mel e de manteiga.
18 Ayenera kubweza zimene anazigwirira ntchito osazidya; sadzasangalala ndi phindu la malonda ake.
Restituirá o trabalho e não o engolirá; da riqueza de seu comério não desfrutará.
19 Pakuti iye anapondereza anthu osauka ndipo anawasiya wopanda thandizo; iyeyo analanda nyumba zimene sanamange.
Pois oprimiu [e] desamparou aos pobres; roubou a casa que não edificou;
20 “Chifukwa choti umbombo wake sutha, sadzatha kusunga chilichonse chimene amakondwera nacho.
Por não ter sentido sossego em seu ventre, nada preservará de sua tão desejada riqueza.
21 Palibe chatsala kuti iye adye; chuma chake sichidzachedwa kutha.
Nada [lhe] restou para que devorasse; por isso sua riqueza não será duradoura.
22 Ngakhale ndi munthu wachuma, mavuto adzamugwera; mavuto aakulu adzamugwera.
Estando cheio de sua fartura, [ainda] estará angustiado; todo o poder da miséria virá sobre ele.
23 Akadya nʼkukhuta, Mulungu adzamugwetsera ukali wamoto ngati mvula yosalekeza.
Quando ele estiver enchendo seu vendre, Deus mandará sobre ele o ardor de sua ira, e [a] choverá sobre ele em sua comida.
24 Ngakhale athawe mkondo wachitsulo, muvi wamkuwa wosongoka udzamulasa.
[Ainda que] fuja das armas de ferro, o arco de bronze o atravessará.
25 Muviwo adzawutulutsira ku msana, songa yake yowala kuchoka mʼmphafa mwake. Adzagwidwa ndi mantha aakulu;
Ele a tirará de [seu] corpo, e a ponta brilhante atingirá seu fígado; haverá sobre ele assombros.
26 mdima wandiweyani ukudikira chuma chake. Moto wopanda wowukoleza udzamupsereza ndi kuwononga zonse zotsala mʼnyumba yake.
Todas as trevas estão reservadas para seus tesouros escondidos; um fogo não assoprado o consumirá; acabará com o que restar em sua tenda.
27 Zamumlengalenga zidzawulula kulakwa kwake; dziko lapansi lidzamuwukira.
Os céus revelarão sua maldade, e a terra se levantará contra ele.
28 Chigumula cha madzi chidzawononga nyumba yake, katundu wake adzatengedwa pa tsiku la ukali wa Mulungu.
As riquezas de sua casa serão transportadas; nos dias de sua ira elas se derramarão.
29 Izi ndi zimene Mulungu amasungira anthu oyipa, mphotho imene Mulungu amayikira iwowo.”
Esta é a parte que Deus dá ao homem perverso, a herança que Deus lhe prepara.

< Yobu 20 >