< Yobu 20 >

1 Pamenepo Zofari wa ku Naama anayankha kuti 2 “Kuvutika kwa mʼmaganizo kwanga kwandifulumiza kuti ndiyankhe chifukwa ndasautsidwa kwambiri. 3 Ndikumva kudzudzula kondinyoza, ndipo kumvetsetsa kwanga kwa zinthu kwandifulumiza kuti ndiyankhe. 4 “Ndithudi iwe ukudziwa momwe zinthu zakhala zikuchitikira kuyambira kale, kuchoka nthawi imene munthu analengedwa pa dziko lapansi, 5 kuti chisangalalo cha woyipa nʼchosachedwa kutha, chimwemwe cha wosapembedza Mulungu nʼchakanthawi kochepa. 6 Ngakhale atamayenda mapewa ake ali mmwamba ndipo mutu wake uli nengʼaa, 7 iye adzatheratu monga momwe imatayikira ndowe yake yomwe; iwo amene ankamuona adzati, ‘Kodi uje uja ali kuti?’ 8 Adzazimirira ngati maloto ndipo sadzapezekanso, adzachotsedwa ngati masomphenya a usiku. 9 Diso limene linamuona silidzamuonanso; sadzapezekanso pamalo pake. 10 Ana ake adzabwezera zonse zimene iyeyo analanda anthu osauka; 11 Mphamvu zaunyamata zimene zili mʼthupi mwake zidzagona naye limodzi mʼfumbi. 12 “Ngakhale zoyipa zili zozuna mʼkamwa mwake ndipo amazibisa kunsi kwa lilime lake, 13 ngakhale salola kuzilavula, ndipo amazisunga mʼkamwa mwake, 14 koma chakudya chake chidzawawasa mʼmimba mwake; chidzasanduka ngati ndulu ya njoka mʼkati mwa iyeyo. 15 Adzachisanza chuma chimene anachimeza; Mulungu adzachitulutsa mʼmimba mwa munthuyo. 16 Iye adzayamwa ndulu ya njoka ndipo ululu wa mphiri udzamupha. 17 Sadzasangalala ndi timitsinje, mitsinje yoyenda uchi ndi mafuta. 18 Ayenera kubweza zimene anazigwirira ntchito osazidya; sadzasangalala ndi phindu la malonda ake. 19 Pakuti iye anapondereza anthu osauka ndipo anawasiya wopanda thandizo; iyeyo analanda nyumba zimene sanamange. 20 “Chifukwa choti umbombo wake sutha, sadzatha kusunga chilichonse chimene amakondwera nacho. 21 Palibe chatsala kuti iye adye; chuma chake sichidzachedwa kutha. 22 Ngakhale ndi munthu wachuma, mavuto adzamugwera; mavuto aakulu adzamugwera. 23 Akadya nʼkukhuta, Mulungu adzamugwetsera ukali wamoto ngati mvula yosalekeza. 24 Ngakhale athawe mkondo wachitsulo, muvi wamkuwa wosongoka udzamulasa. 25 Muviwo adzawutulutsira ku msana, songa yake yowala kuchoka mʼmphafa mwake. Adzagwidwa ndi mantha aakulu; 26 mdima wandiweyani ukudikira chuma chake. Moto wopanda wowukoleza udzamupsereza ndi kuwononga zonse zotsala mʼnyumba yake. 27 Zamumlengalenga zidzawulula kulakwa kwake; dziko lapansi lidzamuwukira. 28 Chigumula cha madzi chidzawononga nyumba yake, katundu wake adzatengedwa pa tsiku la ukali wa Mulungu. 29 Izi ndi zimene Mulungu amasungira anthu oyipa, mphotho imene Mulungu amayikira iwowo.”

< Yobu 20 >