< Yobu 20 >

1 Pamenepo Zofari wa ku Naama anayankha kuti
拿瑪人瑣法回答說:
2 “Kuvutika kwa mʼmaganizo kwanga kwandifulumiza kuti ndiyankhe chifukwa ndasautsidwa kwambiri.
我心中急躁, 所以我的思念叫我回答。
3 Ndikumva kudzudzula kondinyoza, ndipo kumvetsetsa kwanga kwa zinthu kwandifulumiza kuti ndiyankhe.
我已聽見那羞辱我,責備我的話; 我的悟性叫我回答。
4 “Ndithudi iwe ukudziwa momwe zinthu zakhala zikuchitikira kuyambira kale, kuchoka nthawi imene munthu analengedwa pa dziko lapansi,
你豈不知亙古以來, 自從人生在地,
5 kuti chisangalalo cha woyipa nʼchosachedwa kutha, chimwemwe cha wosapembedza Mulungu nʼchakanthawi kochepa.
惡人誇勝是暫時的, 不敬虔人的喜樂不過轉眼之間嗎?
6 Ngakhale atamayenda mapewa ake ali mmwamba ndipo mutu wake uli nengʼaa,
他的尊榮雖達到天上, 頭雖頂到雲中,
7 iye adzatheratu monga momwe imatayikira ndowe yake yomwe; iwo amene ankamuona adzati, ‘Kodi uje uja ali kuti?’
他終必滅亡,像自己的糞一樣; 素來見他的人要說:他在哪裏呢?
8 Adzazimirira ngati maloto ndipo sadzapezekanso, adzachotsedwa ngati masomphenya a usiku.
他必飛去如夢,不再尋見, 速被趕去,如夜間的異象。
9 Diso limene linamuona silidzamuonanso; sadzapezekanso pamalo pake.
親眼見過他的,必不再見他; 他的本處也再見不着他。
10 Ana ake adzabwezera zonse zimene iyeyo analanda anthu osauka;
他的兒女要求窮人的恩; 他的手要賠還不義之財。
11 Mphamvu zaunyamata zimene zili mʼthupi mwake zidzagona naye limodzi mʼfumbi.
他的骨頭雖然有青年之力, 卻要和他一同躺臥在塵土中。
12 “Ngakhale zoyipa zili zozuna mʼkamwa mwake ndipo amazibisa kunsi kwa lilime lake,
他口內雖以惡為甘甜, 藏在舌頭底下,
13 ngakhale salola kuzilavula, ndipo amazisunga mʼkamwa mwake,
愛戀不捨,含在口中;
14 koma chakudya chake chidzawawasa mʼmimba mwake; chidzasanduka ngati ndulu ya njoka mʼkati mwa iyeyo.
他的食物在肚裏卻要化為酸, 在他裏面成為虺蛇的惡毒。
15 Adzachisanza chuma chimene anachimeza; Mulungu adzachitulutsa mʼmimba mwa munthuyo.
他吞了財寶,還要吐出; 上帝要從他腹中掏出來。
16 Iye adzayamwa ndulu ya njoka ndipo ululu wa mphiri udzamupha.
他必吸飲虺蛇的毒氣; 蝮蛇的舌頭也必殺他。
17 Sadzasangalala ndi timitsinje, mitsinje yoyenda uchi ndi mafuta.
流奶與蜜之河, 他不得再見。
18 Ayenera kubweza zimene anazigwirira ntchito osazidya; sadzasangalala ndi phindu la malonda ake.
他勞碌得來的要賠還,不得享用; 不能照所得的財貨歡樂。
19 Pakuti iye anapondereza anthu osauka ndipo anawasiya wopanda thandizo; iyeyo analanda nyumba zimene sanamange.
他欺壓窮人,且又離棄; 強取非自己所蓋的房屋。
20 “Chifukwa choti umbombo wake sutha, sadzatha kusunga chilichonse chimene amakondwera nacho.
他因貪而無厭, 所喜悅的連一樣也不能保守。
21 Palibe chatsala kuti iye adye; chuma chake sichidzachedwa kutha.
其餘的沒有一樣他不吞滅, 所以他的福樂不能長久。
22 Ngakhale ndi munthu wachuma, mavuto adzamugwera; mavuto aakulu adzamugwera.
他在滿足有餘的時候,必到狹窄的地步; 凡受苦楚的人都必加手在他身上。
23 Akadya nʼkukhuta, Mulungu adzamugwetsera ukali wamoto ngati mvula yosalekeza.
他正要充滿肚腹的時候, 上帝必將猛烈的忿怒降在他身上; 正在他吃飯的時候, 要將這忿怒像雨降在他身上。
24 Ngakhale athawe mkondo wachitsulo, muvi wamkuwa wosongoka udzamulasa.
他要躲避鐵器; 銅弓的箭要將他射透。
25 Muviwo adzawutulutsira ku msana, songa yake yowala kuchoka mʼmphafa mwake. Adzagwidwa ndi mantha aakulu;
他把箭一抽,就從他身上出來; 發光的箭頭從他膽中出來, 有驚惶臨在他身上。
26 mdima wandiweyani ukudikira chuma chake. Moto wopanda wowukoleza udzamupsereza ndi kuwononga zonse zotsala mʼnyumba yake.
他的財寶歸於黑暗; 人所不吹的火要把他燒滅, 要把他帳棚中所剩下的燒毀。
27 Zamumlengalenga zidzawulula kulakwa kwake; dziko lapansi lidzamuwukira.
天要顯明他的罪孽; 地要興起攻擊他。
28 Chigumula cha madzi chidzawononga nyumba yake, katundu wake adzatengedwa pa tsiku la ukali wa Mulungu.
他的家產必然過去; 上帝發怒的日子,他的貨物都要消滅。
29 Izi ndi zimene Mulungu amasungira anthu oyipa, mphotho imene Mulungu amayikira iwowo.”
這是惡人從上帝所得的分, 是上帝為他所定的產業。

< Yobu 20 >