< Yobu 19 >

1 Pamenepo Yobu anayankha kuti,
And Job answered and said,
2 “Kodi mudzakhala mukundizunza mpaka liti, ndi kundilasa ndi mawu anuwo?
How long will ye vex my soul, and crush me with words?
3 Inuyo mwandinyoza kwambiri; mwanditsutsa mopanda manyazi.
These ten times have ye reproached me; ye are not ashamed to stupefy me.
4 Ngati ndi zoona kuti ine ndasochera, cholakwachotu nʼchanga.
And be it [that] I have erred, mine error remaineth with myself.
5 Ngati ndithudi mukudziyika nokha pamwamba panga, ndi kugwiritsa ntchito kunyozedwa kwanga polimbana nane,
If indeed ye will magnify yourselves against me, and prove against me my reproach,
6 pamenepa dziwani kuti Mulungu wandilakwira ndipo wandizinga ukonde wake.
Know now that God hath overthrown me, and hath surrounded me with his net.
7 “Ngakhale ndifuwule kuti, ‘Akundizunza!’ Palibe wondiyankha; ngakhale ndipemphe thandizo, palibe wondichitira zolungama.
Behold, I cry out of wrong, and I am not heard; I cry aloud, but there is no judgment.
8 Mulungu wanditsekera njira yanga kotero sindingathe kudutsa; waphimba njira zanga ndi mdima.
He hath hedged up my way that I cannot pass, and he hath set darkness in my paths.
9 Iye wandilanda ulemu wanga ndipo wandivula chipewa chaufumu pamutu panga.
He hath stripped me of my glory, and taken the crown from my head.
10 Wandiphwanyaphwanya mbali zonse ndipo ndatheratu; Iye wazula chiyembekezo changa ngati mtengo.
He breaketh me down on every side, and I am gone; and my hope hath he torn up as a tree.
11 Wandikwiyira ndipo akundiyesa mmodzi mwa adani ake.
And he hath kindled his anger against me, and hath counted me unto him as one of his enemies.
12 Ankhondo ake akubwera kwa ine mwamphamvu, akonzekera zodzalimbana nane ndipo azungulira nyumba yanga.
His troops have come together and cast up their way against me, and have encamped round about my tent.
13 “Mulungu wandisiyanitsa ndi abale anga; wasandutsa odziwana nane kukhala achilendo kwa ine.
He hath put my brethren far from me, and mine acquaintance are quite estranged from me.
14 Abale anga andithawa; abwenzi anga andiyiwala.
My kinsfolk have failed, and my known friends have forgotten me.
15 Anthu odzacheza ku nyumba kwanga ndiponso antchito anga aakazi andisandutsa mlendo; ndasanduka mlendo mʼmaso mwawo.
The sojourners in my house and my maids count me as a stranger; I am an alien in their sight.
16 Ndikayitana wa ntchito wanga, iye sandiyankha, ngakhale ndikapempha ndi pakamwa panga sandichitira kanthu.
I called my servant, and he answered not; I entreated him with my mouth.
17 Mpweya wanga umamunyansa mkazi wanga; ndine chinthu chonyansa kwa abale anga a mimba imodzi.
My breath is strange to my wife, and my entreaties to the children of my [mother's] womb.
18 Inde, ngakhale ana amandinyoza; akandiona amandinyodola.
Even young children despise me; I rise up, and they speak against me.
19 Anzanga onse apamtima amanyansidwa nane; iwo amene ndinkawakonda andiwukira.
All my intimate friends abhor me, and they whom I loved are turned against me.
20 Ndangotsala khungu ndi mafupa okhaokha; ndapulumuka lokumbakumba.
My bones cleave to my skin and to my flesh, and I am escaped with the skin of my teeth.
21 “Mvereni chisoni, inu abwenzi anga, mvereni chisoni, pakuti dzanja la Mulungu landikantha.
Have pity upon me, have pity upon me, ye my friends; for the hand of God hath touched me.
22 Chifukwa chiyani mukundilondola ngati Mulungu? Kodi simunatope nalo thupi langa?
Why do ye persecute me as God, and are not satisfied with my flesh?
23 “Aa, achikhala mawu anga analembedwa, achikhala analembedwa mʼbuku,
Oh would that my words were written! oh that they were inscribed in a book!
24 akanalembedwa pa mwala ndi chitsulo, akanalembedwa pa thanthwe kuti sangathe kufufutidwa!
That with an iron style and lead they were graven in the rock for ever!
25 Koma ndikudziwa kuti mpulumutsi wanga ali ndi moyo, ndipo pa nthawi yomaliza adzabwera kudzanditeteza.
And [as for] me, I know that my Redeemer liveth, and the Last, he shall stand upon the earth;
26 Ndipo khungu langa litatha nʼkuwonongeka, mʼthupi langa lomweli ndidzamuona Mulungu.
And [if] after my skin this shall be destroyed, yet from out of my flesh shall I see God;
27 Ine ndemwe ndidzamuona Iye ndi maso angawa, ineyo, osati wina ayi. Ndithu mtima wanga ukufunitsitsadi!
Whom I shall see for myself, and mine eyes shall behold, and not another: — my reins are consumed within me.
28 “Koma inu mukuti, ‘Haa! Tingamuzunze bwanji, popeza kuti zonsezi zaoneka chifukwa cha iye yemweyo?’
If ye say, How shall we persecute him? when the root of the matter is found in me,
29 Inu muyenera kuopa lupanga; pakuti mkwiyo wake umalangadi ndi lupanga; zikadzatero muzadziwa kuti chiweruzo chilipo ndithu.”
Be ye yourselves afraid of the sword! for the sword is fury against misdeeds, that ye may know there is a judgment.

< Yobu 19 >