< Yobu 17 >

1 “Mtima wanga wasweka, masiku anga atha, manda akundidikira.
Mon souffle se perd, mes jours s'éteignent: pour moi, le tombeau!
2 Ndithudi, anthu ondiseka andizungulira; maso anga akupenyetsetsa mdani wanga.
Si nulle iniquité n'est par devers moi, mon œil peut avec calme regarder leur querelle.
3 “Inu Mulungu, patseni chikole chimene mukufuna. Ndani wina amene adzandiperekera ine chikole?
Ah! dépose ton gage! sois ma caution auprès de Toi! Qui est-ce qui mettrait sa main dans la mienne?
4 Inu mwatseka maganizo awo kuti asamvetse zinthu; choncho simudzawalola kuti apambane.
Car tu as fermé leur cœur à l'intelligence; aussi ne leur laisse pas l'avantage!
5 Ngati munthu apereka mnzake chifukwa cha chuma, ana ake sadzaona mwayi.
Tel convie son prochain à partager, dont les fils ont le regard éteint.
6 “Mulungu wandisandutsa chisudzo chochiseka aliyense, munthu amene anthu amalavulira malovu nkhope yake.
Il m'a fait passer en proverbe dans le peuple, et l'on me crache au visage;
7 Mʼmaso mwanga mwada ndi chisoni; ndawonda ndi mutu womwe.
et le chagrin a rendu mes yeux ternes, et ma figure est toute entière comme une ombre.
8 Anthu olungama akudabwa nazo zimenezi; anthu osachimwa akupsera mtima anthu osapembedza Mulungu.
C'est de quoi les gens de bien sont stupéfaits, et, ce qui irrite l'innocent contre l'impie;
9 Komabe anthu olungama adzasunga njira zawo, ndipo anthu a makhalidwe abwino mphamvu zawo zidzanka zikuchuluka.
mais le juste tient ferme à sa voie, et celui qui a les mains pures, redouble de vigueur.
10 “Tsono bwerani nonsenu, bwerezaninso mawu anuwo, sindidzapezapo munthu wanzeru pakati panupo.
Mais enfin, vous tous, revenez-y, venez encore à la charge, je n'en trouverai pas plus un sage entre vous.
11 Masiku anga atha, zimene ndinakonza zalephereka, pamodzinso ndi zokhumba za mtima wanga.
Mes jours sont passés, mes plans sont déchirés, cette fortune de mon cœur.
12 Anthu awa amasandutsa usiku kukhala usana, nthawi ya usiku iwo amati ‘kwatsala pangʼono kucha.’
Quand il est nuit, je suis, selon eux, en plein jour, et la lumière est plus près que les ténèbres présentes!
13 Ngati nyumba imene ndikuyiyembekezera ndi manda, ngati ndiyala bedi langa mu mdima, (Sheol h7585)
Quand je dois compter sur les Enfers, comme sur ma demeure, étendre ma couche dans le séjour ténébreux, (Sheol h7585)
14 ngati ndinena kwa dzenje la manda ‘ndinu abambo anga,’ ndiponso kwa mphutsi kuti, ‘ndinu amayi anga’ kapena ‘mlongo wanga,’
dire au tombeau: Tu es mon père! et aux vers: Vous êtes ma mère et ma sœur!
15 tsono chiyembekezo changa chili kuti? Ndani angaone populumukira panga?
où donc est mon espoir? Et l'espoir que j'aurais, qui le verrait [accompli]?
16 Ndithu sindidzakhalanso ndi chiyembekezo chilichonse, polowa mʼmanda, pamene ndidzatsikira ku fumbi.” (Sheol h7585)
Il descend vers les portes des Enfers, puisqu'ensemble nous allons reposer dans la poudre. (Sheol h7585)

< Yobu 17 >