< Yeremiya 50 >

1 Uthenga umene Yehova anayankhula ndi mneneri Yeremiya wonena za mzinda wa Babuloni ndi anthu ake ndi uwu:
Słowo, które PAN wypowiedział przeciwko Babilonowi i przeciwko ziemi Chaldejczyków przez proroka Jeremiasza:
2 “Lengeza ndi kulalika pakati pa anthu a mitundu ina, kweza mbendera ndipo ulengeze; usabise kanthu, koma uwawuze kuti, ‘Babuloni wagwa; mulungu wawo Beli wachititsidwa manyazi, nayenso Mariduku wagwidwa ndi mantha. Milungu yake yagwidwa ndi mantha ndipo mafano ake adzagwidwa ndi mantha.’
Opowiadajcie wśród narodów, rozgłaszajcie, podnieście sztandar, głoście i nie zatajajcie. Mówcie: Babilon wzięty, Bel pohańbiony, Merodach rozbity; jego posągi pohańbione, jego bożki pokruszone.
3 Mtundu wa anthu wochokera kumpoto wadzathira nkhondo Babuloni ndi kusandutsa bwinja dziko lake. Kumeneko sikudzakhalanso munthu kapena nyama.
Nadciągnie bowiem przeciwko niemu naród z północy, który zamieni jego ziemię w pustkowie, tak że nikt w niej nie zamieszka. Uciekną [i] odejdą zarówno ludzie, jak i zwierzęta.
4 “Masiku amenewo, nthawi imeneyo,” akutero Yehova, “anthu a ku Israeli ndi anthu a ku Yuda onse pamodzi adzabwera akulira. Adzafunitsitsa kuchita zimene Yehova Mulungu wawo akufuna.
W tych dniach i w tym czasie, mówi PAN, przyjdą synowie Izraela, a wraz z nimi synowie Judy; będą szli w płaczu i będą szukać PANA, swego Boga.
5 Adzafunsa njira ya ku Ziyoni ndi kuyamba ulendo wopita kumeneko. Iwo adzadzipereka kwa Yehova pochita naye pangano lamuyaya limene silidzayiwalika.
Będą pytać o drogę na Syjon i [zwróciwszy] tam swoje twarze, [powiedzą]: Chodźcie i przyłączmy się do PANA wiecznym przymierzem, które nie ulegnie zapomnieniu.
6 “Anthu anga ali ngati nkhosa zotayika; abusa awo anawasocheretsa mʼmapiri. Iwo anayendayenda mʼmapiri ndi mʼzitunda mpaka kuyiwala kwawo.
Mój lud był trzodą owiec zbłąkanych, ich pasterze wiedli ich na manowce, po górach ich rozegnali. Schodził z góry na pagórek, zapomniał o swoim legowisku.
7 Aliyense amene anawapeza anawawononga; adani awo anati, ‘Ife si olakwa, chifukwa iwo anachimwira Yehova, amene ali mpumulo wawo weniweni ndi amene makolo awo anamukhulupirira.’
Wszyscy, którzy ich spotykali, pożerali ich, a ich wrogowie mówią: Nie jesteśmy nic winni, bo to oni zgrzeszyli [przeciwko] PANU, przybytkowi sprawiedliwości, [przeciwko] PANU, nadziei ich ojców.
8 “Thawaniko ku Babuloni; chokani mʼdziko la Ababuloni. Muyambe inu kutuluka ngati atonde amene amatsogolera ziweto.
Uchodźcie ze środka Babilonu, wychodźcie z ziemi Chaldejczyków i bądźcie jak kozły przed trzodą.
9 Taonani, ndidzaukitsa gulu lankhondo lamphamvu la mitundu ina ndi kubwera nalo kuchokera kumpoto kudzamenyana ndi Babuloni. Iwo adzandandalika ankhondo awo ndi kugonjetsa Babuloni. Mivi yawo ili ngati ya ankhondo aluso, yosapita padera.
Oto bowiem wzbudzę i sprowadzę na Babilon gromadę wielkich narodów z ziemi północnej. I uszykują się przeciwko niemu, i stamtąd będzie zdobyty. Ich strzały będą jak u wprawnego mocarza, żadna nie wróci bez skutku.
10 Motero Ababuloni adzafunkhidwa; ndipo onse omufunkha adzakhuta,” akutero Yehova.
Chaldea będzie łupem, [a] wszyscy, którzy ją złupią, zostaną nasyceni, mówi PAN.
11 “Inu Ababuloni, munawononga anthu anga osankhika. Ndiye pano mukukondwa, mukusangalala. Mukulumphalumpha mokondwa ngati mwana wangʼombe wopuntha tirigu ndiponso mukulira monyada ngati ngʼombe zazimuna.
Ponieważ się cieszyliście, ponieważ się radowaliście, grabieżcy mego dziedzictwa; ponieważ utyliście jak jałówka na trawie i ryczycie jak wół;
12 Koma mzinda wanu udzachititsidwa manyazi kwambiri. Mzinda umene uli ngati mayi wanu udzanyazitsidwa. Babuloni adzasanduka chitsirizira cha anthu onse. Mzinda wawo udzakhala ngati thengo, ngati dziko lowuma lachipululu.
Wasza matka będzie bardzo zawstydzona, spłonie ze wstydu wasza rodzicielka. Oto [stanie się] ostatnią z narodów, pustkowiem, ziemią suchą i pustynną.
13 Chifukwa cha mkwiyo wa Yehova Babuloni adzakhala wopanda anthu ndipo adzakhala chipululu chokhachokha. Onse odutsa kumeneko adzachita mantha ndipo azidzangotsonya chifukwa cha chiwonongeko chake chachikulu.
Z powodu gniewu PANA nie będzie zamieszkana, ale cała zostanie spustoszona. Ktokolwiek będzie przechodził obok Babilonu, zdumieje się i będzie świstał nad wszystkimi jego plagami.
14 “Inu okoka uta, konzekani kuti muthire nkhondo mzinda wa Babuloni mbali zonse. Muponyereni mivi yanu yonse chifukwa anachimwira Yehova.
Ustawcie się przeciw Babilonowi w koło. Wszyscy, którzy napinacie łuk, strzelajcie do niego, nie żałujcie strzał, bo zgrzeszył przeciwko PANU.
15 Mufuwulireni mbali zonse pakuti wagonja. Nsanja zake zagwa. Malinga ake agwetsedwa. Kumeneku ndiko kulipsira kwa Yehova. Mulipsireni, mumuchite zomwe iye anachitira anthu ena.
Wołajcie przeciwko niemu zewsząd. Poddał się, upadły jego fundamenty, jego mury są zburzone. Jest to bowiem zemsta PANA. Pomścijcie się nad nim; jak on czynił [innym, tak] jemu też uczyńcie.
16 Chotsani ku Babuloni munthu wofesa mbewu aliyense, ndiponso wodula tirigu ndi chikwakwa chake pa nthawi yokolola. Poona lupanga la ozunza anzawo, aliyense adzabwerera kwa anthu ake; adzathawira ku dziko la kwawo.
Wyniszczcie z Babilonu siewcę i tego, który chwyta sierp w czasie żniwa. Przed mieczem niszczycielskim każdy się zwróci do swego ludu i każdy ucieknie do swojej ziemi.
17 “Aisraeli ali ngati nkhosa zomwe zabalalika pothamangitsidwa ndi mikango. Mfumu ya ku Asiriya ndiye inayamba kuwapha Aisraeliwo. Wotsiriza anali Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni amene anachita ngati kuphwanya mafupa ake.”
Izrael jest owcą przegnaną, [którą] spłoszyły lwy. Najpierw król Asyrii pożarł go, a na koniec ten Nabuchodonozor, król Babilonu, pokruszył jego kości.
18 Nʼchifukwa chake Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti, “Ndidzalanga mfumu ya ku Babuloni pamodzi ndi dziko lake monga momwe ndinalangira mfumu ya ku Asiriya.
Dlatego tak mówi PAN zastępów, Bóg Izraela: Oto ukarzę króla Babilonu i jego ziemię, jak ukarałem króla Asyrii.
19 Koma ndidzabwezera Israeli ku msipu wake ndipo adzadya mʼminda ya ku Karimeli ndi Basani; adzadya nakhuta ku mapiri a ku Efereimu ndi Giliyadi.
I znowu przyprowadzę Izraela do swego mieszkania, i będzie się paść na Karmelu i w Baszanie, i jego dusza nasyci się na górze Efraim i w Gileadzie.
20 Masiku amenewo, nthawi imeneyo,” akutero Yehova, “anthu adzafunafuna zolakwa za Israeli koma sadzapeza nʼchimodzi chomwe, ndipo adzafufuza machimo a Yuda, koma sadzapeza ndi limodzi lomwe, chifukwa otsala amene ndawasiya ndidzawakhululukira.
W tych dniach i w tym czasie, mówi PAN, będą szukać nieprawości Izraela, ale jej nie będzie, i grzechów Judy, ale nie będą znalezione. Przebaczę bowiem tym, których pozostawię.
21 “Lithireni nkhondo dziko la Merataimu ndi anthu okhala ku Pekodi. Muwaphe ndi lupanga ndi kuwawonongeratu,” akutero Yehova. “Chitani zonse monga momwe ndakulamulani.
Wyrusz przeciwko ziemi Meratajim, przeciwko niej i mieszkańcom Pekod. Spustosz i zniszcz doszczętnie, goniąc ich, mówi PAN, i uczyń wszystko, jak ci rozkazałem.
22 Mʼdziko muli phokoso la nkhondo, phokoso la chiwonongeko chachikulu!
Wrzawa wojenna w tej ziemi i wielkie spustoszenie.
23 Taonani mʼmene waphwanyikira ndi kuwonongekera uja amati ndi nyundo ya dziko lonse lapansi. Mzinda wa Babuloni wasanduka chinthu chochititsa mantha pakati pa mitundu ina!
Jakże jest rozbity i złamany młot całej ziemi? Jakże Babilon stał się spustoszeniem wśród narodów?
24 Ndinakutchera msampha, iwe Babuloni, ndipo wakodwamo iwe wosazindikira kanthu; unapezeka ndiponso unakodwa chifukwa unalimbana ndi Yehova.
Zastawiłem na ciebie sidła i zostałeś schwytany, Babilonie, a nie zauważyłeś tego. Znaleziono cię i pochwycono, ponieważ spierałeś się z PANEM.
25 Yehova watsekula nyumba ya zida zake ndipo watulutsa zida za ukali wake, pakuti Ambuye Yehova Wamphamvuzonse ali ndi ntchito yoti agwire mʼdziko la Ababuloni.
PAN otworzył swoją zbrojownię i wyniósł oręż swego gniewu. To bowiem jest dzieło Pana BOGA zastępów w ziemi Chaldejczyków.
26 Mumenyane naye Babuloni mbali zonse. Anthu ake muwawunjike ngati milu ya tirigu. Muwawononge kotheratu ndipo pasakhale wopulumuka ndi mmodzi yemwe.
Ruszajcie przeciwko niemu z krańców [ziemi], otwórzcie jego spichlerze. Zbierzcie go w sterty i zniszczcie go doszczętnie, by nic z niego nie pozostało.
27 Iphani ankhondo ake onse. Onse aphedwe ndithu. Tsoka lawagwera pakuti tsiku lawo lachilango lafika.
Pozabijajcie wszystkie jego cielce, niech idą na rzeź. Biada im, bo nadszedł ich dzień, czas ich nawiedzenia.
28 Tikumva anthu othawa nkhondo ochokera ku Babuloni akulengeza mu Yerusalemu za kulipsira kwa Yehova Mulungu wathu. Iye akulipsira chifukwa chowononga Nyumba yake.
[Słychać] głos uciekających i tych, co uchodzą z ziemi Babilonu, aby ogłosić na Syjonie pomstę PANA, naszego Boga, pomstę za jego świątynię.
29 “Itanani anthu oponya mivi kudzathira nkhondo Babuloni. Muyitanenso onse amene amakoka mauta. Mangani misasa ya nkhondo momuzungulira; musalole munthu aliyense kuthawa. Muchiteni monga momwe iye anachitira anthu ena. Iyeyu ananyoza Yehova, Woyera wa Israeli.
Zgromadźcie przeciwko Babilonowi wszystkich strzelców, którzy napinają łuk; rozbijcie obóz przeciw niemu dokoła, aby [nikt] nie uszedł. Odpłaćcie mu według jego uczynków, według wszystkiego, co [innym] czynił, uczyńcie mu. Wynosił się bowiem przeciwko PANU, przeciwko Świętemu Izraela.
30 Nʼchifukwa chake, anyamata ake adzaphedwa mʼmabwalo ake; ankhondo ake onse adzaphedwa tsiku limenelo,” akutero Yehova.
Dlatego jego młodzieńcy polegną na ulicach i wszyscy jego wojownicy zostaną zgładzeni w tym dniu, mówi PAN.
31 “Taona, ndikukuthira nkhondo, iwe wodzikuzawe,” akutero Ambuye Yehova Wamphamvuzonse, “chifukwa tsiku lako lafika, nthawi yoti ndikulange yakwana.
Oto jestem przeciwko tobie, zuchwalcze, mówi Pan, BÓG zastępów. Nadszedł bowiem twój dzień [i] czas, gdy cię nawiedzę.
32 Wodzikuzawe udzapunthwa nʼkugwa ndipo palibe amene adzakudzutse; ndidzayatsa moto mʼmizinda yake umene udzanyeketsa onse amene amuzungulira.”
Potknie się zuchwalec i upadnie, i nikt go nie podniesie. Wzniecę ogień w jego miastach, który pochłonie wszystko wokół niego.
33 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Anthu a ku Israeli akuzunzidwa, pamodzi ndi anthu a ku Yuda, ndipo onse amene anawagwira ukapolo awagwiritsitsa, akukana kuwamasula.
Tak mówi PAN zastępów: Synowie Izraela i synowie Judy razem cierpią ucisk. Wszyscy, którzy ich pojmali, trzymają ich i nie chcą ich wypuścić.
34 Koma Mpulumutsi wawo ndi wamphamvu; dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse. Iye adzawateteza molimba pa mlandu wawo nʼcholinga choti abweretse mtendere mʼdziko lawo, koma adzavutitsa okhala ku Babuloni.”
[Ale] ich Odkupiciel jest potężny, jego imię to PAN zastępów, skutecznie będzie bronił ich sprawy, aby zapewnić pokój tej ziemi i trwożyć mieszkańców Babilonu.
35 Yehova akuti, “Imfa yalunjika pa Ababuloni, pa akuluakulu ake ndi pa anthu ake a nzeru!
Miecz [spadnie] na Chaldejczyków, mówi PAN, i na mieszkańców Babilonu, na jego książąt i mędrców;
36 Imfa yalunjika pa aneneri abodza kuti asanduke zitsiru. Imfa yalunjika pa ankhondo ake kuti agwidwe ndi mantha aakulu.
Miecz na kłamców, aby zgłupieli, miecz na jego wojowników, aby byli przerażeni;
37 Imfa ilunjike pa akavalo ake ndi magaleta ake. Ilunjikanso pa magulu ankhondo achilendo amene ali pakati pawo kuti asanduke ngati akazi. Chiwonongeko chilunjikenso pa chuma chake kuti chidzafunkhidwe.
Miecz na jego konie i rydwany oraz na całą różnorodną ludność, która jest pośród niego, aby była jak kobiety; miecz na jego skarby, aby były zagrabione;
38 Chilala chilunjike pa madzi ake kuti aphwe. Babuloni ndi dziko la mafano, ndipo anthu afika poyaluka nawo mafanowo.
Susza na jego wody, aby wyschły. Ziemia bowiem jest [pełna] rzeźbionych obrazów, a szaleją przy [swoich] bożkach.
39 “Nʼchifukwa chake nyama zakuthengo ndi afisi zidzakhala kumeneko ndipo kudzakhalanso akadzidzi. Kumeneko sikudzapezekako anthu, ndithu anthu sadzakhalako pa mibado yonse.
Dlatego zamieszkają tam dzikie zwierzęta pustyni i straszne bestie wysp, zamieszkają w nim też młode sowy. Nie będzie już zaludniony na wieki i nie będą [w nim] mieszkać po wszystkie pokolenia.
40 Monga momwe Mulungu anawonongera Sodomu ndi Gomora pamodzi ndi mizinda yonse yozungulira,” akutero Yehova, “momwemonso palibe amene adzakhale kumeneko; anthu sadzayendanso mʼmenemo.
Jak Bóg zniszczył Sodomę i Gomorę oraz sąsiednie miasta, mówi PAN, [tak] też nikt tam nie zamieszka ani syn człowieczy nie będzie w nim gościł.
41 “Taonani! Gulu lankhondo likubwera kuchokera kumpoto; mtundu wa anthu amphamvu pamodzi ndi mafumu ambiri, wanyamuka kuchokera kumathero a dziko lapansi.
Oto lud nadciągnie z północy, naród wielki, i liczni królowie zostaną wzbudzeni z krańców ziemi.
42 Atenga mauta ndi mikondo; ndi anthu ankhanza ndipo alibe chifundo. Phokoso lawo likumveka ngati mkokomo wa nyanja. Akwera pa akavalo awo, ndipo akonzekera kudzakuthira nkhondo iwe Babuloni.
Pochwycą łuk i włócznię, są okrutni i bezlitośni; ich głos huczy jak morze i jeżdżą na koniach, każdy uszykowany do walki przeciwko tobie, córko Babilonu!
43 Mfumu ya ku Babuloni yamva za mbiri yawo, ndipo yalobodokeratu. Ikuda nkhawa, ikumva ululu ngati wa mayi pa nthawi yake yochira.
Król Babilonu usłyszał o nich wieść i osłabły mu ręce. Ogarnęła go udręka [i] bóle jak rodzącą kobietę.
44 Taonani, monga mkango wochokera ku nkhalango ya ku Yorodani kupita ku msipu wobiriwira, momwemonso ine ndidzapirikitsa Babuloni mʼdziko lake mwadzidzidzi. Pambuyo pake ndidzawayikira wowalamulira amene ndamufuna Ine. Wofanana nane ndani ndipo ndani amene angalimbane nane? Ndi mtsogoleri wa dziko uti amene anganditengere ku bwalo la milandu?”
Oto jak lew wystąpi z wezbrania Jordanu przeciwko przybytkowi mocarza. Wypędzę go jednak nagle z tej ziemi, a ustanowię nad nią mojego wybrańca. Któż bowiem jest mi równy? Kto wyznaczy mi termin rozprawy? A kto jest tym pasterzem, który się ostoi przede mną?
45 Nʼchifukwa chake imvani. Izi ndi zimene Ine Yehova ndakonza zolangira anthu a ku Babuloni. Ngakhale ana omwe adzatengedwa ukapolo ndipo aliyense adzachita mantha chifukwa cha iwo.
Dlatego słuchajcie postanowienia PANA, które powziął przeciwko Babilonowi i jego zamysłów, które przygotował przeciwko ziemi Chaldejczyków. Zaprawdę, wywloką ich najmniejsi z tej trzody, spustoszą ich i [ich] mieszkania.
46 Akadzagwa Babuloni padzakhala mfuwu waukulu ndipo dziko lapansi lidzanjenjemera, ndipo kulira kwawo kudzamveka pakati pa mitundu yonse ya anthu.
Od huku przy zdobyciu Babilonu ziemia się porusza, słychać krzyk wśród narodów.

< Yeremiya 50 >