< Yeremiya 5 >

1 “Pitani uku ndi uku mʼmisewu ya Yerusalemu, mudzionere nokha, funafunani mʼmabwalo ake. Ngati mungapeze munthu mmodzi amene amachita zachilungamo ndi kufunafuna choonadi, ndipo ndidzakhululukira mzinda uno.
Courez çà et là par les rues de Jérusalem, et regardez et sachez et cherchez dans ses places si vous trouvez un homme, s’il y a quelqu’un qui fasse ce qui est droit, qui cherche la fidélité, et je pardonnerai à la ville.
2 Ngakhale anthu akulumbira kuti, ‘Pali Yehova wamoyo,’ komabe akungolumbira mwachinyengo.”
Et s’ils disent: L’Éternel est vivant! en cela même, ils jurent faussement.
3 Inu Yehova, kodi suja mumafuna anthu onena zoona? Inu munawakantha anthuwo, koma sanamve kupweteka; munawaphwanya anthuwo, koma sanatengepo phunziro. Anawumitsa mitima yawo ngati mwala ndipo anakaniratu kulapa.
Éternel! tes yeux ne [regardent-ils] pas à la fidélité? Tu les as frappés, mais ils n’en ont point ressenti de douleur; tu les as consumés, ils ont refusé de recevoir la correction; ils ont rendu leurs faces plus dures qu’un roc, ils ont refusé de revenir.
4 Ndiye ndinati, “Awa ndi amphawi chabe; anthu ochita zopusa. Sadziwa njira ya Yehova, sazindikira zimene Mulungu wawo amafuna.
Et j’ai dit: Voilà, ce sont de pauvres gens, ce sont des fous; car ils ne connaissent pas la voie de l’Éternel, le jugement de leur Dieu.
5 Tsono ndidzapita kwa atsogoleri ndi kukayankhula nawo; ndithu iwo amadziwa njira ya Yehova, amadziwa zomwe Mulungu wawo amafuna.” Koma ayi, iwonso anathyola goli la Yehova ndipo anadula msinga zawo.
Je m’en irai vers les grands, et je leur parlerai; car eux, ils connaissent la voie de l’Éternel, le jugement de leur Dieu; mais ceux-ci, tous ensemble, ont brisé le joug, rompu les liens.
6 Choncho mkango wochokera ku nkhalango udzawapha, mmbulu wochokera ku thengo udzawawononga, kambuku adzawabisalira pafupi ndi mizinda yawo kuti akhadzule aliyense amene adzayesera kutuluka mʼmizindamo pakuti kuwukira kwawo ndi kwakukulu ndipo abwerera mʼmbuyo kwambiri.
C’est pourquoi un lion de la forêt les frappera, un loup du soir les ravagera; le léopard veille devant leurs villes, quiconque en sort est déchiré; car leurs transgressions sont multipliées, leurs infidélités se sont renforcées.
7 Yehova akuti, “Kodi ndingakukhululukireni bwanji ndi zimene mwachita? Ana anu andisiya Ine ndipo amapembedza milungu imene si milungu konse. Ine ndinawapatsa zonse zimene ankasowa, komabe iwo anachita chigololo namasonkhana ku nyumba za akazi achiwerewere.
Pourquoi te pardonnerai-je? Tes fils m’ont abandonné, et ils jurent par ce qui n’est pas Dieu; je les ai rassasiés, et ils ont commis adultère, et sont allés en troupe dans la maison de la prostituée.
8 Monga amachitira akavalo onenepa akamamemesa, aliyense wa iwo ankathamangira mkazi wa mnzake.
Chevaux bien nourris, ils courent çà et là, chacun hennit après la femme de son prochain.
9 Tsono ndingaleke kuwalanga chifukwa cha zimenezi?” akutero Yehova. “Kodi nʼkuleka kuwulipsira mtundu woterewu?
Ne punirais-je pas de telles choses? dit l’Éternel; et mon âme ne se vengerait-elle pas d’une nation comme celle-là?
10 “Pitani ku minda yake ya mipesa ndi kukayiwononga, koma musakayiwononge kotheratu. Sadzani nthambi zake pakuti anthu amenewa si a Yehova.
Montez sur ses murailles, et détruisez! mais ne détruisez pas entièrement; ôtez ses créneaux, car ils ne sont pas à l’Éternel;
11 Nyumba ya Israeli ndi nyumba ya Yuda onse akhala osakhulupirika kotheratu kwa Ine.”
car la maison d’Israël et la maison de Juda ont agi très perfidement envers moi, dit l’Éternel.
12 Iwowa ankanama ponena za Yehova kuti, “Yehova sangachite zimenezi! Choyipa sichidzatigwera; sitidzaona nkhondo kapena njala.
Ils ont renié l’Éternel, et ont dit: Il n’est pas! et le mal ne viendra pas sur nous; nous ne verrons ni l’épée ni la famine,
13 Mawu a aneneri azidzangopita ngati mphepo; ndipo mwa iwo mulibe uthenga wa Yehova. Choncho zimene amanena zidzawachitikira okha.”
et les prophètes seront du vent, et la parole n’est pas en eux: ainsi leur sera-t-il fait.
14 Chifukwa chake Yehova Mulungu Wamphamvuzonse akuti, “Popeza kuti anthu awa ayankhula mawu amenewa, tsono mawu anga ndidzawasandutsa moto mʼkamwa mwako ndipo anthu awa ndidzawasandutsa nkhuni zimene moto udzapserezeretu.
C’est pourquoi, ainsi dit l’Éternel, le Dieu des armées: Parce que vous avez prononcé cette parole, voici, je ferai que mes paroles dans ta bouche seront du feu, et ce peuple sera le bois, et le [feu] les consumera.
15 Inu Aisraeli,” Yehova akuti, “Ndikukubweretserani mtundu wa anthu ochokera kutali, ndi mtundu umene sunagonjetsedwepo, mtundu wakalekale umene chiyankhulo chawo inu simuchidziwa, zimene akunena inu simungazimvetse.
Voici, je fais venir de loin une nation contre vous, maison d’Israël, dit l’Éternel, une nation puissante, une nation ancienne, une nation dont tu ne sais pas la langue, et dont tu ne comprends pas la parole.
16 Zida zawo za nkhondo zapha anthu ambirimbiri; onsewo ndi ankhondo amphamvu okhaokha.
Son carquois est comme un sépulcre ouvert, ils sont tous des hommes vaillants.
17 Adzakudyerani zokolola zanu ndi chakudya chanu, adzapha ana anu aamuna ndi aakazi; adzakupherani nkhosa zanu ndi ngʼombe zanu, adzawononga mpesa wanu ndi mikuyu yanu. Ndi malupanga awo adzagwetsa mizinda yanu yotetezedwa imene mumayidalira.
Elle dévorera ta moisson et ton pain, elle dévorera tes fils et tes filles, elle dévorera ton menu et ton gros bétail, elle dévorera ta vigne et ton figuier, elle détruira par l’épée tes villes fortes sur lesquelles tu te confiais.
18 “Komabe pa masiku amenewo sindidzakuwonongani kotheratu,” akutero Yehova.
Mais, même en ces jours-là, dit l’Éternel, je ne vous détruirai pas entièrement.
19 Ndipo pamene anthu adzafunsa Yehova kuti, “Chifukwa chiyani Yehova Mulungu wathu wachita zimenezi?” Iwe udzawawuze kuti, “Monga momwe mwasiyira Ine ndi kutumikira milungu yachilendo mʼdziko mwanu, momwemonso mudzatumikira anthu a mʼdzikonso lachilendo.”
Et il arrivera que, quand vous direz: Pourquoi l’Éternel, notre Dieu, nous a-t-il fait toutes ces choses? tu leur diras: Comme vous m’avez abandonné et que vous avez servi des dieux étrangers dans votre pays, ainsi vous servirez les étrangers dans un pays qui n’est pas le vôtre.
20 “Lengeza izi kwa ana a Yakobo ndipo mulalikire kwa anthu a ku Yuda kuti,
Annoncez ceci dans la maison de Jacob, et faites-le entendre dans Juda, disant:
21 Imvani izi, inu anthu opusa ndi opanda nzeru, inu amene maso muli nawo koma simupenya, amene makutu muli nawo koma simumva.
Écoutez pourtant ceci, peuple insensé et sans intelligence, qui avez des yeux et ne voyez pas, qui avez des oreilles et n’entendez pas.
22 Kodi simuyenera kuchita nane mantha?” Akutero Yehova. “Kodi simuyenera kunjenjemera pamaso panga? Ine ndinayika mchenga kuti ukhale malire a nyanja, malire a muyaya amene nyanjayo singadutsepo. Mafunde angawombe motani, koma sangathe kupitirira malirewo; mafunde angakokome motani, koma sangadutse malirewo.
Ne me craindrez-vous pas, dit l’Éternel, ne tremblerez-vous pas devant moi, qui ai mis le sable pour limite à la mer, statut perpétuel, qu’elle n’outrepassera pas? Ses vagues se soulèvent, mais elles ne prévaudront pas; et elles bruient, mais elles ne l’outrepasseront pas.
23 Koma anthu awa ndi nkhutukumve ndiponso a mitima yowukira; andifulatira ndipo andisiyiratu.
Mais ce peuple-ci a un cœur indocile et rebelle; ils se sont détournés, et s’en sont allés;
24 Sananenepo mʼmitima mwawo kuti, ‘Tiyeni tizipembedza Yehova Mulungu wathu. Kodi suja amatipatsa pa nthawi yake mvula yachizimalupsa ndi yamasika. Iye salephera konse kutipatsa nyengo ya kholola.’
et ils n’ont pas dit dans leur cœur: Craignons pourtant l’Éternel, notre Dieu, qui donne les pluies en leur temps, la pluie de la première saison et la pluie de la dernière saison, [et] qui nous garde les semaines ordonnées de la moisson.
25 Koma zolakwa zanu zalepheretsa zonsezi; ndipo machimo anu akumanitsani zabwino.
Vos iniquités ont détourné ces choses, et vos péchés ont retenu de vous le bien.
26 “Pakati pa anthu anga pali anthu ena oyipa amene amabisalira anzawo monga amachitira mlenje mbalame ndiponso ngati amene amatchera misampha kuti akole anthu anzawo.
Car il se trouve des méchants parmi mon peuple; ils épient comme l’oiseleur qui se baisse, ils posent des pièges, ils prennent des hommes.
27 Nyumba zawo zadzaza ndi chuma chochipeza mwa chinyengo ngati zikwere zodzaza ndi mbalame. Nʼchifukwa chake asanduka otchuka ndi olemera.
Comme une cage est pleine d’oiseaux, ainsi leurs maisons sont pleines de fraude; c’est pourquoi ils sont devenus grands et se sont enrichis.
28 Ndipo ananenepa ndi kukhala ndi matupi osalala. Ntchito zawo zoyipa nʼzopanda malire; saweruza mwachilungamo nkhani ya ana amasiye kuti iyende bwino, sateteza ufulu wa anthu osauka.
Ils sont devenus gras et luisants, aussi ils débordent de méchancetés; ils ne jugent pas la cause, la cause de l’orphelin, et ils prospèrent; et ils ne font pas droit aux pauvres.
29 Kodi Ine ndingaleke kuwalanga chifukwa cha zimenezi? Kodi ndisawulipsire mtundu woterewu? Akutero Yehova.
Ne punirais-je pas de telles choses? dit l’Éternel; mon âme ne se vengerait-elle pas d’une nation comme celle-là?
30 “Chinthu chothetsa nzeru ndi choopsa kwambiri chachitika mʼdzikomo:
Une chose étonnante et horrible est arrivée dans le pays:
31 Aneneri akunenera zabodza, ndipo ansembe akuvomerezana nawo, ndipo anthu anga akukonda zimenezi. Koma mudzatani potsiriza?
les prophètes prophétisent avec mensonge, et les sacrificateurs dominent par leur moyen; et mon peuple l’aime ainsi. Et que ferez-vous à la fin?

< Yeremiya 5 >