< Yeremiya 47 >

1 Uthenga umene Yehova anamupatsa mneneri Yeremiya wonena za Afilisti, Farao asanathire nkhondo Gaza ndi uwu:
The word of Jehovah that came to Jeremiah the prophet concerning the Philistines, before Pharaoh smote Gaza.
2 Yehova akuti, “Taonani mmene madzi akubwerera kuchokera kumpoto; adzasanduka mtsinje wosefukira ndi a mkokomo. Adzasefukira mʼdziko monse ndi kumiza chilichonse mʼmenemo, mizinda ndi onse okhala mʼmenemo. Anthu adzafuwula; anthu onse okhala mʼdzikomo adzalira
Thus says Jehovah: Behold, waters rise up out of the north, and shall become an overflowing stream, and shall overflow the land and all that is therein, the city and those who dwell therein. And the men shall cry, and all the inhabitants of the land shall wail
3 akadzamva mgugu wa ngʼombe zazimuna zothamanga, phokoso la magaleta ake ndi kulira kwa mikombero yake. Makolo sadzatembenuka kuti athandize ana awo; manja awo adzangoti khoba.
at the noise of the stamping of the hoofs of his strong ones, at the rushing of his chariots, at the rumbling of his wheels. The fathers do not look back to their sons for feebleness of hands,
4 Pakuti tsiku lafika lowononga Afilisti onse ndi kupha onse otsala, onse amene akanatha kuthandiza Turo ndi Sidoni. Yehova ali pafupi kuwononga Afilisti, otsala ochokera ku zilumba za ku Kafitori.
because of the day that comes to destroy all the Philistines, to cut off from Tyre and Sidon every helper who remains. For Jehovah will destroy the Philistines, the remnant of the isle of Caphtor.
5 Anthu a ku Gaza ameta mipala; anthu a ku Asikeloni akhala chete. Inu otsala a ku chigwa, mudzakhala mukudzichekacheka mpaka liti?
Baldness has come upon Gaza. Ashkelon is brought to naught, the remnant of their valley. How long will thou cut thyself?
6 “Mukulira kuti, ‘Aa, lupanga la Yehova, kodi udzapumula liti? Bwerera mʼmalo ako; ukhale momwemo ndipo ukhale chete.’
O thou sword of Jehovah, how long will it be ere thou be quiet? Put up thyself into thy scabbard. Rest, and be still.
7 Koma lupangalo lidzapumula bwanji pamene Yehova walilamulira kuti lithire nkhondo Asikeloni ndi anthu a mʼmbali mwa nyanja?”
How can thou be quiet, since Jehovah has given thee a charge against Ashkelon, and against the sea-shore. He has appointed it there.

< Yeremiya 47 >