< Yeremiya 36 >

1 Chaka chachinayi cha Yehoyakimu mwana wa Yosiya mfumu ya Yuda, Yehova anayankhula ndi Yeremiya kuti,
And it came to pass in the fourth year of Jehoiakim the son of Josiah, king of Judah, that this word came to Jeremiah from Jehovah, saying,
2 “Tenga buku ndipo ulembemo mawu onse amene ndayankhula nawe otsutsa Israeli, Yuda ndi mitundu yonse ya anthu, kuyambira nthawi imene ndinayamba kuyankhula nawe pa nthawi ya ulamuliro wa Yosiya mpaka lero lino.
Take thee a roll of a book, and write in it all the words that I have spoken to thee against Israel, and against Judah, and against all the nations, from the day I spoke to thee, from the days of Josiah, even to this day.
3 Mwina mwake anthu a ku Yuda adzamva za zoopsa zonse zimene ndakonza kuti ndiwachitire, ndipo munthu aliyense adzatembenuka ndi kusiya ntchito zake zoyipa. Motero ndidzawakhululukira zoyipa zawo ndi machimo awo.”
It may be that the house of Judah will hear all the evil which I purpose to do to them, that they may return every man from his evil way, that I may forgive their iniquity and their sin.
4 Tsono Yeremiya anayitana Baruki mwana wa Neriya. Baruki analemba mʼbuku mawu onse amene Yeremiya ankamuwuza, mawu amene Yehova anamuwuza Yeremiya.
Then Jeremiah called Baruch the son of Neriah. And Baruch wrote from the mouth of Jeremiah all the words of Jehovah, which he had spoken to him, upon a roll of a book.
5 Kenaka Yeremiya anawuza Baruki kuti, “Ine andiletsa kupita ku Nyumba ya Mulungu.
And Jeremiah commanded Baruch, saying, I am shut up. I cannot go into the house of Jehovah.
6 Tsono iwe upite ku Nyumba ya Yehova pa tsiku losala kudya ndipo ukawerenge mawu a Yehova ochokera mʼbukumu amene ndinakulembetsa anthu onse akumva. Ukawawerengere anthu onse a ku Yuda amene amabwera ku Nyumba ya Mulungu kuchokera ku mizinda yawo.
Therefore go thou, and read in the roll, which thou have written from my mouth, the words of Jehovah in the ears of the people in Jehovah's house upon the fast-day. And also thou shall read them in the ears of all Judah who come out of their cities.
7 Mwina mwake adzapempha kwa Yehova ndipo aliyense adzatembenuka ndi kusiya makhalidwe ake oyipa pakuti mkwiyo ndi ukali wa Yehova pa anthu awa ndi woopsa kwambiri.”
It may be they will present their supplication before Jehovah, and will return each one from his evil way, for great is the anger and the wrath that Jehovah has pronounced against this people.
8 Baruki mwana wa Neriya anachita zonse zimene mneneri Yeremiya anamuwuza kuti achite. Mʼnyumba ya Yehova, iye anawerenga mawu a Yehova ochokera mʼbukulo.
And Baruch the son of Neriah did according to all that Jeremiah the prophet commanded him, reading in the book the words of Jehovah in Jehovah's house.
9 Pa mwezi wachisanu ndi chinayi wa chaka chachisanu cha Yehoyakimu mwana wa Yosiya mfumu ya Yuda, anthu onse a mu Yerusalemu ndi onse amene anabwera kumeneko kuchokera ku mizinda ya Yuda, anapangana za kusala kudya kuti apepese Yehova.
Now it came to pass in the fifth year of Jehoiakim the son of Josiah, king of Judah, in the ninth month, that all the people in Jerusalem, and all the people who came from the cities of Judah to Jerusalem, proclaimed a fast before Jehovah.
10 Atayima pa chipinda cha Gemariya mwana wa mlembi Safani, chimene chinali mʼbwalo lapamwamba, pafupi ndi Chipata Chatsopano cholowera ku Nyumba ya Yehova, Baruki anawerenga mawu onse a Yeremiya amene anali mʼbuku muja kwa anthu onse amene anali ku Nyumba ya Yehova.
Then Baruch read in the book the words of Jeremiah in the house of Jehovah, in the chamber of Gemariah the son of Shaphan, the scribe, in the upper court, at the entry of the new gate of Jehovah's house, in the ears of all the people.
11 Mikaya mwana wa Gemariya, mwana wa Safani, atamva mawu onse a Yehova ochokera mʼbukumo,
And when Micaiah the son of Gemariah, the son of Shaphan, had heard out of the book all the words of Jehovah,
12 anapita ku nyumba ya mfumu nakalowa ku chipinda cha mlembi. Akuluakulu, mlembi Elisama, Delaya mwana wa Semaya, Elinatani mwana wa Akibori, Gemariya mwana wa Safani, Zedekiya mwana wa Hananiya pamodzi ndi akuluakulu ena onse, anali atasonkhana kumeneko.
he went down into the king's house, into the scribe's chamber. And, lo, all the rulers were sitting there: Elishama the scribe, and Delaiah the son of Shemaiah, and Elnathan the son of Achbor, and Gemariah the son of Shaphan, and Zedekiah the son of Hananiah, and all the rulers.
13 Tsono Mikaya anawafotokozera mawu onse amene anamva pamene Baruki ankawerenga buku lija anthu onse akumva.
Then Micaiah declared to them all the words that he had heard when Baruch read the book in the ears of the people.
14 Pambuyo pake akuluakulu onsewo anatuma Yehudi mwana wa Netaniya, mwana wa Selemiya, mwana wa Kusi, kwa Baruki kukamuwuza kuti, “Bwera ndi buku limene unawerenga kwa anthu.” Ndipo Baruki mwana wa Neriya anapita nalo bukulo kwa anthuwo.
Therefore all the rulers sent Jehudi the son of Nethaniah, the son of Shelemiah, the son of Cushi, to Baruch, saying, Take in thy hand the roll from which thou have read in the ears of the people, and come. So Baruch the son of Neriah took the roll in his hand, and came to them.
15 Iwo anati, “Khala pansi, ndipo tiwerengere bukuli.” Ndipo Baruki anawawerengera.
And they said to him, Sit down now, and read it in our ears. So Baruch read it in their ears.
16 Atamva mawu onsewo, anayangʼanana mwa mantha ndipo anamuwuza Baruki kuti, “Ndithudi tikafotokozera mfumu mawu onsewa.”
Now it came to pass, when they had heard all the words, they turned in fear one toward another, and said to Baruch, We will surely tell the king of all these words.
17 Tsono anamufunsa Baruki kuti, “Tatiwuze, unalemba bwanji mawu onsewa? Kodi ndi Yeremiya anakulembetsa zimenezi?”
And they asked Baruch, saying, Tell us now, How did thou write all these words at his mouth?
18 Baruki anayankha kuti, “Inde, ndi Yeremiya amene anandiwuza mawu onsewa, ndipo ine ndinawalemba ndi utoto mʼbukumu.”
Then Baruch answered them, He pronounced all these words to me with his mouth, and I wrote them with ink in the book.
19 Kenaka akuluakuluwo anamuwuza Baruki kuti, “Iweyo ndi Yeremiya, pitani mukabisale. Munthu aliyense asadziwe kumene muli.”
Then the rulers said to Baruch, Go, hide thee, thou and Jeremiah, and let no man know where ye are.
20 Atayika bukulo mʼchipinda cha mlembi Elisama, analowa mʼbwalo, napita kwa mfumu ndi kukayifotokozera zonse.
And they went in to the king into the court, but they had laid up the roll in the chamber of Elishama the scribe, and they told all the words in the ears of the king.
21 Itamva zimenezi mfumu inatuma Yehudi kuti akatenge bukulo, ndipo Yehudi anakalitenga ku chipinda cha mlembi Elisama ndipo anawerengera mfumu pamodzi ndi akuluakulu ake amene anali naye.
So the king sent Jehudi to fetch the roll, and he took it out of the chamber of Elishama the scribe. And Jehudi read it in the ears of the king, and in the ears of all the rulers who stood beside the king.
22 Unali mwezi wachisanu ndi chinayi ndipo mfumu inali mʼnyumba ya pa nyengo yozizira, ikuwotha moto umene anasonkha.
Now the king was sitting in the winter-house in the ninth month, and the brazier was burning before him.
23 Yehudi ankati akawerenga masamba atatu kapena anayi a bukulo, mfumu inkawangʼamba ndi mpeni ndi kuwaponya pa moto ndipo anapitiriza kuchita zimenezi mpaka buku lonse linapsa.
And it came to pass, when Jehudi had read three or four leaves, that the king cut it with the penknife, and cast it into the fire that was in the brazier, until all the roll was consumed in the fire that was in the brazier.
24 Mfumu pamodzi ndi omutumikira ake onse amene anamva mawu onsewa sanachite mantha kapena kungʼamba zovala zawo.
And they were not afraid, nor tore their garments, neither the king, nor any of his servants who heard all these words.
25 Ngakhale kuti Elinatani, Delaya, ndi Gemariya anapempha mfumu kuti isatenthe bukulo, mfumuyo sinawamvere.
Moreover Elnathan and Delaiah and Gemariah had made intercession to the king that he would not burn the roll, but he would not hear them.
26 Mʼmalo mwake, mfumu inalamula Yerahimeeli mwana wake, Seraya mwana wa Azirieli ndi Selemiya mwana wa Abideeli kuti agwire mlembi Baruki ndi mneneri Yeremiya. Koma pamenepo nʼkuti Yehova atawabisa.
And the king commanded Jerahmeel the king's son, and Seraiah the son of Azriel, and Shelemiah the son of Abdeel, to take Baruch the scribe and Jeremiah the prophet, but Jehovah hid them.
27 Mfumu itatentha buku limene linali ndi mawu amene Yeremiya anamulembetsa Baruki, Yehova anayankhula ndi Yeremiya kuti,
Then the word of Jehovah came to Jeremiah after the king had burned the roll, and the words which Baruch wrote at the mouth of Jeremiah, saying,
28 “Tenganso buku lina ndipo ulembe mawu onse amene anali mʼbuku loyamba lija, limene Yehoyakimu analitentha.
Take thee again another roll, and write in it all the former words that were in the first roll, which Jehoiakim the king of Judah has burned.
29 Ndiponso akamuwuze Yehoyakimu mfumu ya Yuda kuti, ‘Yehova akuti: Iwe unatentha buku lija ndipo unati: Nʼchifukwa chiyani unalemba kuti mfumu ya ku Babuloni idzabwera ndithu kudzawononga dziko lino ndi kupha anthu pamodzi ndi nyama zomwe?’
And concerning Jehoiakim king of Judah thou shall say, Thus says Jehovah: Thou have burned this roll, saying, Why have thou written in it, saying, The king of Babylon shall certainly come and destroy this land, and shall cause to cease from there man and beast?
30 Nʼchifukwa chake kunena za Yehoyakimu mfumu ya Yuda Yehova akuti sipadzaoneka munthu wina wolowa mʼmalo mwake pa mpando wa Davide. Akadzafa mtembo wake udzaponyedwa kunja ndipo udzakhala pa dzuwa masana, ndi pachisanu chowundana usiku.
Therefore thus says Jehovah concerning Jehoiakim king of Judah: He shall have none to sit upon the throne of David. And his dead body shall be cast out in the day to the heat, and in the night to the frost.
31 Ndidzamulanga pamodzi ndi ana ake ndiponso omutumikira ake chifukwa cha zoyipa zawo; ndidzagwetsa pa iwo ndi pa onse amene akukhala mu Yerusalemu ndiponso pa anthu a ku Yuda masautso onse amene ndinawanena, chifukwa sanamvere.”
And I will punish him and his seed and his servants for their iniquity. And I will bring upon them, and upon the inhabitants of Jerusalem, and upon the men of Judah, all the evil that I have pronounced against them, but they did not hearken.
32 Choncho Yeremiya anatenga buku lina napatsa mlembi Baruki mwana wa Neriya, ndipo Yeremiya anamulembetsa mawu onse amene anali mʼbuku limene Yehoyakimu mfumu ya Yuda anatentha. Ndipo anawonjezerapo mawu ambiri monga omwewo.
Then Jeremiah took another roll, and gave it to Baruch the scribe, the son of Neriah, who wrote in it from the mouth of Jeremiah all the words of the book which Jehoiakim king of Judah had burned in the fire, and there were added besides to them many like words.

< Yeremiya 36 >