< Yeremiya 26 >

1 Yehoyakimu, mwana wa Yosiya mfumu ya ku Yuda atayamba kulamulira, Yehova anayankhula ndi Yeremiya kuti,
У почетку царовања Јоакима, сина Јосијиног, цара Јудиног, дође ова реч од Господа говорећи:
2 “Kayime mʼbwalo la Nyumba ya Yehova. Ndipo ukayankhule kwa anthu onse okhala mʼmizinda ya ku Yuda amene amabwera kudzapembedza ku Nyumba ya Yehova. Ukawawuze zonse zomwe ndakulamula; usakasiyeko ndi mawu amodzi omwe.
Овако говори Господ: Стани у трему дома Господњег, и говори свим градовима Јудиним, који долазе да се поклоне у дому Господњем, све речи које ти заповедам да им кажеш, не изостави ни речи,
3 Mwina mwake adzamvera, ndipo aliyense adzatembenuka kuleka njira yake yoyipa. Ndiye ine ndidzaleka osapatsa chilango chimene ndinakonzekera kuti ndiwalange nacho chifukwa cha ntchito zawo zoyipa.
Не би ли послушали и вратили се сваки са свог злог пута, да ми се сажали са зла које им мислим учинити за злоћу дела њихових.
4 Ukawawuze kuti, ‘Yehova akuti: Ngati simundimvera Ine ndi kuleka kutsatira malamulo anga, amene ndakupatsani,
Реци им дакле: Овако вели Господ: ако ме не послушате да ходите у мом закону који сам ставио пред вас,
5 ndipo ngati simumvera mawu a atumiki anga, aneneri amene ndakhala ndikukutumizirani, ngakhale kuti simunawamvere,
Да слушате речи слуга мојих пророка, које вам шаљем, које слах зарана једнако, али их не послушасте,
6 ndiye kuti Ine ndidzasandutsa Nyumba ino kukhala ngati Silo ndipo mzinda uno udzakhala chinthu chotembereredwa pakati pa mitundu yonse ya pa dziko lapansi.’”
Учинићу с домом овим као са Силомом, и град овај даћу у проклетство свим народима на земљи.
7 Ansembe, aneneri ndi anthu onse anamva Yeremiya akuyankhula mawu amenewa mʼNyumba ya Yehova.
А свештеници и пророци и сав народ чуше Јеремију где говори те речи у дому Господњем.
8 Yeremiya atangotsiriza kuwawuza anthu aja zonse zimene Yehova anamulamula kuti ayankhule, ansembe, aneneri pamodzi ndi anthu onse anamugwira ndipo anati, “Uyenera kuphedwa!
И кад Јеремија изговори све што му Господ заповеди да каже свему народу, ухватише га свештеници и пророци и сав народ говорећи: Погинућеш.
9 Chifukwa chiyani walosera mʼdzina la Yehova kuti Nyumba ino idzakhala ngati Silo ndipo mzinda uno udzakhala wopanda anthu ngati chipululu?” Anthu onse anamuzungulira Yeremiya mʼNyumba ya Yehova.
Зашто пророкова у име Господње говорећи: Овај ће дом бити као Силом, и овај ће град опустети да неће у њему нико живети? И скупи се сав народ на Јеремију у дом Господњи.
10 Koma nduna za ku Yuda zitamva zomwe zinachitikazi, zinanyamuka kuchokera ku nyumba yaufumu kupita ku Nyumba ya Yehova, nakakhala pamalo pawo, pa Chipata Chatsopano cha Nyumba ya Yehova.
А кнезови Јудини чувши то дођоше из дома царског у дом Господњи, и седоше пред нова врата Господња.
11 Pamenepo ansembe ndi aneneri anawuza ndunazo pamodzi ndi anthu onse kuti, “Munthu uyu ayenera kuphedwa chifukwa amalosera zoyipira mzinda uno. Inu mwadzimvera nokha zimenezi!”
И рекоше свештеници и пророци кнезовима и свему народу говорећи: Овај је човек заслужио смрт, јер пророкова против овог града, као што чусте својим ушима.
12 Ndipo Yeremiya anawuza nduna zija ndi anthu onse kuti, “Yehova anandituma kunenera mawu onse amene mwawamva otsutsa Nyumba ino ndi mzinda uno.
Тада проговори Јеремија свим кнезовима и свему народу говорећи: Господ ме посла да пророкујем против овог дома и против овог града све што чусте.
13 Tsopano konzani njira zanu ndi zochita zanu ndipo mverani Yehova Mulungu wanu. Mukatero ndiye kuti Yehova adzaleka osakupatsani chilango chimene ankati akupatseni.
Зато поправите путеве своје и дела своја, и послушајте реч Господа Бога свог, и сажалиће се Господу са зла које је изрекао за вас.
14 Kunena za ine, ndili mʼmanja mwanu; mundichite chilichonse chimene mukuganiza kuti ndi chabwino ndi choyenera.
А ја, ево сам у вашим рукама, чините од мене шта мислите да је добро и право.
15 Komatu dziwani kuti ngati mundipha, inu pamodzi ndi mzinda uno ndi onse amene amakhala muno, mudzapalamula mlandu wokhetsa magazi a munthu wosalakwa. Ndithudi Yehova anandituma kuti ndidzayankhule mawu onsewa inu mukumva.”
Али знајте зацело, ако ме убијете, крв праву свалићете на се и на овај град и на становнике његове, јер доиста Господ ме посла к вама да говорим све ове речи, да чујете.
16 Pamenepo ndunazo pamodzi ndi anthu onse anawuza ansembe ndi aneneri kuti, “Munthu uyu sayenera kuphedwa! Pakuti wayankhula kwa ife mʼdzina la Yehova Mulungu wathu.”
Тада рекоше кнезови и сав народ свештеницима и пророцима: Није овај човек заслужио смрт, јер нам је говорио у име Господа Бога нашег.
17 Akuluakulu ena a mʼdzikomo anayimirira ndi kuwuza gulu lonse la anthu kuti,
И усташе неки од старешина земаљских, и проговорише свему збору народном и рекоше:
18 “Mʼmasiku a Hezekiya mfumu ya ku Yuda, Mika wa ku Moreseti ankalosera. Iye ankawuza anthu kuti Yehova Wamphamvuzonse akuti, “‘Ziyoni adzatipulidwa ngati munda, Yerusalemu adzasanduka bwinja, ndipo phiri la Nyumba ya Mulungu lidzasanduka nkhalango yowirira.’
Михеј Морашћанин пророкова у време Језекије, цара Јудиног, и говори свему народу Јудином и рече: Овако вели Господ над војскама: Сион ће се преорати као њива и град ће Јерусалим бити гомила камења, и гора овог дома висока шума.
19 Kodi Hezekiya mfumu ya ku Yuda ndi anthu onse anamupha amene uja? Kodi suja mfumu inaopa Yehova ndi kupempha kuti ayikomere mtima? Ndipo suja Yehova anasintha maganizo ake nʼkuleka kuwalanga monga mʼmene anakonzera? Ifetu tikudziyitanira tsoka lalikulu!”
Је ли га зато убио Језекија, цар Јудин и сав Јуда? Није ли се побојао Господа и молио се Господу? И Господу се сажали ради зла које беше изрекао на њих; ми дакле чинимо велико зло душама својим.
20 (Panalinso munthu wina, Uriya mwana wa Semaya wa ku Kiriati-Yeyarimu, amene ankalosera mʼdzina la Yehova. Iyeyu analosera za mzinda uno ndi dziko lino monga mmene wachitira Yeremiya.
И још беше један који пророкова у име Господње, Урија син Семајин из Киријат-Јарима; он пророкова против овог града и против ове земље исто онако као Јеремија.
21 Mfumu Yehoyakimu, ankhondo ake onse ndi nduna zake anamva mawu akewo, ndipo anafuna kumupha. Koma Uriya atamva zimenezi, anachita mantha nathawira ku Igupto.
И кад чу цар Јоаким и све војводе његове и сви кнезови речи његове, тражи га цар да га убије; а Урија чувши побоја се и побеже и дође у Мисир.
22 Komabe Mfumu Yehoyakimu anatuma Elinatani mwana wa Akibori pamodzi ndi anthu ena, ku Igupto.
А цар Јоаким посла неке у Мисир, Елнатана сина Аховоровог и друге с њим.
23 Iwo anakamutenga Uriya ku Igupto kuja nabwera naye kwa Mfumu Yehoyakimu. Iye anamupha ndi lupanga ndipo mtembo wake anakawutaya ku manda a anthu wamba).
И они изведоше Урију из Мисира и доведоше к цару Јоакиму, и уби га мачем, и баци тело његово у гробље простог народа.
24 Koma Ahikamu mwana wa Safani ndiye anateteza Yeremiya, motero sanamupereke kwa anthu kuti amuphe.
Али рука Ахикама, сина Сафановог, би уз Јеремију, те га не предаше у руке народу да га погубе.

< Yeremiya 26 >