< Yeremiya 24 >

1 Nebukadinezara, mfumu ya ku Babuloni anatenga ukapolo Yekoniya mwana wa Yehoyakimu mfumu ya ku Yuda pamodzi ndi nduna zake, anthu aluso ndi akatswiri a ku Yuda ndi kupita nawo ku Babuloni. Pambuyo pake Yehova anandionetsa madengu awiri a nkhuyu atayikidwa pa khomo pa Nyumba ya Yehova.
L'Eternel me fit voir [une vision], et voici deux paniers de figues, posés devant le Temple de l'Eternel, après que Nébucadnetsar Roi de Babylone eut transporté de Jérusalem Jéchonias fils de Jéhojakim, Roi de Juda, et les principaux de Juda, avec les charpentiers et les serruriers, et les eut emmenés à Babylone.
2 Mʼdengu limodzi munali nkhuyu zabwino kwambiri, ngati nkhuyu zoyambirira kucha. Mʼdengu linalo munali nkhuyu zoyipa kwambiri zosati nʼkudya.
L'un des paniers avait de fort bonnes figues, comme sont d'ordinaire les figues qui sont les premières mûres; et l'autre panier avait de fort mauvaises figues, lesquelles on n'aurait pu manger, tant elles étaient mauvaises.
3 Yehova anandifunsa kuti, “Yeremiya, kodi ukuona chiyani?” Ndinayankha kuti, “Ndikuona nkhuyu zabwino kwambiri ndi nkhuyu zoyipa zosati nʼkudya.”
Et l'Eternel me dit: que vois-tu, Jérémie? Et je répondis: des figues, de bonnes figues, fort bonnes; et de mauvaises, fort mauvaises, lesquelles on ne saurait manger, tant elles sont mauvaises.
4 Tsono Yehova anandiwuza kuti,
Alors la parole de l'Eternel me fut [adressée], en disant:
5 “Ine Yehova, Mulungu wa Israeli ndikuti, ‘Anthu a ku Yuda amene ndinawachotsa ku malo ano nʼkupita nawo ku ukapolo ku dziko la Ababuloni ndikuwafanizira ndi nkhuyu zabwinozi.
Ainsi a dit l'Eternel, le Dieu d'Israël: comme ces figues sont bonnes, ainsi je me souviendrai, pour leur faire du bien, de ceux qui ont été transportés de Juda, lesquels j'ai envoyés hors de ce lieu au pays des Caldéens.
6 Ndidzaonetsesa kuti ndiwachitire zabwino ndipo ndidzabwera nawonso ku dziko lino. Ndidzawamanga osati kuwapasula; ndidzawadzala osati kuwazula.
Et je mettrai mes yeux sur eux pour leur faire du bien, et je les ferai retourner en ce pays, je les y rétablirai, et je ne les ruinerai plus, je les planterai, et je ne les arracherai point.
7 Ndidzawapatsa mtima woti andidziwe kuti ndine Yehova. Adzakhala anthu anga ndipo Ine ndidzakhala Mulungu wawo, chifukwa adzabwerera kwa Ine ndi mtima wawo wonse.
Et je leur donnerai un cœur pour me connaître, [pour connaître, dis-je], que je suis l'Eternel; et ils seront mon peuple, et je serai leur Dieu: car ils se retourneront à moi de tout leur cœur.
8 “‘Koma monga nkhuyu zoyipa zija, zomwe ndi zoyipa kwambiri zosati nʼkudya,’ Yehova akuti, ‘ndi mmene ndidzalangire Zedekiya mfumu ya ku Yuda, nduna zake pamodzi ndi otsala a mu Yerusalemu, kaya adzakhala ali mʼdziko muno kapena mʼdziko la Igupto.
Et comme ces figues sont si mauvaises qu'on n'en peut manger, tant elles sont mauvaises; ainsi certainement, a dit l'Eternel, je rendrai tel Sédécias le Roi de Juda, et les principaux de sa Cour, et le reste de Jérusalem qui sont demeurés dans ce pays, et ceux qui s'habitueront au pays d'Egypte.
9 Ndidzawasandutsa chinthu chonyansa kwa maufumu onse a dziko lapansi, chinthu chonyozeka ndi chopandapake, chinthu chochitidwa chipongwe ndi chotembereredwa kulikonse kumene ndidzawabalalitsira.
Et je les livrerai pour être agités pour leur malheur par tous les Royaumes de la terre, et pour être en opprobre, en proverbe, en raillerie, et en malédiction par tous les lieux où je les aurai chassés.
10 Ndidzawatumizira nkhondo, njala ndi mliri mpaka atawonongedwa mʼdziko limene ndinawapatsa iwo ndi makolo awo.’”
Et j'enverrai sur eux l'épée, la famine, et la mortalité, jusqu’à ce qu'ils soient consumés de dessus la terre que je leur avais donnée, à eux, et à leurs pères.

< Yeremiya 24 >