< Yesaya 7 >

1 Pamene Ahazi mwana wa Yotamu, mdzukulu wa Uziya anali mfumu ya Yuda, Rezini mfumu ya Siriya ndi Peka mwana wa Remaliya, mfumu ya Israeli anabwera kudzathira nkhondo mzinda wa Yerusalemu, koma sanathe kuwugonjetsa.
Og det skete i de Dage da Akaz, Jotams Søn, Uzzijas Sønnesøn, var Konge i Juda, at Kong Rezin af Syrien og Remaljas Søn, kong Peka af Israel, drog op for at angribe Jerusalem, hvad de dog ikke var stærke nok til.
2 Tsono nyumba ya Davide inawuzidwa kuti, “Dziko la Siriya lagwirizana ndi Efereimu.” Choncho mfumu Ahazi ndi anthu ake ananjenjemera, monga momwe mitengo ya mʼnkhalango imagwedezekera ndi mphepo.
Da det meldtes Davids Hus, at Syrerne havde lejret sig i Efraim, skjalv hans og hans Folks Hjerte, som Skovens Træer skælver for Vinden.
3 Pamenepo Yehova anawuza Yesaya kuti, “Tuluka, iwe ndi mwana wako Seariyasubu, mupite mukakumane ndi Ahazi kumapeto kwa ngalande yamadzi yochokera ku Dziwe Lakumtunda, pa msewu wopita ku Munda wa mmisiri wochapa nsalu.
Så sagde HERREN til Esajas: "Med din Søn Sjearjasjub" skal du gå Akaz i Møde ved Enden af Øvredammens Vandledning ved Vejen til Blegepladsen
4 Ukamuwuze kuti, ‘Chenjera, khala phee ndipo usaope. Usataye mtima chifukwa cha zitsa ziwiri zomwe zikufuka, chifukwa cha ukali woopsa wa Rezini ndi Siriya, ndiponso wa Peka mwana wa Remaliya.
og sige til ham: Tag dig i Vare og hold dig i Ro! Frygt ikke og lad ikke dit Hjerte ængste sig for disse to rygende Brandstumper, for Rezins og Syriens og Remaljas Søns fnysende Vrede!
5 Mfumu ya Siriya, Efereimu ndi mwana wa Remaliya apangana kuti akuchitire choyipa. Akunena kuti,
Fordi Syrien, Efraim og Remaljas Søn har lagt onde Råd op imod dig og siger:
6 ‘Tiyeni tikalimbane ndi Yuda. Tiyeni tiliwononge ndi kuligawa; tiligawane pakati pathu, ndipo tilonge ufumu mwana wa Tabeeli kumeneko.’
Lad os drage op mod Juda og indjage det Skræk, lad os tilrive os det og gøre Tabeals Søn til Konge der!
7 Komabe zimene akunena Ambuye Yehova ndi izi: “‘Zimenezo sizidzatheka, sizidzachitika konse,
derfor, så siger den Herre HERREN: Det skal ikke lykkes; det skal ikke ske!
8 pakuti Siriya amadalira Damasiko, ndipo Damasiko amadalira mfumu Rezini basi. Zisanathe zaka 65 Efereimu adzawonongedwa kotheratu, sadzakhalanso mtundu wa anthu.
Thi Syriens Hoved er Damaskus, og Damaskus's Hoved er Rezin, og om fem og tresindstyve År er Efraim knust og ikke længer et Folk.
9 Dziko la Efereimu limadalira Samariya ndipo Samariya amadalira mwana wa Remaliya basi. Mukapanda kulimbika pa chikhulupiriro chanu, ndithu simudzalimba konse.’”
Og Efraims Hoved er Samaria, og Samarias Hoved er Remaljas Søn. Er I ikke troende, bliver I ikke boende."
10 Yehova anayankhulanso ndi Ahazi,
Fremdeles sagde HERREN til Akaz:
11 “Pempha chizindikiro kwa Yehova Mulungu wako, chikhale chozama ngati manda kapena chachitali ngati mlengalenga.” (Sheol h7585)
"Kræv dig et Tegn af HERREN din Gud nede i Dødsriget eller oppe i Himmelen!" (Sheol h7585)
12 Koma Ahazi anati, “Ine sindipempha; sindikufuna kuyesa Yehova.”
Men Akaz svarede: "Jeg kræver intet, jeg frister ikke HERREN."
13 Apo Yesaya anati, “Imva tsopano, iwe nyumba ya Davide! Kodi sikokwanira kutopetsa anthu? Kodi mudzayeseranso kutopetsa Mulungu wanga?
Da sagde Esajas: "Hør nu, Davids Hus! Er det eder ikke nok at trætte Mennesker, siden I også trætter min Gud?
14 Nʼchifukwa chake Ambuye mwini adzakupatsani chizindikiro: Onani, namwali adzakhala woyembekezera ndipo adzabala mwana wamwamuna, ndipo mwanayo adzamutcha Imanueli.
Derfor vil Herren selv give eder et Tegn: Se, Jomfruen bliver frugtsommelig og føder en Søn, og hun kalder ham Immanuel".
15 Azidzadya chambiko ndi uchi, mpaka atadziwa kukana choyipa ndi kusankha chabwino.
Surmælk og Vildhonning skal være hans Føde, ved den Tid han ved at vrage det onde og vælge det gode;
16 Koma nthawi yokana choyipa ndi kusankha chabwino kwa mwanayo isanafike, mayiko a mafumu awiri amene amakuopsaniwo adzakhala atasanduka bwinja.
thi før Drengen ved at vrage det onde og vælge det gode, skal Landet, for hvis to Konger du gruer, være folketomt.
17 Yehova adzabweretsa pa inu, pa anthu anu ndiponso pa nyumba ya bambo wanu masiku a mavuto woti sanakhalepo kuyambira tsiku limene Efereimu anapatukana ndi Yuda. Yehova adzabweretsa mfumu ya ku Asiriya.”
Over dig, dit Folk og din Faders Hus vil Herren bringe Dage, hvis Lige ikke har været, siden Efraim rev sig løs fra Juda: Assyrerkongen!"
18 Tsiku limenelo Yehova adzalizira likhweru ntchentche zochokera ku mitsinje yakutali ku Igupto, ndiponso njuchi zochokera ku dziko la Asiriya.
På hin Dag skal HERREN fløjte ad Fluerne ved Udløbet af Ægyptens Strømme og ad Bierne i Assyrien;
19 Onsewo adzafika ndi kudzakhazikika mu zigwa zozama, mʼmingʼalu ya matanthwe ndi mʼzitsamba zonse zaminga ndiponso ponse pamene pali malo omwetsera ziweto.
og de skal komme og alle til Hobe kaste sig over Dalkløfter og Klipperevner, over hvert Tjørnekrat og hvert Vandingssted.
20 Tsiku limenelo Ambuye adzalemba ganyu ometa ochokera kutsidya kwa Mtsinje, ndiye mfumu ya ku Asiriya, kudzameta tsitsi lanu la ku mutu ndi la mʼmiyendo ndi ndevu zomwe.
På hin Dag afrager Herren med en hinsides Floden lejet Ragekniv, Assyrerkongen, både Hovedhåret og Kroppens Hår; ja, selv Skægget skraber den af.
21 Tsiku limenelo adzangosunga ngʼombe yayikazi yayingʼono ndi mbuzi ziwiri.
På hin Dag kan en Mand holde sig en ung Ko og et Par Får;
22 Ndipo chifukwa cha kuchuluka kwa mkaka umene ziwetozi zidzapereka, munthuyo azidzadya chambiko. Aliyense amene adzatsalire mʼdzikomo azidzadya chambiko ndi uchi.
og på Grund af den megen Mælk, de giver, skal han spise Sur mælk; thi Surmælk og Vildhonning skal enhver, der er tilbage i Landet, spise.
23 Tsiku limenelo, paliponse pamene panali mitengo ya mpesa 1,000 ndipo mtengo wake ndi wokwana masekeli asiliva 1,000, padzamera mkandankhuku ndi minga.
På hin Dag skal det ske, at hvert et Sted, hvor der nu er tusind Vinstokke, tusind Sekel Sølv værd, skal blive til Torn og Tidsel;
24 Anthu adzapita kumeneko kukachita uzimba ali ndi uta ndi mivi, popeza kuti mʼdziko monsemo mudzakhala mkandankhuku ndi minga.
med Pil og Bue kommer man der, thi hele Landet skal blive til Torn og Tidsel;
25 Ndipo mʼmapiri monse mʼmene kale munkalimidwa ndi khasu, simudzapitamo kuopa mkandankhuku ndi minga; malowo adzasanduka odyetserako ngʼombe ndi nkhosa.
og alle de Bjerge, der nu dyrkes med Hakke, skal man holde sig fra af Frygt for Torn og Tidsel. Det bliver Overdrev for Okser og trædes ned af Får.

< Yesaya 7 >