< Yesaya 66 >

1 Yehova akuti, “Kumwamba ndi mpando wanga waufumu ndipo dziko lapansi ndilo chopondapo mapazi anga. Tsono nyumba ili kuti yomwe mundimangire, ndipo malo ali kuti amene inu mungandikonzere kuti ndizipumuliramo?
This is what Yahweh says, “Heaven is my throne, and the earth is my footstool. Where then is the house you will build for me? Where is the place where I may rest?
2 Kodi si manja anga amene anapanga zinthu zonsezi, motero zonsezi ndi zanga?” Akutero Yehova. “Koma munthu amene ndimakondwera naye ndi uyu: amene ali wodzichepetsa ndi wosweka mtima, ndipo amamvera mawu anga.
My hand has made all these things; that is how these things came to be—this is Yahweh's declaration. This is the man of whom I approve, the broken and contrite in spirit, and who trembles at my word.
3 Koma aliyense amene amapereka nsembe ngʼombe yayimuna amaphanso munthu, ndipo aliyense amene amapereka mwana wankhosa, amaphanso galu. Aliyense amene amapereka nsembe chopereka cha chakudya amaperekanso magazi a nkhumba. Ndipo amene amafukiza lubani pa guwa lansembe la chikumbutso amapembedzanso fano. Popeza iwo asankha njira zawozawo, ndiponso kusangalatsidwa ndi zonyansa zawo.
He who slaughters an ox also murders a man; he who sacrifices a lamb also breaks a dog's neck; he who offers a grain offering offers swine's blood; he who offers a memorial of incense also blesses wickedness. They have chosen their own ways, and they take pleasure in their abominations.
4 Inenso ndawasankhira chilango chowawa ndipo ndidzabweretsa pa iwo zimene amaziopa zija. Pakuti pamene ndinawayitana palibe amene anayankha, pamene ndinayankhula palibe amene anatchera khutu. Anachita zoyipa pamaso panga ndi kusankha kuchita zimene zimandinyansa zija.”
In the same way I will choose their own punishment; I will bring on them what they fear, because when I called, no one answered; when I spoke, no one listened. They did what was evil in my sight, and chose to do what displeases me.”
5 Imvani mawu a Yehova, inu amene mumanjenjemera ndi mawu ake: “Abale anu amene amakudani, ndi kukuchotsani pakati pawo chifukwa cha dzina langa, amanena kuti, ‘Yehova alemekezeke kuti ife tione chimwemwe chanu!’ Koma ndi iwowo amene adzachite manyazi.
Hear the word of Yahweh, you who tremble at his word, “Your brothers who hate and exclude you for my name's sake have said, 'May Yahweh be glorified, then we will see your joy,' but they will be put to shame.
6 Imvani mfuwu mu mzinda, imvani phokoso mʼNyumba ya Mulungu! Limenelo ndi liwu la Yehova, kulanga adani ake onse.
A sound of battle tumult comes from the city, a sound from the temple, the sound of Yahweh paying back his enemies.
7 “Mzinda uli ngati amayi apakati amene asanayambe kumva zowawa wachira kale; asanayambe kumva ululu, wabala kale mwana wamwamuna.
Before she goes into labor, she gives birth; before pain is upon her, she gave birth to a son.
8 Ndani anamvapo zinthu zoterezi? Ndani anazionapo zinthu zoterezi? Kodi dziko nʼkupangika tsiku limodzi, kapena mtundu wa anthu nʼkubadwa tsiku limodzi? Komatu Ziyoni atangoyamba kumva zowawa nthawi yomweyo anabereka ana ake.
Who has heard of such a thing? Who has seen such things? Will a land be born in one day? Can a nation be established in one moment? Yet as soon as Zion goes into labor, she gives birth to her children.
9 Kodi Ine ndingangofikitsa amayi apakati mpaka nthawi yake yochira, koma osalola kuti abaledi mwana?” akutero Yehova. “Kodi ndingatseke mimba pa nthawi yoti abeleke?” akutero Mulungu wako.
Do I bring a baby to the birth opening and not permit the child to be born?—asks Yahweh. Or do I bring a child to moment of delivery and then hold it back?—asks your God.”
10 “Kondwera nayeni Yerusalemu ndipo musangalale chifukwa cha Iye, inu nonse amene mumakonda Yerusalemu, kondwera nayeni kwambiri, nonse amene mumamulira.
Rejoice with Jerusalem and be glad for her, all you who love her; rejoice with her, all you who mourned over her!
11 Pakuti mudzagawana naye ulemerero wake ngati kuyamwa ndi kukhuta mkaka wambiri wa mʼmawere a chitonthozo chake.”
For you will nurse and be satisfied; with her breasts you will be comforted; for you will drink them to the full and be delighted with the abundance of her glory.
12 Yehova akuti, “Ndidzamupatsa mtendere ngati mtsinje wa madzi, ndiponso chuma cha anthu a mitundu ina ngati mtsinje wosefukira. Mudzakhala ngati mwana woyamwa amene amayi ake amunyamulira pambalipa, kapena kumufungata pa miyendo yake.
This is what Yahweh says, “I am about to spread prosperity over her like a river, and the riches of the nations like an overflowing stream. You will nurse at her side, be carried in her arms, and be dandled on her knees.
13 Monga momwe amayi amasangalatsira mwana wawo, moteronso Ine ndidzakusangalatsani; ndipo mudzasangalala chifukwa cha Yerusalemu.”
As a mother comforts her child, so I will comfort you, and you will be comforted in Jerusalem.”
14 Mukadzaona zimenezi mitima yanu idzakondwera. Mudzabiriwira ngati udzu. Zimenezi zidzakulimbikitsani ndi kukupatsani moyo wamphamvu. Mudzadziwa kuti ndimathandiza amene amanditumikira ndi kuti ndimakwiyira adani anga.
You will see this, and your heart will rejoice, and your bones will sprout like the tender grass. The hand of Yahweh will be made known to his servants, but he will show his anger against his enemies.
15 Taonani, Yehova akubwera ngati moto, ndipo magaleta ake ali ngati kamvuluvulu; Iye adzaonetsa mkwiyo wake nadzalanga adani ake ndi malawi amoto.
For look, Yahweh is coming with fire, and his chariots are coming like the windstorm to bring the heat of his anger and his rebuke with flames of fire.
16 Pakuti Yehova adzalanga anthu onse ndi moto ndi lupanga, Yehova adzapha anthu ambiri.
For Yahweh executes judgment on mankind by fire and with his sword. Those killed by Yahweh will be many.
17 Yehova akuti, “Amene amadzipatula ndi kudziyeretsa okha kuti apite ku minda, ali ndi mtsogoleri awo, nʼkumadya nyama ya nkhumba, mbewa ndi zinthu zina zonyansa, onsewa adzafera limodzi.”
They consecrate themselves and make themselves pure, so they may enter the gardens, following the one in the middle of those who eat the flesh of pig and abominable things like mice. “They will come to an end—this is Yahweh's declaration.
18 “Ndipo Ine, chifukwa cha zochita zawo ndi maganizo awo, ndili pafupi kubwera kudzasonkhanitsa mitundu yonse ya anthu ndi ziyankhulo zonse. Iwo adzabwera ndi kuona ulemerero wanga.
For I know their deeds and their thoughts. The time is coming when I will gather all nations and languages. They will come and will see my glory.
19 “Ndidzayika chizindikiro pakati pawo, ndipo ndidzatumiza ena mwa iwowa amene anapulumuka kuti apite kwa anthu a mitundu ina inu ku Tarisisi, ku Libiya ndi ku Ludi (akatswiri a mauta) ku Tubala ndi Grisi, ndi ku mayiko akutali a mbali mwa nyanja amene sanamvepo za mbiri yanga kapena kuona ulemerero wanga. Iwo adzalalika za ulemerero wanga pakati pa anthu a mitundu ina.
I will set a mighty sign among them. Then I will send survivors from them to the nations: To Tarshish, Put, and Lud, archers who draw their bows, to Tubal, Javan, and to the distant coastlands where they have not heard about me nor seen my glory. They will proclaim my glory among the nations.
20 Ndipo adzabwera nawo abale anu onse ngati mphatso yopereka kwa Yehova kuchokera kwa anthu a mitundu yonse. Iwo adzakwera nawo kupita ku Yerusalemu, phiri langa loyera ku Yerusalemu monga nsembe kwa Yehova, atakwera akavalo, magaleta ndi ngolo, ndi pa abulu ndi ngamira,” akutero Yehova. “Adzabwera nawo ngati momwe Aisraeli amabwerera ndi zopereka zachakudya ku Nyumba ya Yehova mu ziwiya zoyeretsedwa monga mwa mwambo.
They will bring back all your brothers out of all the nations, as an offering to Yahweh. They will come on horses, and in chariots, in wagons, on mules, and on camels, to my holy mountain Jerusalem—says Yahweh. For the people of Israel will bring a grain offering in a clean vessel into the house of Yahweh.
21 Ndipo ndidzasankha ena mwa iwonso kukhala ansembe ndi Alevi,” akutero Yehova.
Some of these I will even choose as priests and Levites—says Yahweh.
22 “Monga momwe mlengalenga mwatsopano ndi dziko lapansi latsopano zimene ndidzapanga zidzakhala mpaka muyaya pamaso panga, ndi chonchonso dzina lanu ndi zidzukulu zanu zidzakhalire.” Akutero Yehova.
For just as the new heavens and the new earth that I will make will remain before me—this is Yahweh's declaration—so your descendants will remain, and your name will remain.
23 “Anthu a mitundu yonse adzabwera kudzandipembedza ku Yerusalemu, pa chikondwerero chilichonse cha pokhala pa mwezi watsopano ndi tsiku la Sabata lililonse,” akutero Yehova.
From one month to the next, and from one Sabbath to the next, all people will come to bow down to me—says Yahweh.
24 “Akamachoka adzaona mitembo ya anthu amene anandiwukira Ine. Mphutsi zawo sizidzafa, kapena moto wawo sudzazimitsidwa. Anthu a mitundu ina yonse powaona adzanyansidwa nawo.”
They will go out and see the dead bodies of the men who have rebelled against me, for the worms that eat them will not die, and the fire that consumes them will not be quenched; and it will be an abhorrence to all flesh.”

< Yesaya 66 >