< Yesaya 54 >

1 “Sangalala, iwe mayi wosabala, iwe amene sunabalepo mwana; imba nyimbo, ndi kufuwula mwachimwemwe, iwe amene sunamvepo ululu wa pobereka; chifukwa mkazi wosiyidwa adzakhala ndi ana ambiri kuposa mkazi wokwatiwa,” akutero Yehova.
Rejoice, you barren that bear not; break forth and cry, you that do not travail: for more are the children of the desolate than of her that has a husband: for the Lord has said,
2 Kulitsa malo omangapo tenti yako, tambasula kwambiri nsalu zake, usaleke; talikitsa zingwe zako, limbitsa zikhomo zako.
Enlarge the place of your tent, and of your curtains: fix [the pins], spare not, lengthen your cords, and strengthen your pins;
3 Pakuti udzasendeza malire ako kumanja ndi kumanzere; ndipo zidzukulu zako zidzalanda dziko la anthu a mitundu ina ndipo zidzakhala mʼmizinda yawo yosiyidwa.
spread forth [your tent] yet to the right and the left: for your seed shall inherit the Gentiles, and you shall make the desolate cities to be inhabited.
4 “Usachite mantha; sadzakunyozanso. Usakhumudwe; sudzapeputsidwanso. Udzayiwala za manyazi zimene zinakuchitikira nthawi ya unyamata wako ndipo za manyazi zimene zinakuchitikira pa nthawi ya umasiye wako sudzazikumbukanso.
Fear not, because you has been put to shame, neither be confounded, because you was reproached: for you shall forget your former shame, and shall no more at all remember the reproach of your widowhood.
5 Pakuti Mlengi wako ali ngati mwamuna wako, dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse. Woyerayo wa Israeli ndiye Mpulumutsi wanu; dzina lake ndi Mulungu wa dziko lonse lapansi.
For [it is] the Lord that made you; the Lord of hosts is his name: and he that delivered you, he is the God of Israel, [and] shall be called [so] by the whole earth.
6 Yehova wakuyitananso, uli ngati mkazi wosiyidwa ndi wodzaza ndi chisoni mu mtima, mkazi amene anakwatiwa pa unyamata wake kenaka nʼkukanidwa,” akutero Mulungu wako.
The Lord has not called you as a deserted and faint-hearted woman, nor as a woman hated from [her] youth, says your God.
7 “Kwa kanthawi kochepa, Ine ndinakusiya, koma ndidzakutenganso chifukwa ndimakukonda kwambiri.
For a little while I left you: but with great mercy will I have compassion upon you.
8 Ndinakufulatira kwa kanthawi kochepa ndili wokwiya kwambiri. Koma ndi kukoma mtima kwanga kwa muyaya, ndidzakuchitira chifundo,” akutero Yehova Mpulumutsi wako.
In a little wrath I turned away my face from you; but with everlasting mercy will I have compassion upon you, says the Lord that delivers you.
9 “Kwa ine zimenezi zili ngati mmene zinalili mʼnthawi ya Nowa. Monga ndinalumbira nthawi imeneyo kuti sindidzawononganso dziko lapansi ndi madzi. Kotero tsopano ndalumbira kuti sindidzakupseraninso mtima, sindidzakudzudzulaninso.
From the time of the water of Noe this is my [purpose]: as I sware to him at that time, [saying] of the earth, I will no more be angry with you, neither when you are threatened,
10 Ngakhale mapiri atagwedezeka ndi zitunda kusunthidwa, koma chikondi changa chosasinthika pa iwe sichidzatha. Pangano langa lamtendere silidzasintha,” akutero Yehova amene amakuchitira chifundo.
shall the mountains depart, nor shall your hills be removed: so neither shall my mercy fail you, nor shall the covenant of your peace be at all removed: for the Lord [who is] gracious to you has spoken [it].
11 “Iwe mzinda wozunzika, wokunthidwa ndi namondwe ndiponso wopanda wokutonthoza, Ine ndidzakongoletsa miyala yako. Maziko ako ndidzamanga ndi miyala ya safiro.
Afflicted and outcast you has not been comforted: behold, I [will] prepare carbuncle [for] your stones, and sapphire for your foundations;
12 Ndidzamanga nsanja zako zankhondo ndi miyala yokongola ya rubi. Ndidzamanga zipata zako ndi miyala yonyezimira ngati moto, ndipo linga lako lonse lidzakhala la miyala yamtengowapatali.
and I will make your buttresses jasper, and your gates crystal, and your border precious stones.
13 Yehova adzaphunzitsa ana ako onse, ndipo ana ako adzakhala ndi mtendere wochuluka.
And [I will cause] all your sons [to be] taught of God, and your children [to be] in great peace.
14 Udzakhazikika mʼchilungamo chenicheni: Sudzakhalanso wopanikizika, chifukwa sudzaopa kanthu kalikonse. Sudzakhalanso ndi mantha chifukwa manthawo sadzafika pafupi ndi iwe.
And you shall be built in righteousness: abstain from injustice, and you shall not fear; and trembling shall not come near you.
15 Ngati wina adzakuthirani nkhondo, si ndine amene ndachititsa; aliyense amene adzalimbana nanu adzagonja chifukwa cha iwe.
Behold, strangers shall come to you by me, and shall sojourn with you, and shall run to you for refuge.
16 “Taona, ndi Ine amene ndinalenga munthu wosula zitsulo amene amakoleza moto wamakala ndi kusula zida zoti azigwiritse ntchito. Ndipo ndine amene ndinalenga munthu wosakaza kuti awononge;
Behold, I have created you, not as the coppersmith blowing coals, and bringing out a vessel [fit] for work; but I have created you, not for ruin, that [I] should destroy [you].
17 palibe chida chopangidwa ndi mdani chimene chidzakupweteke, ndipo onse okuneneza pa mlandu udzawatsutsa. Umu ndimo adzapezekere atumiki a Yehova. Chipambano chawo chichokera kwa Ine,” akutero Yehova.
I will not suffer any weapon formed against you to prosper; and every voice that shall rise up against you for judgment, you shall vanquish them all; and your adversaries shall be [condemned] thereby. There is an inheritance to them that serve the Lord, and you shall be righteous before me, says the Lord.

< Yesaya 54 >

A Dove is Sent Forth from the Ark
A Dove is Sent Forth from the Ark