< Yesaya 32 >

1 Taonani, kudzakhala mfumu ina imene idzalamulira mwachilungamo, ndipo akalonga ake adzaweruza molungama.
Evo, car æe carovati pravo i knezovi æe vladati po pravdi.
2 Munthu aliyense adzakhala ngati pothawirapo mphepo ndi malo obisalirapo namondwe, adzakhala ngati mitsinje ya mʼchipululu, ngati mthunzi wa thanthwe lalikulu la mʼdziko lowuma.
I èovjek æe biti kao zaklon od vjetra, i kao utoèište od poplave, kao potoci na suhu mjestu, kao sjen od velike stijene u zemlji sasušenoj.
3 Ndipo maso a anthu openya sadzakhalanso otseka, ndipo makutu a anthu akumva adzamvetsetsa.
I oèi onijeh koji vide neæe biti zaslijepljene, i uši onijeh koji èuju slušaæe.
4 Anthu a mtima wopupuluma adzadziwa ndi kuchita zinthu mofatsa, ndipo anthu ovutika kuyankhula adzayankhula mosadodoma ndi momveka.
I srce nerazumnijeh razumjeæe mudrost, i jezik mutavijeh govoriæe brzo i razgovijetno.
5 Chitsiru sichidzatchedwanso munthu waulemu wake ndipo munthu woyipa sadzalemekezedwa.
Nevaljalac se neæe više zvati knez, niti æe se tvrdica nazivati podašnijem.
6 Pakuti munthu opusa amayankhula zauchitsiru, amaganiza kuchita zoyipa: Iye amachita zoyipira Mulungu, ndipo amafalitsa zolakwika zokhudza Yehova; anjala sawapatsa chakudya ndipo aludzu sawapatsa madzi.
Jer nevaljalac o nevaljalstvu govori, i srce njegovo gradi bezakonje, radeæi licemjerno i govoreæi na Boga laž, da isprazni dušu gladnomu i napoj žednomu da uzme.
7 Munthu woyipa njira zake ndi zoyipanso, iye kwake nʼkulingalira zinthu zoyipa. Amalingalira zakuti awononge anthu aumphawi ndi mabodza ake ngakhale kuti waumphawiyo akuyankhula zoona.
I sprave tvrdièine zle su; smišlja lukavštine da zatre nište rijeèima lažnijem i kad siromah govori pravo.
8 Koma munthu wolemekezeka amalingaliranso kuchita zinthu zabwino, Iye amakhazikika pa zinthu zabwinozo.
Ali knez smišlja kneževski, i ustaje da radi kneževski.
9 Khalani maso, inu akazi amene mukungokhala wopanda kulingalira kuti kunja kulinji ndipo imvani mawu anga. Inu akazi odzitama, imvani zimene ndikunena!
Ustanite, žene mirne, slušajte glas moj; kæeri bezbrižne, èujte rijeèi moje.
10 Pakapita chaka ndi masiku pangʼono inu akazi amatama mudzanjenjemera; chifukwa mitengo ya mphesa idzakanika ndipo zipatso sizidzaoneka.
Za mnogo godina biæete u smetnji, vi bezbrižne; jer neæe biti berbe, i sabiranje neæe doæi.
11 Nthunthumirani inu okhala mosatekesekanu; ndipo njenjemerani, inu akazi omadzikhulupirira nokhanu. Vulani zovala zanu, ndipo valani ziguduli mʼchiwuno mwanu.
Strašite se, vi mirne; drkæite, vi bezbrižne, svucite se, budite gole, i pripašite oko sebe kostrijet,
12 Dzigugudeni pachifuwa mwachisoni chifukwa minda yachonde, ndi mphesa yawonongeka.
Bijuæi se u prsi za lijepijem njivama, za rodnijem èokotima.
13 Mʼdziko la anthu anga mwamera minga ndi mkandankhuku. Zoona, mulilire nyumba zonse zachikondwerero ndi mzinda uno umene unali wachisangalalo.
Trnje i èkalj niknuæe na zemlji naroda mojega, i po svijem kuæama veselijem, u gradu veselom.
14 Nyumba yaufumu idzasiyidwa, mzinda waphokoso udzakhala wopanda anthu; malinga ndi nsanja zidzasanduka chipululu mpaka muyaya. Abulu adzasangalalamo ndipo ziweto zidzapezamo msipu.
Jer æe se dvorovi ostaviti, vreve gradske nestaæe; kule i stražare postaæe peæine dovijeka, radost divljim magarcima i paša stadima,
15 Yehova adzatipatsa mzimu wake, ndipo dziko lachipululu lidzasanduka munda wachonde, ndipo munda wachonde udzakhala ngati nkhalango.
Dokle se ne izlije na nas duh s visine i pustinja postane njiva a njiva se stane uzimati za šumu.
16 Tsono mʼchipululu mudzakhala chiweruzo cholungama ndipo mʼminda yachonde mudzakhala chilungamo.
Tada æe sud stanovati u pustinji, i pravda æe stajati na njivi.
17 Mtendere udzakhala chipatso chachilungamo; zotsatira za chilungamo zidzakhala bata ndi kudzidalira mpaka muyaya.
I mir æe biti djelo pravde, što æe pravda uèiniti biæe pokoj i bezbrižnost dovijeka.
18 Anthu anga adzakhala mʼmidzi yamtendere, mʼnyumba zodalirika, ndi malo osatekeseka a mpumulo.
I moj æe narod sjedjeti u mirnu stanu i u šatorima pouzdanijem, na poèivalištima tihim.
19 Ngakhale nkhalango idzawonongedwa ndi matalala ndipo mzinda udzagwetsedwa mpaka pansi,
Ali æe grad pasti na šumu, i grad æe se vrlo sniziti.
20 inutu mudzakhala odalitsika ndithu. Mudzadzala mbewu zanu mʼmbali mwa mtsinje uliwonse, ndipo ngʼombe zanu ndi abulu anu zidzadya paliponse.
Blago vama koji sijete pokraj svake vode, i puštate volove i magarce.

< Yesaya 32 >