< Yesaya 26 >

1 Tsiku limenelo anthu a mʼdziko la Yuda adzayimba nyimbo iyi. Tili ndi mzinda wolimba. Mulungu amawuteteza ndi zipupa ndi malinga.
In that day this song will be sung in the land of Judah: We have a strong city; God has made salvation its walls and ramparts.
2 Tsekulani zipata za mzinda kuti mtundu wolungama ndi wokhulupirika ulowemo.
Open the gates, that the righteous nation that keeps faith may enter in.
3 Inu mudzamupatsa munthu wa mtima wokhazikika mtendere weniweni.
The mind that is stayed on you, you will keep him in perfect peace, for he trusts in you.
4 Mudalireni Yehova mpaka muyaya, chifukwa Yehova Mulungu ndiye Thanthwe losatha.
Trust in Yahweh forever; for in Yah, Yahweh, is an everlasting rock.
5 Iye amatsitsa anthu amene amadziyika pamwamba, iye amagwetsa pansi mzinda wodzitukumula, amagumula makoma ake ndi kuwagwetsa pansi pa fumbi penipeni.
For he will bring down those who live proudly; the fortified city he will lay low, he will lay low to the ground; he will level it to the dust.
6 Mapazi a anthu akuwupondereza, mapazi a anthu oponderezedwa, mapazi anthu osauka.
It will be trampled down by the feet of the poor and the treading of the needy.
7 Njira ya munthu wolungama ndi yosalaza, Inu Wolungamayo, mumasalaza njira ya wolungama.
The path of the righteous is level, Righteous One; the path of the righteous you make straight.
8 Inde Yehova, timayenda mʼnjira zanu zolungama, ife timayembekezera Inu; mitima yathu imakhumba kukumbukira ndi kulemekeza dzina lanu.
Yes, in the path of your judgments, Yahweh, we wait for you; your name and your reputation are our desire.
9 Moyo wanga umalakalaka Inu usiku wonse; nthawi yammawa ndimafunafuna Inu. Pamene muweruza dziko lapansi anthu amaphunzira kuchita chilungamo.
I have longed for you in the night; yes, my spirit within me seeks you earnestly. For when your judgments come on the earth, the inhabitants of the world learn about righteousness.
10 Ngakhale mukomere mtima anthu oyipa, saphunzira chilungamo. Amachita zoyipa mʼdziko la chilungamo, ndipo sazindikira ululu wa Yehova.
Let favor be shown to the wicked one, but he will not learn righteousness. In the land of uprightness he acts wickedly and does not see the majesty of Yahweh.
11 Inu Yehova, mwatukula dzanja lanu kuti muwalange, koma iwo sakuliona dzanjalo. Aloleni anthu aone ndi kuchita manyazi poona mmene mukondera anthu anu; ndipo moto umene mwasonkhera adani anu uwapsereze.
Yahweh, your hand is lifted up, but they do not notice. But they will see your zeal for the people and be put to shame, because fire of your adversaries will devour them.
12 Yehova, mumatipatsa mtendere; ndipo zonse zimene ife tinazichita munatichitira ndinu.
Yahweh, you will bring about peace for us; for indeed, you have also accomplished all our works for us.
13 Inu Yehova Mulungu wathu, ngakhale takhala tikulamulidwa ndi ena mʼmalo mwanu, koma ife timalemekeza dzina lanu lokha.
Yahweh our God, other masters besides you have ruled over us; but we praise your name alone.
14 Iwo tsopano sadzadzukanso; mizimu yawo sidzabwera kudzativutitsa pakuti mwawalanga ndipo mwawawononga; palibenso amene amawakumbukira.
They are dead, they will not live; they are deceased, they will not arise. Indeed, you came in judgment and destroyed them, and made every memory of them to perish.
15 Inu Yehova, mwaukulitsa mtundu wathu; mwauchulukitsa ndithu ndipo mwalandirapo ulemu; mwaukuza mbali zonse za dziko.
You have increased the nation, Yahweh, you have increased the nation; you are honored; you have extended all the borders of the land.
16 Yehova, anthu anu anabwera kwa Inu pamene anali mʼmasautso; pamene munawalanga, iwo anapemphera kwa Inu.
Yahweh, in trouble have they looked to you; they whispered prayers when your discipline was on them.
17 Monga mayi woyembekezera pamene nthawi yake yobereka yayandikira amamva kupweteka ndipo amalira ndi ululu, ifenso tinali chimodzimodzi pamaso panu, Inu Yehova.
As a pregnant woman nears the time for her to give birth, when she is in pain and cries out in her labor pains, so we have been before you, Lord.
18 Ife chimodzimodzi tinamva ululu, ngati mayi pa nthawi yobala mwana, koma sitinapindulepo kanthu, kapena kupulumutsa dziko lapansi; sitinabadwitse anthu atsopano pa dziko pano.
We have been pregnant, we have been in labor, but it is as if we have only given birth to wind. We have not brought salvation to the earth, and the inhabitants of the world have not fallen.
19 Koma anthu anu amene anafa adzakhalanso ndi moyo; matupi awo adzadzuka. Iwo amene ali ku fumbi tsopano adzadzuka ndi kuyimba mosangalala. Monga mame amafewetsa pansi kutsitsimutsa zomera, momwenso Yehova adzaukitsa anthu amene anafa kale.
Your dead will live; their dead bodies will arise. Awake and sing for joy, you who live in the dust; for your dew is the dew of light, and the earth will bring forth its dead.
20 Abale anga, pitani mukalowe mʼnyumba zanu ndipo mukadzitsekere; mukabisale kwa kanthawi kochepa mpaka ukali wake utatha.
Go, my people, enter into your rooms and shut your doors behind you; hide for a little while, until the indignation has passed by.
21 Taonani, Yehova akubwera kuchokera kumene amakhala; akubwera kudzalanga anthu a dziko lapansi chifukwa cha machimo awo. Dziko lapansi lidzawulula magazi amene anakhetsedwa pa dzikolo; dziko lapansi silidzabisanso mitembo ya anthu ophedwa.
For, look, Yahweh is about to come out of his place to punish the inhabitants of the earth for their iniquity; the earth will uncover her bloodshed, and will no longer conceal her slain.

< Yesaya 26 >