< Yesaya 20 >

1 Mʼchaka chimene mkulu wankhondo wotumidwa ndi mfumu ya ku Asiriya, anabwera ku Asidodi ndi kuwuthira nkhondo ndi kuwulanda,
In the yeer wherynne Tharthan entride in to Azotus, whanne Sargon, the kyng of Assiriens, hadde sent hym, and he hadde fouyte ayens Azotus, and hadde take it;
2 nthawi imeneyo Yehova anawuza Yesaya mwana wa Amozi kuti, “Pita kavule chiguduli ndi nsapato zako.” Ndipo iye anaterodi, ankangoyenda wamaliseche ndiponso wopanda nsapato.
in that tyme the Lord spak in the hond of Isaye, the sone of Amos, and seide, Go thou, and vnbynde the sak fro thi leendis, and take awei thi schoon fro thi feet. And he dide so, goynge nakid and vnschood.
3 Kenaka Yehova anati, “Monga momwe mtumiki wanga Yesaya wakhala akuyendera wamaliseche ndiponso wopanda nsapato kwa zaka zitatu ngati chizindikiro ndi chenjezo kwa dziko la Igupto ndi Kusi,
And the Lord seide, As my seruaunt Ysaie yede nakid and vnschood, a signe and greet wondur of thre yeer schal be on Egipt, and on Ethiopie;
4 momwemonso mfumu ya ku Asiriya idzatenga ukapolo anthu a ku Igupto ndi a ku Kusi, anyamata ndi okalamba. Iwo adzakhala amaliseche ndi opanda nsapato, matako ali pa mtunda. Zimenezi zidzachititsa manyazi Igupto.
so the kyng of Assiriens schal dryue the caitifte of Egipt, and the passyng ouer of Ethiopie, a yong man and an eld man, nakid and vnschood, with the buttokis vnhilid, to the schenschipe of Egipt.
5 Amene ankadalira Kusi, ndiponso amene ankadzitukumula chifukwa cha Igupto adzakhumudwa ndi kuchita manyazi.
And thei schulen drede, and schulen be schent of Ethiopie, her hope, and of Egipt, her glorie.
6 Tsiku limenelo anthu amene amakhala mʼmbali mwa nyanja adzati, ‘Taonani zomwe zawachitikira amene ife tinkawadalira, amene ife tinkathawirako kuti atithandize ndi kutipulumutsa kwa mfumu ya ku Asiriya! Nanga ife tidzapulumuka bwanji?’”
And a dwellere of this ile schal seie in that dai, This was our hope, to which we fledden for help, that thei schulden delyuere vs fro the face of the kyng of Assiryens; and hou moun we ascape?

< Yesaya 20 >