< Hoseya 5 >

1 “Ansembe inu, imvani izi! Inu Aisraeli, tcherani khutu! Inu nyumba yaufumu, mvetserani! Chiweruzo ichi ndi chotsutsa inu: Inu munali ngati msampha ku Mizipa, munali ngati ukonde woyalidwa pa phiri la Tabori.
Preestis, here ye this, and the hous of Israel, perseyue ye, and the hous of the kyng, herkne ye; for whi doom is to you, for ye ben maad a snare to lokyng afer, and as a net spred abrood on Thabor.
2 Owukira azama mʼmoyo wakupha, Ine ndidzawalanga onsewo.
And ye bowiden doun sacrifices in to depthe; and Y am the lernere of alle hem.
3 Ndimadziwa zonse za Efereimu; Aisraeli ndi osabisika kwa Ine. Efereimu wayamba tsopano kuchita zachiwerewere; Israeli wadziyipitsa.
Y knowe Effraym, and Israel is not hid fro me; for now Effraym dide fornicacioun, Israel is defoulid.
4 “Ntchito zawo siziwalola kubwerera kwa Mulungu wawo. Mʼmitima mwawo muli mzimu wachiwerewere; Iwo sadziwa Yehova.
Thei schulen not yiue her thouytis, that thei turne ayen to her God; for the spirit of fornicacioun is in the myddis of hem, and thei knewen not the Lord.
5 Kudzikuza kwa Israeli kwakhala umboni womutsutsa; Aisraeli, ngakhale Aefereimu, anagwa mʼmachimo awo; Yudanso anagwa nawo pamodzi.
And the boost of Israel schal answere in to the face therof, and Israel and Effraym schulen falle in her wickidnesse; also Judas schal falle with hem.
6 Pamene adzapita ndi nkhosa zawo ndi ngʼombe zawo kukapereka nsembe kwa Yehova, iwo sadzamupeza; Iye wawachokera.
In her flockis, and in her droues thei schulen go to seke the Lord, and thei schulen not fynde; he is takun awei fro hem.
7 Iwo ndi osakhulupirika kwa Yehova; amabereka ana amʼchigololo ndipo chikondwerero chawo cha mwezi watsopano chidzawawononga pamodzi ndi minda yawo.
Thei trespassiden ayens the Lord, for thei gendriden alien sones; now the monethe schal deuoure hem with her partis.
8 “Womba lipenga mu Gibeya, liza mbetete mu Rama. Fuwulani mfuwu wankhondo mu Beti-Aveni; iwe Benjamini tsogolera.
Sowne ye with a clarioun in Gabaa, with a trumpe in Rama; yelle ye in Bethauen, after thi bak, Beniamyn.
9 Efereimu adzasanduka bwinja pa tsiku la chilango. Ine ndikulengeza zomwe zidzachitikadi pakati pa mafuko a Israeli.
Effraym schal be in to desolacioun, in the dai of amendyng, and in the lynagis of Israel Y schewide feith.
10 Atsogoleri a Yuda ali ngati anthu amene amasuntha miyala ya mʼmalire. Ndidzawakhutulira ukali wanga ngati madzi a chigumula.
The princes of Juda ben maad as takynge terme; Y schal schede out on hem my wraththe as watir.
11 Efereimu waponderezedwa, akulangidwa chifukwa chotsatira mafano.
Effraym suffrith fals chalenge, and is brokun bi doom; for he bigan to go after filthis.
12 Ine ndili ngati njenjete kwa Efereimu, ngati chinthu chowola kwa anthu a ku Yuda.
And Y am as a mouyte to Effraym, and as rot to the hous of Juda.
13 “Efereimu ataona nthenda yake, ndi Yuda ataona zilonda zake, pamenepo Efereimu anatembenukira kwa Asiriya, ndipo anawatumizira mfumu yayikulu kudzawathandiza. Koma mfumuyo singathe kukuchizani, singathe kuchiritsa mabala anu.
And Effraym siy his sikenesse, and Judas siy his boond. And Effraym yede to Assur, and sente to the kyng veniere. And he mai not saue you, nether he mai vnbynde the boond fro you.
14 Pakuti Ine ndidzakhala ngati mkango kwa Efereimu. Ngati mkango wamphamvu kwa Yuda. Ndidzawakhadzula nʼkuchokapo; ndidzawatenga ndipo palibe amene adzawalanditse.
For Y am as a lionesse to Effraym, and as a whelp of a lioun to the hous of Juda.
15 Ndipo ndidzabwerera ku malo anga mpaka anthu anga atavomereza kulakwa kwawo. Ndipo iwo adzafunafuna nkhope yanga; mʼmasautso awo adzandifunitsitsa Ine.”
Y my silf schal take, and go, and take awei, and noon is that schal delyuere. I schal go, and turne ayen to my place, til ye failen, and seken my face.

< Hoseya 5 >