< Hoseya 5 >

1 “Ansembe inu, imvani izi! Inu Aisraeli, tcherani khutu! Inu nyumba yaufumu, mvetserani! Chiweruzo ichi ndi chotsutsa inu: Inu munali ngati msampha ku Mizipa, munali ngati ukonde woyalidwa pa phiri la Tabori.
"Listen to this, you priests. Listen, house of Israel, and give ear, house of the king. For the judgment is against you; for you have been a snare at Mizpah, and a net spread on Tabor.
2 Owukira azama mʼmoyo wakupha, Ine ndidzawalanga onsewo.
The rebels are deep in slaughter; but I discipline all of them.
3 Ndimadziwa zonse za Efereimu; Aisraeli ndi osabisika kwa Ine. Efereimu wayamba tsopano kuchita zachiwerewere; Israeli wadziyipitsa.
I know Ephraim, and Israel is not hidden from me; for now, Ephraim, you have played the prostitute. Israel is defiled.
4 “Ntchito zawo siziwalola kubwerera kwa Mulungu wawo. Mʼmitima mwawo muli mzimu wachiwerewere; Iwo sadziwa Yehova.
Their deeds won't allow them to turn to their God; for the spirit of prostitution is within them, and they do not know the LORD.
5 Kudzikuza kwa Israeli kwakhala umboni womutsutsa; Aisraeli, ngakhale Aefereimu, anagwa mʼmachimo awo; Yudanso anagwa nawo pamodzi.
The pride of Israel testifies to his face. Therefore Israel and Ephraim will stumble in their iniquity. Judah also will stumble with them.
6 Pamene adzapita ndi nkhosa zawo ndi ngʼombe zawo kukapereka nsembe kwa Yehova, iwo sadzamupeza; Iye wawachokera.
They will go with their flocks and with their herds to seek the LORD; but they won't find him. He has withdrawn himself from them.
7 Iwo ndi osakhulupirika kwa Yehova; amabereka ana amʼchigololo ndipo chikondwerero chawo cha mwezi watsopano chidzawawononga pamodzi ndi minda yawo.
They are unfaithful to the LORD; for they have borne illegitimate children. Now the new moon will devour them with their fields.
8 “Womba lipenga mu Gibeya, liza mbetete mu Rama. Fuwulani mfuwu wankhondo mu Beti-Aveni; iwe Benjamini tsogolera.
"Blow the cornet in Gibeah, and the trumpet in Ramah. Sound a battle cry at Beth Aven, behind you, Benjamin.
9 Efereimu adzasanduka bwinja pa tsiku la chilango. Ine ndikulengeza zomwe zidzachitikadi pakati pa mafuko a Israeli.
Ephraim will become a desolation in the day of rebuke. Among the tribes of Israel, I have made known that which will surely be.
10 Atsogoleri a Yuda ali ngati anthu amene amasuntha miyala ya mʼmalire. Ndidzawakhutulira ukali wanga ngati madzi a chigumula.
The princes of Judah are like those who remove a landmark. I will pour out my wrath on them like water.
11 Efereimu waponderezedwa, akulangidwa chifukwa chotsatira mafano.
Ephraim is oppressed, he is crushed in judgment; Because he is intent in his pursuit of idols.
12 Ine ndili ngati njenjete kwa Efereimu, ngati chinthu chowola kwa anthu a ku Yuda.
Therefore I am to Ephraim like a moth, and to the house of Judah like rottenness.
13 “Efereimu ataona nthenda yake, ndi Yuda ataona zilonda zake, pamenepo Efereimu anatembenukira kwa Asiriya, ndipo anawatumizira mfumu yayikulu kudzawathandiza. Koma mfumuyo singathe kukuchizani, singathe kuchiritsa mabala anu.
"When Ephraim saw his sickness, and Judah his wound, Then Ephraim went to Assyria, and sent to king Jareb: but he is not able to heal you, neither will he cure you of your wound.
14 Pakuti Ine ndidzakhala ngati mkango kwa Efereimu. Ngati mkango wamphamvu kwa Yuda. Ndidzawakhadzula nʼkuchokapo; ndidzawatenga ndipo palibe amene adzawalanditse.
For I will be to Ephraim like a lion, and like a young lion to the house of Judah. I myself will tear in pieces and go away. I will carry off, and there will be no one to deliver.
15 Ndipo ndidzabwerera ku malo anga mpaka anthu anga atavomereza kulakwa kwawo. Ndipo iwo adzafunafuna nkhope yanga; mʼmasautso awo adzandifunitsitsa Ine.”
I will go and return to my place, until they acknowledge their offense, and seek my face. In their affliction they will seek me earnestly."

< Hoseya 5 >