< Hoseya 4 >

1 Inu Aisraeli, imvani mawu a Yehova, chifukwa Yehova ali ndi mlandu ndi inu amene mumakhala mʼdzikoli: “Mʼdziko mwanu mulibe kukhulupirika, mulibe chikondi mulibe kulabadira za Mulungu.
Hear the word of the Lord, you children of Israel: for the Lord [has] a controversy with the inhabitants of the land, because there is no truth, nor mercy, nor knowledge of God in the land.
2 Muli kutemberera kokha, kunama ndi kupha. Kuba ndi kuchita chigololo; machimo achita kunyanya ndipo akungokhalira kuphana.
Cursing, and lying, and murder, and theft, and adultery abound in the land, and they mingle blood with blood.
3 Chifukwa chake dziko likulira ndipo onse amene amakhalamo akuvutika; zirombo zakuthengo ndi mbalame zamumlengalenga ndiponso nsomba zamʼnyanja zikufa.
Therefore shall the land mourn, and shall be diminished with all that dwell in it, with the wild beasts of the field, and the reptiles of the earth, and with the birds of the sky, and the fish of the sea shall fail:
4 “Koma wina asapeze mnzake chifukwa, wina aliyense asayimbe mlandu mnzake, pakuti anthu ako ali ngati anthu amene amayimba mlandu wansembe.
that neither any one may plead, nor any one reprove [another]; but my people are as a priest spoken against.
5 Mumapunthwa usana ndi usiku ndipo aneneri amapunthwa nanu pamodzi. Choncho ndidzawononga amayi anu.
Therefore they shall fall by day, and the prophet with you shall fall: I have compared your mother to night.
6 Anthu anga akuwonongeka chifukwa chosadziwa. “Pakuti mwakana kudziwa, Inenso ndidzakukanani monga ansembe anga; chifukwa mwayiwala lamulo la Mulungu wanu, Inenso ndidzayiwala ana anu.
My people are like as if they had no knowledge: because you have rejected knowledge, I will also reject you, that you shall not minister as priest to me: and [as] you has forgotten the law of your God, I also will forget your children.
7 Ansembe ankati akachuluka iwo ankandichimwiranso kwambiri; iwo anasinthanitsa ulemerero wawo ndi chinthu china chonyansa.
According to their multitude, so they sinned against me: I will turn their glory into shame.
8 Amalemererapo pa machimo a anthu anga ndipo amafunitsitsa kuti anthuwo azipitiriza kuchimwa.
They will devour the sins of my people, and will set their hearts on their iniquities.
9 Ndipo zidzakhala motere: zochitikira anthu ena, zidzachitikiranso ansembe. Ndidzawalanga onsewo chifukwa cha njira zawo, ndidzawabwezera chifukwa cha machitidwe awo.
And the priest shall be as the people: and I will avenge on them their ways, and I will recompense to them their counsels.
10 “Iwo azidzadya koma sadzakhuta; azidzachita zachiwerewere koma sadzachulukana, chifukwa anasiya Yehova kuti adzipereke
And they shall eat, and shall not be satisfied: they have gone a-whoring, and shall by no means prosper: because they have left off to take heed to the Lord.
11 ku zachiwerewere, ku vinyo wakale ndi watsopano, zimene zimachotsa nzeru zomvetsa zinthu
The heart of my people has gladly engaged in fornication and wine and strong drink.
12 za anthu anga. Anthu anga amapempha nzeru ku fano lamtengo ndipo ndodo yawo yamtengo imawayankha. Mzimu wachiwerewere umawasocheretsa; iwo sakukhulupirika kwa Mulungu wawo.
They asked counsel by [means of] signs, and they reported answer to them by their staves: they have gone astray in a spirit of whoredom, and gone grievously a-whoring from their God.
13 Amapereka nsembe pamwamba pa mapiri ndi kufukiza lubani pa zitunda, pa tsinde pa mtengo wa thundu, mnjale ndi mkundi, pamene pali mthunzi wabwino. Nʼchifukwa chake ana anu aakazi akuchita zachiwerewere ndipo akazi a ana anu akuchita zigololo.
They have sacrificed on the tops of the mountains, and on the hills they have sacrificed under the oak and poplar, and under the shady tree, because the shade was good: therefore your daughters shall go a-whoring, and your daughters-in-law shall commit adultery.
14 “Ine sindidzalanga ana anu aakazi pamene iwo adzachita zachiwerewere, kapena akazi a ana anu pamene adzachita zigololo. Paja inu nomwe amunanu mumayenda ndi akazi achiwerewere, ndipo mumapereka nsembe pamodzi ndi akazi achiwerewere a ku malo opembedzerako. Anthu amene alibe nzeru adzawonongeka ndithu!
And I will not visit upon your daughters when they shall commit fornication, nor your daughters-in-law when they shall commit adultery: for they themselves mingled themselves with harlots, and sacrificed with polluted ones, and the people that understood not entangled itself with a harlot.
15 “Ngakhale umachita chigololo, iwe Israeli, Yuda asapezeke ndi mlandu wotere. “Usapite ku Giligala. Usapite ku Beti-Aveni. Ndipo usalumbire kuti, ‘Pali Yehova wamoyo!’
But you, O Israel, be not ignorant, and go you not, [men of] Juda, to Galgala; and go not up to the house of On, and swear not by the living Lord.
16 Aisraeli ndi nkhutukumve, ngosamva ngati ana angʼombe. Kodi Yehova angathe kuwaweta bwanji ngati ana ankhosa pa msipu wabwino?
For Israel was maddened like a mad heifer: now the Lord will feed them as a lamb in a wide place.
17 Efereimu waphathana ndi mafano; mulekeni!
Ephraim, joined with idols, has laid stumbling blocks in his own way.
18 Ngakhale pamene zakumwa zawo zatha, amapitiriza kuchita zachiwerewere; atsogoleri awo amakonda kwambiri njira zawo zochititsa manyazi.
He has chosen the Chananites: they have grievously gone a-whoring: they have loved dishonour through her insolence.
19 Adzachotsedwa ndi kamvuluvulu ndipo adzachita manyazi chifukwa cha nsembe zawo.
You are a blast of wind in her wings, and they shall be ashamed because of their altars.

< Hoseya 4 >