< Hoseya 3 >

1 Yehova anati kwa ine, “Pita kamukondenso mkazi wako, ngakhale ali pa chibwenzi ndi wina ndi kuti ndi wachigololo. Mukonde iyeyo monga momwe Yehova amakondera Aisraeli, ngakhale iwo amapita kukapembedza milungu ina ndi kukonda nsembe za keke zamphesa zowuma.”
And Jehovah said to me, Go again, love a woman beloved of her friend, and an adulteress, even as Jehovah loves the sons of Israel, though they turn to other gods, and love cakes of raisins.
2 Motero ndinamukwatira popereka ndalama khumi ndi zisanu zasiliva, ndiponso mitanga isanu ndi iwiri ya barele.
So I bought her to me for fifteen pieces of silver, and a homer of barley, and a half-homer of barley.
3 Kenaka ndinamuwuza mkaziyo kuti, “Ukhale nane masiku ambiri; usachitenso zachiwerewere kapena chigololo ndi munthu wina, ndipo ine ndidzakhala nawe.”
And I said to her, Thou shall abide for me many days. Thou shall not play the harlot, and thou shall not be any man's wife. So I will also be toward thee.
4 Pakuti Aisraeli adzakhala masiku ambiri opanda mfumu kapena kalonga, osapereka nsembe kapena kuyimika miyala yachipembedzo, wopanda efodi kapena fano.
For the sons of Israel shall abide many days without king, and without ruler, and without sacrifice, and without pillar, and without ephod or teraphim.
5 Pambuyo pake Aisraeli adzabwerera ndi kufunafuna Yehova Mulungu wawo ndi Davide mfumu yawo. Adzabwera kwa Yehova akunjenjemera ndipo adzalandira madalitso mʼmasiku awo otsiriza.
Afterward the sons of Israel shall return and seek Jehovah their God and David their king, and shall come with fear to Jehovah and to his goodness in the latter days.

< Hoseya 3 >