< Hoseya 11 >

1 “Israeli ali mwana, ndinamukonda, ndipo ndinayitana mwana wanga kuti atuluke mu Igupto.
« Quand Israël était un enfant, je l'ai aimé, et a appelé mon fils hors d'Égypte.
2 Koma ndimati ndikamapitiriza kuyitana iwo amandithawa kupita kutali. Ankapereka nsembe kwa Abaala ndipo ankafukiza lubani kwa mafano.
Ils les ont appelés, et ils se sont éloignés d'eux. Ils sacrifiaient aux Baals, et brûlaient de l'encens à des images gravées.
3 Ndi Ine amene ndinaphunzitsa Efereimu kuyenda, ndipo ndinawagwira pa mkono; koma iwo sanazindikire kuti ndine amene ndinawachiritsa.
J'ai pourtant appris à Ephraïm à marcher. Je les ai pris par les bras, mais ils ne savaient pas que je les avais guéris.
4 Ndinawatsogolera ndi zingwe zachifundo cha anthu ndi zomangira za chikondi; ndinachotsa goli mʼkhosi mwawo ndipo ndinawerama nʼkuwadyetsa.
Je les ai tirés avec des cordes d'homme, avec des liens d'amour; et j'étais pour eux comme ceux qui soulèvent le joug sur leur cou; Je me suis penché vers lui et je l'ai nourri.
5 “Sadzabwerera ku Igupto, koma Asiriya ndiye adzakhala mfumu yawo pakuti akana kutembenuka.
« Ils ne retourneront pas dans le pays d'Égypte; mais l'Assyrien sera leur roi, parce qu'ils ont refusé de se repentir.
6 Malupanga adzangʼanima mʼmizinda yawo, ndipo adzawononga mipiringidzo ya zipata zawo nadzathetseratu malingaliro awo.
L'épée s'abattra sur leurs villes, et détruira les barreaux de leurs portes, et mettra fin à leurs plans.
7 Anthu anga atsimikiza zondifulatira Ine. Ngakhale atayitana Wammwambamwamba, sizidzatheka kuti Iye awakwezenso.
Mon peuple est décidé à se détourner de moi. Bien qu'ils appellent le Très-Haut, il ne les exaltera certainement pas.
8 “Kodi ndingakusiye bwanji iwe Efereimu? Kodi ndingakupereke bwanji iwe Israeli? Kodi ndingakuchitire bwanji zimene ndinachitira Adima? Kodi ndingathe bwanji kukuchitira zimene ndinachitira Zeboimu? Mtima wanga wakana kutero; chifundo changa chonse chikusefukira.
« Comment puis-je t'abandonner, Ephraïm? Comment puis-je te livrer, Israël? Comment puis-je faire en sorte que tu aimes Admah? Comment puis-je vous faire aimer Zeboiim? Mon cœur est retourné à l'intérieur de moi, ma compassion est éveillée.
9 Sindidzalola kuti ndikulange ndi mkwiyo wanga woopsa, kapena kutembenuka ndi kuwononga Efereimu. Pakuti Ine ndine Mulungu osati munthu, Woyerayo pakati panu. Sindidzabwera mwaukali.
Je n'exécuterai pas l'ardeur de ma colère. Je ne reviendrai pas pour détruire Ephraïm, car je suis Dieu, et non un homme, le Saint parmi vous. Je ne viendrai pas en colère.
10 Iwo adzatsatira Yehova; Iye adzabangula ngati mkango. Akadzabangula, ana ake adzabwera akunjenjemera kuchokera kumadzulo.
Ils marcheront après Yahvé, qui rugira comme un lion; car il rugira, et les enfants viendront en tremblant de l'ouest.
11 Adzabwera akunjenjemera ngati mbalame kuchokera ku Igupto, ngati nkhunda kuchokera ku Asiriya. Ine ndidzawakhazikanso mʼnyumba zawo,” akutero Yehova.
Ils sortiront d'Égypte en tremblant comme un oiseau, et comme une colombe du pays d'Assyrie; et je les installerai dans leurs maisons, dit Yahvé.
12 Efereimu wandizungulira ndi mabodza, nyumba ya Israeli yandizungulira ndi chinyengo. Ndipo Yuda wawukira Mulungu, wawukira ngakhale Woyerayo amene ndi wokhulupirika.
Ephraïm m'entoure de mensonges, et la maison d'Israël par la tromperie. Juda s'éloigne toujours de Dieu, et est infidèle au Saint.

< Hoseya 11 >