< Hoseya 11 >

1 “Israeli ali mwana, ndinamukonda, ndipo ndinayitana mwana wanga kuti atuluke mu Igupto.
When Israel was a child, then I loved him, and out of Egypt I called my son.
2 Koma ndimati ndikamapitiriza kuyitana iwo amandithawa kupita kutali. Ankapereka nsembe kwa Abaala ndipo ankafukiza lubani kwa mafano.
The more the prophets called them, the more they went from them. They sacrificed to the Baalim, and burned incense to graven images.
3 Ndi Ine amene ndinaphunzitsa Efereimu kuyenda, ndipo ndinawagwira pa mkono; koma iwo sanazindikire kuti ndine amene ndinawachiritsa.
Yet I taught Ephraim to walk. I took them on my arms, but they did not know that I healed them.
4 Ndinawatsogolera ndi zingwe zachifundo cha anthu ndi zomangira za chikondi; ndinachotsa goli mʼkhosi mwawo ndipo ndinawerama nʼkuwadyetsa.
I drew them with cords of a man, with bands of love, and I was to them as those who lift up the yoke on their jaws. And I laid food before them.
5 “Sadzabwerera ku Igupto, koma Asiriya ndiye adzakhala mfumu yawo pakuti akana kutembenuka.
They shall not return into the land of Egypt, but the Assyrian shall be their king, because they refused to return to me.
6 Malupanga adzangʼanima mʼmizinda yawo, ndipo adzawononga mipiringidzo ya zipata zawo nadzathetseratu malingaliro awo.
And the sword shall fall upon their cities, and shall consume their bars, and devour them, because of their own counsels.
7 Anthu anga atsimikiza zondifulatira Ine. Ngakhale atayitana Wammwambamwamba, sizidzatheka kuti Iye awakwezenso.
And my people are bent on backsliding from me. Though they call them to him who is on high, none at all will exalt him.
8 “Kodi ndingakusiye bwanji iwe Efereimu? Kodi ndingakupereke bwanji iwe Israeli? Kodi ndingakuchitire bwanji zimene ndinachitira Adima? Kodi ndingathe bwanji kukuchitira zimene ndinachitira Zeboimu? Mtima wanga wakana kutero; chifundo changa chonse chikusefukira.
How shall I give thee up, Ephraim? How shall I cast thee off, Israel? How shall I make thee as Admah? How shall I set thee as Zeboiim? My heart is turned within me. My compassions are kindled together.
9 Sindidzalola kuti ndikulange ndi mkwiyo wanga woopsa, kapena kutembenuka ndi kuwononga Efereimu. Pakuti Ine ndine Mulungu osati munthu, Woyerayo pakati panu. Sindidzabwera mwaukali.
I will not execute the fierceness of my anger. I will not return to destroy Ephraim. For I am God, and not man, the Holy One in the midst of thee, and I will not come in wrath.
10 Iwo adzatsatira Yehova; Iye adzabangula ngati mkango. Akadzabangula, ana ake adzabwera akunjenjemera kuchokera kumadzulo.
They shall walk after Jehovah, who will roar like a lion. For he will roar, and the sons shall come trembling from the west.
11 Adzabwera akunjenjemera ngati mbalame kuchokera ku Igupto, ngati nkhunda kuchokera ku Asiriya. Ine ndidzawakhazikanso mʼnyumba zawo,” akutero Yehova.
They shall come trembling as a bird out of Egypt, and as a dove out of the land of Assyria. And I will make them to dwell in their houses, says Jehovah.
12 Efereimu wandizungulira ndi mabodza, nyumba ya Israeli yandizungulira ndi chinyengo. Ndipo Yuda wawukira Mulungu, wawukira ngakhale Woyerayo amene ndi wokhulupirika.
Ephraim encompasses me around with falsehood, and the house of Israel with deceit, but Judah yet rules with God, and is faithful with the Holy One.

< Hoseya 11 >