< Habakuku 3 >

1 Pemphero la mneneri Habakuku potsata mayimbidwe a Sigionoti.
A prayer of Habakkuk the prophet, set to Shigionoth.
2 Inu Yehova, ndamva za kutchuka kwanu; Inu Yehova, ntchito zanu zandiopsa. Muzichitenso masiku athu ano, masiku athu ano zidziwike; mu ukali wanu mukumbukire kuchita chifundo.
O Jehovah, I have heard the report of thee, and am afraid. O Jehovah, revive thy work in the midst of the years. In the midst of the years make it known. In wrath remember mercy.
3 Mulungu anabwera kuchokera ku Temani, Woyerayo kuchokera ku Phiri la Parani. (Sela) Ulemerero wake unaphimba mlengalenga ndipo dziko lapansi linadzaza ndi matamando ake.
God came from Teman, and the Holy One from mount Paran. (Selah) His glory covered the heavens, and the earth was full of his praise.
4 Kuwala kwa ulemerero wake kunali ngati kutuluka kwa dzuwa; kunyezimira kunkatuluka mʼdzanja lake, mʼmene anabisamo mphamvu zake.
And his brightness was as the light. He had rays from his hand, and there was the hiding of his power.
5 Patsogolo pake pankagwa mliri; nthenda yoopsa inkagwa kumbuyo kwake.
Before him went the pestilence. And fiery bolts went forth at his feet.
6 Iye anayimirira ndi kugwedeza dziko lapansi; anayangʼana ndipo mitundu ya anthu inanjenjemera. Mapiri okhazikika anagumuka ndipo zitunda zakalekale zinatitimira. Njira zake ndi zachikhalire.
He stood, and measured the earth. He beheld, and drove apart the nations. And the eternal mountains were scattered. The everlasting hills bowed. His goings were as of old.
7 Ndinaona matenti a ku Kusani ali pa mavuto, mokhala a ku Midiyani muli ululu waukulu.
I saw the tents of Cushan in affliction. The curtains of the land of Midian trembled.
8 Inu Yehova, kodi munakwiyira mitsinje? Kodi munakalipira timitsinje? Kodi munapsera mtima nyanja pamene munakwera pa akavalo anu ndiponso magaleta anu achipulumutso?
Was Jehovah displeased with the rivers? Was thine anger against the rivers, or thy wrath against the sea, that thou rode upon thy horses, upon thy chariots of salvation?
9 Munasolola uta wanu mʼchimake, munayitanitsa mivi yambiri. (Sela) Munagawa dziko lapansi ndi mitsinje;
Thy bow was made quite bare. The oaths to the tribes were a sure word. (Selah) Thou split the earth with rivers.
10 mapiri anakuonani ndipo anagwedezeka. Madzi amphamvu anasefukira; nyanja yozama inakokoma ndipo mafunde ake anakwera kwambiri.
The mountains saw thee, and were afraid. The tempest of waters passed by. The deep uttered its voice, and lifted up its hands on high.
11 Dzuwa ndi mwezi zinayima chilili mlengalenga, pa kungʼanima kwa mivi yanu yowulukayo, pa kunyezimira kwa mkondo wanu.
The sun and moon stood still in their habitation, at the light of thine arrows as they went, at the shining of thy glittering spear.
12 Munayendayenda mʼdziko lapansi muli ndi ukali, ndipo munapondereza mitundu ya anthu muli ndi mkwiyo.
Thou marched though the land in indignation. Thou threshed the nations in anger.
13 Munapita kukalanditsa anthu anu, kukapulumutsa wodzozedwa wanu. Munakantha mtsogoleri wa dziko la anthu oyipa, munawononga anthu ake onse. (Sela)
Thou went forth for the salvation of thy people, for the salvation of thine anointed. Thou wound the head out of the house of the wicked man, laying bare the foundation even to the neck. (Selah)
14 Ndi mkondo wake womwe munalasa mtsogoleri wake pamene ankhondo ake anabwera mwamphamvu kudzatibalalitsa, ankasangalala ngati kuti akudzawononga osauka amene akubisala.
Thou pierced with his own staves the head of his warriors. They came as a whirlwind to scatter me. Their rejoicing was as to devour the poor man secretly.
15 Munapondaponda pa nyanja ndi akavalo anu, kuvundula madzi amphamvu.
Thou walked through the sea with thy horses, the heap of mighty waters.
16 Ndinamva ndipo mtima wanga unagunda kwambiri, milomo yanga inanjenjemera pakumva phokosolo; mafupa anga anaguluka, ndipo mawondo anga anawombana. Komabe ndikuyembekezera mofatsa, tsiku la masautso limene lidzafike pa mtundu wa anthu umene ukutithira nkhondo.
I heard, and my body trembled. My lips quivered at the voice. Rottenness enters into my bones, and I tremble in my place, because I must wait quietly for the day of trouble, for the coming up of the people who invade us.
17 Ngakhale mtengo wa mkuyu usachite maluwa, ndipo mipesa ikhale yopanda mphesa. Ngakhale mitengo ya olivi isabereke zipatso, ndipo mʼminda musatuluke kanthu. Ngakhale nkhosa ndi ngʼombe zithe mʼkhola,
For though the fig tree shall not flourish, nor shall fruit be in the vines; the labor of the olive shall fail, and the fields shall yield no food; the flock shall be cut off from the fold, and there shall be no herd in the stalls;
18 komabe ine ndidzakondwera mwa Yehova, ndidzasangalala mwa Mulungu Mpulumutsi wanga.
yet I will rejoice in Jehovah. I will joy in the God of my salvation.
19 Ambuye Yehova ndiye mphamvu yanga; amalimbitsa miyendo yanga ngati ya mbawala yayikazi, amandithandiza kukafika pamwamba pa phiri. Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za nsambo.
Jehovah, the Lord, is my strength. And he makes my feet like hinds' feet, and will make me to walk upon my high places.

< Habakuku 3 >