< Genesis 9 >

1 Ndipo Mulungu anadalitsa Nowa ndi ana ake aamuna nati kwa iwo, “Berekanani ndipo muchulukane ndi kudzaza dziko lapansi.
And God blessed Noe and his sons, and said to them, Increase and multiply, and fill the earth and have dominion over it.
2 Nyama zonse za dziko lapansi, ndi mbalame zonse za mlengalenga, ndi chamoyo chilichonse chokwawa, ndiponso nsomba zonse za ku nyanja; zidzakuopani ndipo ndazipereka kuti muzilamulire.
And the dread and the fear of you shall be upon all the wild beasts of the earth, on all the birds of the sky, and on all things moving upon the earth, and upon all the fishes of the sea, I have placed them under your power.
3 Tsopano chamoyo chilichonse chidzakhala chakudya chanu. Monga momwe ndinakupatsirani ndiwo zamasamba, tsopano ndikupatsaninso nyama iliyonse.
And every reptile which is living shall be to you for meat, I have given all things to you as the green herbs.
4 “Koma musamadye nyama imene ikanali ndi magazi oyenda.
But flesh with blood of life you shall not eat.
5 Aliyense wopha munthu adzaphedwa, nyama iliyonse yopha munthu idzaphedwa, munthu aliyense wopha munthu mnzake, adzaphedwa.
For your blood of your lives will I require at the hand of all wild beasts, and I will require the life of man at the hand of [his] brother man.
6 “Aliyense wopha munthu, adzaphedwanso ndi munthu; pakuti Mulungu analenga munthu mʼchifanizo chake.
He that sheds man's blood, instead of that blood shall his own be shed, for in the image of God I made man.
7 Inu muberekane ndi kuchulukana kuti mudzaze dziko lonse lapansi ndi kuligonjetsa.”
But do you increase and multiply, and fill the earth, and have dominion over it.
8 Mulungu anawuza Nowa ndi ana ake kuti,
And God spoke to Noe, and to his sons with him, saying,
9 “Tsopano Ine ndapangana ndi iwe ndi zidzukulu zako zamʼtsogolomo,
And behold I establish my covenant with you, and with your seed after you,
10 pamodzi ndi zamoyo zonse, mbalame, ziweto ndi nyama zonse za kuthengo, ndi zonse zimene zinatuluka mʼchombo pamodzi ndi iwe.
and with every living creature with you, of birds and of beasts, and with all the wild beasts of the earth, as many as are with you, of all that come out of the ark.
11 Pangano langa ndi ili: Ine ndilonjeza kuti sindidzawononganso zamoyo ndi madzi a chigumula. Chigumula sichidzawononganso dziko lapansi.”
And I will establish my covenant with you and all flesh shall not any more die by the water of the flood, and there shall no more be a flood of water to destroy all the earth.
12 Ndipo Mulungu anati, “Ine ndikupereka chizindikiro ichi cha pangano langa la pakati pa Ine ndi iwe, ana ako, zamoyo zonse, pamodzi ndi mibado ya mʼtsogolo.
And the Lord God said to Noe, This [is] the sign of the covenant which I set between me and you, and between every living creature which is with you for perpetual generations.
13 Ndayika utawaleza wanga mʼmitambo, ndipo chidzakhala chizindikiro cha pangano langa ndi dziko lapansi.
I set my bow in the cloud, and it shall be for a sign of covenant between me and the earth.
14 Nthawi zonse pakakhala mitambo mu mlengalenga ndipo utawaleza uwoneka,
And it shall be when I gather clouds upon the earth, that my bow shall be seen in the cloud.
15 ndizikumbukira pangano langa pakati pa Ine ndi inu ndi zolengedwa zonse. Madzi sadzakhalanso chigumula chowononga dziko lapansi.
And I will remember my covenant, which is between me and you, and between every living soul in all flesh, and there shall no longer be water for a deluge, so as to blot out all flesh.
16 Utawaleza ukamadzaoneka mʼmitambo, ndidzawuona ndi kukumbukira pangano losatha pakati pa Mulungu ndi zamoyo zonse pa dziko lapansi.”
And my bow shall be in the cloud, and I will look to remember the everlasting covenant between me and the earth, and between [every] living soul in all flesh, which is upon the earth.
17 Choncho Mulungu anati kwa Nowa, “Ichi ndiye chizindikiro cha pangano limene ndalichita pakati pa Ine ndi zamoyo zonse pa dziko lapansi.”
And God said to Noe, This [is] the sign of the covenant, which I have made between me and all flesh, which is upon the earth.
18 Ana aamuna a Nowa amene anatuluka mʼchombo muja anali Semu, Hamu ndi Yafeti. Hamu anali abambo ake a Kanaani.
Now the sons of Noe which came out of the ark, were Sem, Cham, Japheth. And Cham was father of Chanaan.
19 Ana aamuna a Nowa amenewa ndiwo anali makolo a anthu onse pa dziko lapansi.
These three are the sons of Noe, of these were men scattered over all the earth.
20 Nowa anali munthu woyamba kulima munda wamphesa.
And Noe began to be a husbandman, and he planted a vineyard.
21 Tsiku lina pamene Nowa anamwako vinyo wa zipatso za mʼmundawo analedzera ndipo anavula zovala zake zonse ndi kugona mu tenti yake ali maliseche.
And he drank of the wine, and was drunk, and was naked in his house.
22 Hamu, abambo ake a Kanaani ataona kuti abambo ake ali maliseche anakawuza abale ake awiri aja omwe anali panja.
And Cham the father of Chanaan saw the nakedness of his father, and he went out and told his two brothers without.
23 Koma Semu ndi Yafeti anatenga chofunda nachiyika pa mapewa awo; ndipo anayenda chamʼmbuyo naphimba umaliseche wa abambo awo. Anafulatira kuti asaone umaliseche wa abambo awo.
And Sem and Japheth having taken a garment, put it on both their backs and went backwards, and covered the nakedness of their father; and their face [was] backward, and they saw not the nakedness of their father.
24 Nowa atadzuka, kuledzera kutatha, ndikudziwa zimene mwana wake wamngʼono wamwamuna uja anamuchitira,
And Noe recovered from the wine, and knew all that his younger son had done to him.
25 anati, “Atembereredwe Kanaani! Adzakhala kapolo wa pansi kwenikweni kwa abale ake.”
And he said, Cursed be the servant Chanaan, a slave shall he be to his brethren.
26 Anatinso, “Atamandike Yehova, Mulungu wa Semu! Kanaani akhale kapolo wa Semu.
And he said, Blessed [be] the Lord God of Sem, and Chanaan shall be his bond-servant.
27 Mulungu akulitse dziko la Yafeti; Yafeti alandire madalitso pamodzi ndi Semu, ndipo Kanaani akhale kapolo wawo.”
May God make room for Japheth, and let him dwell in the habitations of Sem, and let Chanaan be his servant.
28 Chitatha chigumula, Nowa anakhala ndi moyo zaka 350.
And Noe lived after the flood three hundred and fifty years.
29 Anamwalira ali ndi zaka 950.
And all the days of Noe were nine hundred and fifty years, and he died.

< Genesis 9 >