< Genesis 50 >

1 Kenaka Yosefe anadzigwetsa pa nkhope ya abambo ake, nawapsompsona kwinaku akulira.
Which thing Joseph seiy, and felde on `the face of the fader, and wepte, and kiste hym;
2 Ndipo Yosefe analamula antchito ake a chipatala kuti akonze thupi la Israeli ndi mankhwala kuti lisawole. Kotero antchitowo anakonzadi thupilo.
and he comaundide hise seruauntis, lechis, that thei schulden anoynte the fadir with swete smellynge spiceries.
3 Antchito aja zinawatengera masiku 40 kuti akonze mtembo uja popeza ntchito ngati imeneyi inafunikira masiku monga amenewa. Ndipo Aigupto anamulira Yakobo kwa masiku makumi asanu ndi awiri.
While thei `filliden the comaundementis, fourti daies passiden, for this was the custom of deed bodies anoyntid; and Egipt biwepte hym seuenti daies.
4 Yosefe atatha kulira maliro a abambo ake, anayankhula kwa nduna za Farao nati, “Ngati mungandikomere mtima, chonde mundiyankhulire kwa Farao kumuwuza kuti,
And whanne the tyme of weiling was fillid, Joseph spak to the meyne of Farao, If Y haue founde grace in youre siyt, speke ye in the eeris of Farao; for my fadir chargide me,
5 ‘Abambo anga anandilumbiritsa ndipo anati, ‘Ndatsala pangʼono kumwalira, ukandiyike mʼmanda amene ndinakumba ndekha mʼdziko la Kanaani.’ Tsono mundilole ndikayike abambo anga, ndipo ndikabweranso.’”
and seide, Lo! Y die, thou schalt birie me in my sepulcre which Y diggide to me in the lond of Canaan; therfor Y schal stie that Y birie my fadir, and Y schal turne ayen.
6 Farao anati, “Pita ukayike abambo ako monga anakulumbiritsa kuti uchite.”
And Farao seide to hym, Stie, and birie thi fader, as thou art chargid.
7 Kotero Yosefe anapita kukayika abambo ake. Nduna zonse za Farao, akuluakulu a bwalo lake ndi akuluakulu a ku Igupto, anapita naye pamodzi.
And whanne `he stiede, alle the elde men of `the hous of Farao yeden with him, and alle the grettere men in birthe of the lond of Egipt; the hous of Joseph with her britheren,
8 Anapitanso onse a pa banja la Yosefe ndi abale ake ndi onse amene anali a pa banja la abambo ake. Ana awo okha, nkhosa ndi ngʼombe zinatsala ku Goseni
without litle children, and flockis, and grete beestis, whiche thei leften in the lond of Gessen, yeden with him.
9 Asilikali okwera pa magaleta ndi asilikali a pa akavalo anapita nayenso pamodzi. Linali gulu lalikulu.
And he hadde charis, and horsmen, and felouschip, and cumpany was maad not litil.
10 Atafika pa Goreni ha-Atadi, pafupi ndi Yorodani, anachita mwambo waukulu wa maliro. Choncho Yosefe analira maliro a abambo ake masiku asanu ndi awiri.
And thei camen to the cornfloor of Adad, which is set ouer Jordan, where thei maden the seruice of the deed bodi, with greet weilyng and strong, and fillide seuen daies.
11 Akanaani amene ankakhala ku Goreni ha-Atadi ataona mwambo wa maliro anati, “Aigupto ali ndi mwambo wa maliro a akulu.” Ndi chifukwa chake malo amenewo a pafupi ndi Yorodani amatchedwa Abeli-Mizraimu.
And whanne the dwellers of the lond of Canaan hadden seyn this, thei seiden, This is a greet weiling to Egipcians; and therfor thei clepiden the name of that place the weilyng of Egipt.
12 Choncho ana a Yakobo anachita monga momwe abambo awo anawalamula:
Therfor the sones of Jacob diden, as he hadde comaundid to hem;
13 Ndiye kuti ana a Yakobo anamunyamula kupita naye ku Kanaani kuti akamuyike mʼphanga limene lili mʼmunda wa Makipela pafupi ndi Mamre. Abrahamu anagula mundawo kwa Efroni Mhiti kuti pakhale manda.
and thei baren hym in to the lond of Canaan, and thei birieden hym in the double denne, which denne with the feeld Abraham hadde bouyt of Effron Ethei, ayens the face of Mambre, into possessioun of sepulcre.
14 Atatha kuyika abambo ake, Yosefe anabwerera ku Igupto, pamodzi ndi abale ake ndi onse amene anapita nawo kukayika abambo ake.
And Joseph turnede ayen in to Egipt with hise britheren and al the felouschipe, whanne the fadir was biried.
15 Abale ake a Yosefe ataona kuti abambo awo amwalira, anati, “Nanga tidzatani ngati Yosefe anatisungira mangawa nafuna kutibwezera pa zoyipa zonse zimene tinamuchitira?”
And whanne the fadir was deed, the britheren of Joseph dredden, and spaken togidere, lest perauenture he be myndeful of the wrong which he suffride, and yelde to vs al the yuel, that we diden.
16 Motero anatumiza mawu kwa Yosefe kuti, “Abambo anu anasiya malangizo asanafe nati:
And thei senten to hym, and seiden, Thi fadir comaundide to vs,
17 ‘Zimene mudzayenera kunena kwa Yosefe ndi izi: Ndikukupempha kuti uwakhululukire abale ako cholakwa chawo ndi machimo awo, popeza anakuchitira zoyipa.’ Ndiye tsopano chonde tikhululukireni zolakwa zimene ife akapolo a Mulungu wa abambo anu tinachita.” Yosefe atangomva mawu amenewa anayamba kulira.
bifore that he diede, that we schulden seie to thee these thingis bi hise wordis; Y beseche, that thou foryete the wickidnesse of thi britheren, and the synne, and malice which thei hauntiden ayens thee; also we preien, that thou foryyue this wickidnesse to thi fadir, the seruaunt of God. Whanne these thingis weren herd, Joseph wepte.
18 Kenaka abale ake anabwera nadzigwetsa pansi pamaso pake, nati, “Ife ndife akapolo anu.”
And hise britheren camen to hym, and worschipiden lowe to erthe, and seiden, We ben thi seruauntis.
19 Koma Yosefe anawawuza kuti, “Musachite mantha. Kodi ine ndalowa mʼmalo mwa Mulungu?
To whiche he answeride, Nyle ye drede; whether we moun ayenstonde Goddis wille?
20 Inu munafuna kundichitira zoyipa, koma Mulungu anasandutsa zoyipazo kuti zikhale zabwino kuti zikwaniritsidwe zimene zikuchitika panozi, zopulumutsa miyoyo yambiri.
Ye thouyten yuel of me, and God turnede it in to good, that he schulde enhaunse me, as ye seen in present tyme, and that he schulde make saaf many puplis;
21 Kotero, musachite mantha. Ine ndidzasamalira inu pamodzi ndi ana anu omwe.” Tsono iye anawalimbitsa mtima powayankhula moleza mtima.
nyle ye drede, Y schal fede you and youre litle children. And he coumfortide hem, and spak swetli, and liytly;
22 Yosefe anakhala mu Igupto pamodzi ndi banja lonse la abambo ake. Anakhala ndi moyo zaka 110
and he dwellide in Egipt, with al the hows of his fadir. And he lyuyde an hundrid yeer,
23 ndipo anaona mʼbado wachitatu wa ana a Efereimu. Yosefe anatenganso ana a Makiri, mwana wa Manase kukhala ngati ana a mʼbanja lake.
and he seiy the sones of Effraym til to the thridde generacioun; also the sones of Machir, son of Manasses, weren borun in the knees of Joseph.
24 Kenaka Yosefe anati kwa abale ake, “Ine ndatsala pangʼono kufa. Koma mosakayika Mulungu adzakuyangʼanirani nadzakutengani kukutulutsani mʼdziko lino kupita ku dziko limene Iye analonjeza kwa Abrahamu, Isake ndi Yakobo.”
Whanne these thingis weren don, Joseph spak to hise brithren, Aftir my deeth God schal visite you, and he schal make to stie fro this lond to the loond which he swoor to Abraham, Ysaac, and Jacob.
25 Ndipo Yosefe analumbiritsa ana a Israeli lumbiro nati, “Lonjezani kuti Mulungu akadzakusungani mudzanyamula mafupa anga kuwachotsa ku malo kuno.”
And whanne he hadde chargid hem, and hadde seid, God schal visite you, bere ye out with you my boonus fro this place,
26 Choncho Yosefe anafa ali ndi zaka 110. Motero iwo atakonza thupi lake ndi mankhwala kuti lisawole, analiyika mʼbokosi ku Igupto.
he diede, whanne an hundrid and ten yeeris of his lijf weren fillid; and he was anoyntid with swete smellynge spiceries, and was kept in a beere in Egipt.

< Genesis 50 >