< Genesis 5 >

1 Ndondomeko ya mibado ya Adamu ndi iyi: Pamene Mulungu analenga munthu, anamulenga mʼchifaniziro cha Mulungu.
This is the book of the generations of Adam. In the day that God created man, he made him in God’s likeness.
2 Iye analenga mwamuna ndi mkazi. Anawadalitsa ndipo anawatcha “Munthu.”
He created them male and female, and blessed them. On the day they were created, he named them Adam.
3 Pamene Adamu anali ndi zaka 130, anabereka mwana wamwamuna wofanana naye ndipo anamutcha Seti.
Adam lived one hundred and thirty years, and became the father of a son in his own likeness, after his image, and named him Seth.
4 Atabadwa Seti, Adamu anakhala ndi moyo zaka zina 800 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
The days of Adam after he became the father of Seth were eight hundred years, and he became the father of other sons and daughters.
5 Zaka zonse za Adamu zinali 930 ndipo anamwalira.
All the days that Adam lived were nine hundred and thirty years, then he died.
6 Pamene Seti anali ndi zaka 105, anabereka Enosi.
Seth lived one hundred and five years, then became the father of Enosh.
7 Atabadwa Enosi, Seti anakhala ndi moyo zaka zina 807 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
Seth lived after he became the father of Enosh eight hundred and seven years, and became the father of other sons and daughters.
8 Zaka zonse za Seti zinali 912 ndipo anamwalira.
All of the days of Seth were nine hundred and twelve years, then he died.
9 Pamene Enosi anali ndi zaka 90, anabereka Kenani.
Enosh lived ninety years, and became the father of Kenan.
10 Atabadwa Kenani, Enosi anakhala ndi moyo zaka zina 815 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
Enosh lived after he became the father of Kenan eight hundred and fifteen years, and became the father of other sons and daughters.
11 Zaka zonse za Enosi pamodzi zinali 905 ndipo anamwalira.
All of the days of Enosh were nine hundred and five years, then he died.
12 Pamene Kenani anali ndi zaka 70, anabereka Mahalaleli.
Kenan lived seventy years, then became the father of Mahalalel.
13 Atabadwa Mahalaleli, Kenani anakhala ndi moyo zaka zina 840 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
Kenan lived after he became the father of Mahalalel eight hundred and forty years, and became the father of other sons and daughters
14 Zaka zonse za Kenani zinali 910, ndipo anamwalira.
and all of the days of Kenan were nine hundred and ten years, then he died.
15 Pamene Mahalaleli anali ndi zaka 65, anabereka Yaredi.
Mahalalel lived sixty-five years, then became the father of Jared.
16 Atabadwa Yaredi, Mahalaleli anakhala ndi moyo zaka zina 830 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
Mahalalel lived after he became the father of Jared eight hundred and thirty years, and became the father of other sons and daughters.
17 Zaka zonse za Mahalaleli zinali 895 ndipo anamwalira.
All of the days of Mahalalel were eight hundred and ninety-five years, then he died.
18 Pamene Yaredi anali ndi zaka 162, anabereka Enoki.
Jared lived one hundred and sixty-two years, then became the father of Enoch.
19 Atabadwa Enoki, Yaredi anakhala ndi moyo zaka zina 800 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
Jared lived after he became the father of Enoch eight hundred years, and became the father of other sons and daughters.
20 Zaka zonse za Yaredi zinali 962 ndipo anamwalira.
All of the days of Jared were nine hundred and sixty-two years, then he died.
21 Pamene Enoki anali ndi zaka 65, anabereka Metusela.
Enoch lived sixty-five years, then became the father of Methuselah.
22 Atabadwa Metusela, Enoki anayenda ndi Mulungu zaka 300 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
After Methuselah’s birth, Enoch walked with God for three hundred years, and became the father of more sons and daughters.
23 Zaka zonse za Enoki zinali 365.
All the days of Enoch were three hundred and sixty-five years.
24 Enoki anayenda ndi Mulungu; ndipo iye sanaonekenso chifukwa Mulungu anamutenga.
Enoch walked with God, and he was not found, for God took him.
25 Pamene Metusela anali ndi zaka 187, anabereka Lameki.
Methuselah lived one hundred and eighty-seven years, then became the father of Lamech.
26 Ndipo atabadwa Lameki, Metusela anakhala ndi moyo zaka zina 782 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
Methuselah lived after he became the father of Lamech seven hundred and eighty-two years, and became the father of other sons and daughters.
27 Zaka zonse za Metusela zinali 969, ndipo anamwalira.
All the days of Methuselah were nine hundred and sixty-nine years, then he died.
28 Pamene Lameki anali ndi zaka 182, anabereka mwana wamwamuna.
Lamech lived one hundred and eighty-two years, then became the father of a son.
29 Ndipo anamutcha Nowa ndipo anati, “Iyeyu adzatipumulitsa ku ntchito zathu zolemetsazi, zolima nthaka imene Yehova anayitemberera.”
He named him Noah, saying, “This one will comfort us in our work and in the toil of our hands, caused by the ground which the LORD has cursed.”
30 Atabadwa Nowa, Lameki anakhala zaka zina 595 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
Lamech lived after he became the father of Noah five hundred and ninety-five years, and became the father of other sons and daughters.
31 Zaka zonse za Lameki zinali 777, ndipo kenaka anamwalira.
All the days of Lamech were seven hundred and seventy-seven years, then he died.
32 Pamene Nowa anali ndi zaka 500, anabereka Semu, Hamu ndi Yafeti.
Noah was five hundred years old, then Noah became the father of Shem, Ham, and Japheth.

< Genesis 5 >